< Mateyu 23 >
1 Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake:
Alors Jésus, parlant à la foule et à ses disciples,
2 “Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose.
dit: Les scribes et les pharisiens sont assis sur le siège de Moïse.
3 Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa.
Tout ce qu'ils vous disent d'observer, observez-le et faites-le; mais ne faites pas leurs œuvres, car ils disent et ne font pas.
4 Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.
Car ils lient des fardeaux lourds et pénibles à porter, et les mettent sur les épaules des hommes; mais eux-mêmes ne lèvent pas le petit doigt pour les aider.
5 “Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo.
Mais ils font toutes leurs œuvres pour être vus des hommes. Ils élargissent leurs phylactères et agrandissent les franges de leurs vêtements,
6 Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge.
ils aiment les places d'honneur dans les fêtes, les meilleures places dans les synagogues,
7 Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’
les salutations sur les places publiques, et être appelés par les hommes « Rabbi, Rabbi".
8 “Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale.
Mais vous ne devez pas être appelés « Rabbi », car un seul est votre maître, le Christ, et vous êtes tous frères.
9 Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba.
N'appelez aucun homme sur la terre votre père, car un seul est votre Père, celui qui est dans les cieux.
10 Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu.
Ne vous faites pas appeler maîtres, car un seul est votre maître, le Christ.
11 Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani.
Mais celui qui est le plus grand parmi vous sera votre serviteur.
12 Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.
Quiconque s'élèvera sera abaissé, et quiconque s'abaissera sera élevé.
13 “Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe.
« Malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous dévorez les maisons des veuves, et, pour faire semblant, vous faites de longues prières. C'est pourquoi vous recevrez une plus grande condamnation.
14 Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.
« Mais malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous fermez le Royaume des cieux aux hommes; vous n'entrez pas vous-mêmes, et vous ne permettez pas à ceux qui entrent d'entrer.
15 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna )
Malheur à vous, scribes et pharisiens hypocrites! Car vous parcourez la mer et la terre pour faire un seul prosélyte; et quand il le devient, vous en faites un fils de la géhenne deux fois plus que vous. (Geenna )
16 “Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
« Malheur à vous, guides aveugles, qui dites: 'Celui qui jure par le temple n'est rien; mais celui qui jure par l'or du temple s'oblige'.
17 Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo?
Insensés aveugles! Car lequel est le plus grand, l'or ou le temple qui sanctifie l'or?
18 Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
Et: « Si quelqu'un jure par l'autel, il n'est rien; mais si quelqu'un jure par le don qui est sur l'autel, il est obligé ».
19 Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo?
Bande d'aveugles! Car lequel est le plus grand, le don ou l'autel qui sanctifie le don?
20 Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo.
Celui donc qui jure par l'autel, jure par lui et par tout ce qui est dessus.
21 Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo.
Celui qui jure par le temple, jure par lui et par celui qui l'a habité.
22 Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.
Celui qui jure par le ciel, jure par le trône de Dieu et par celui qui y est assis.
23 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo.
« Malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous payez la dîme de la menthe, de l'aneth et du cumin, et vous avez négligé les choses les plus graves de la loi: la justice, la miséricorde et la foi. Or, vous auriez dû faire ces choses-là, et ne pas laisser les autres en suspens.
24 Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.
Guides aveugles, vous poussez le moucheron et vous avalez le chameau!
25 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa.
« Malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous nettoyez le dehors de la coupe et du plat, mais au dedans ils sont pleins de rapines et d'iniquités.
26 Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.
Pharisien aveugle, nettoie d'abord le dedans de la coupe et du plat, afin que le dehors devienne pur lui aussi.
27 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse.
« Malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous êtes semblables à des tombeaux blanchis, qui paraissent beaux au dehors, mais qui, au dedans, sont pleins d'ossements de morts et de toute espèce d'impuretés.
28 Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.
De même, vous aussi, au dehors, vous paraissez justes aux yeux des hommes, mais, au dedans, vous êtes pleins d'hypocrisie et d'iniquité.
29 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama.
« Malheur à vous, scribes et pharisiens, hypocrites! Car vous bâtissez les tombeaux des prophètes et vous décorez les tombeaux des justes,
30 Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’
et vous dites: « Si nous avions vécu du temps de nos pères, nous n'aurions pas participé avec eux au sang des prophètes ».
31 Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.
Vous vous rendez donc témoignage à vous-mêmes que vous êtes les enfants de ceux qui ont tué les prophètes.
32 Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!
Remplissez donc la mesure de vos pères.
33 “Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna )
Serpents, rejetons de vipères, comment échapperez-vous au jugement de la géhenne? (Geenna )
34 Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina.
C'est pourquoi voici que je vous envoie des prophètes, des sages et des scribes. Vous tuerez et crucifierez les uns, vous flagellerez les autres dans vos synagogues et vous les persécuterez de ville en ville,
35 Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu.
afin que retombe sur vous tout le sang innocent versé sur la terre, depuis le sang d'Abel le juste jusqu'au sang de Zacharie, fils de Barachie, que vous avez tué entre le sanctuaire et l'autel.
36 Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.
En vérité, je vous le dis, toutes ces choses arriveront à cette génération.
37 “Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune.
« Jérusalem, Jérusalem, qui tue les prophètes et lapide ceux qui lui sont envoyés! Combien de fois ai-je voulu rassembler tes enfants, comme une poule rassemble ses poussins sous ses ailes, et tu n'as pas voulu!
38 Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja.
Voici, ta maison te sera laissée déserte.
39 Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’”
Car, je vous le dis, vous ne me verrez plus désormais, jusqu'à ce que vous disiez: « Béni soit celui qui vient au nom du Seigneur! »".