< Mateyu 23 >
1 Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake:
Tedy Ježíš mluvil zástupům a učedlníkům svým,
2 “Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose.
Řka: Na stolici Mojžíšově posadili se zákoníci a farizeové.
3 Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa.
Protož všecko, což by koli rozkázali vám zachovávati, zachovávejte a čiňte, ale podle skutků jejich nečiňte; neboť praví, a nečiní.
4 Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.
Svazujíť zajisté břemena těžká a nesnesitelná, a vzkládají na ramena lidská, ale prstem svým nechtí jimi ani pohnouti.
5 “Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo.
A všeckyť ty své skutky činí, aby byli vidíni od lidí. Rozšiřují zajisté nápisy své a veliké dělají podolky pláštů svých,
6 Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge.
A milují přední místa na večeřích, a první stolice v školách,
7 Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’
A pozdravování na trhu, a aby byli nazýváni od lidí: Mistři, mistři.
8 “Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale.
Ale vy nebývejte nazýváni mistři; nebo jeden jest Mistr váš, totiž Kristus, vy pak všickni bratří jste.
9 Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba.
A otce nenazývejte sobě na zemi; nebo jeden jest Otec váš, kterýž jest v nebesích.
10 Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu.
Ani se nazývejte vůdcové; nebo jeden jest vůdce váš Kristus.
11 Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani.
Ale kdo z vás větší jest, budeť služebníkem vaším.
12 Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.
Nebo kdož by se sám povyšoval, bude ponížen; a kdož by se ponížil, bude povýšen.
13 “Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe.
Ale běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, že zavíráte království nebeské před lidmi; nebo sami tam nevcházíte, ani těm, jenž by vjíti chtěli, vcházeti dopouštíte.
14 Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, že zžíráte domy vdovské, za příčinou dlouhého modlení; protož těžší soud ponesete.
15 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna )
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, že obcházíte moře i zemi, abyste učinili jednoho novověrce, a když bude učiněn, učiníte jej syna zatracení, dvakrát více, nežli jste sami. (Geenna )
16 “Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
Běda vám, vůdcové slepí, kteříž říkáte: Přisáhl-li by kdo skrze chrám, to nic není; ale kdo by přisáhl skrze zlato chrámové, povinenť jest přísaze dosti činiti.
17 Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo?
Blázni a slepci; nebo co jest většího, zlato-li, čili chrám, kterýž posvěcuje zlata?
18 Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
A přisáhl-li by kdo skrze oltář, nic není; ale kdo by přisáhl skrze ten dar, kterýž jest na něm, povinen jest.
19 Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo?
Blázni a slepci, i co jest většího, dar-li, čili oltář, kterýž posvěcuje daru?
20 Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo.
A protož kdokoli přisahá skrze oltář, přisahá skrze něj, i skrze to všecko, což na něm jest.
21 Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo.
A kdož přisahá skrze chrám, přisahá skrze něj, i skrze toho, kterýž přebývá v něm.
22 Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.
A kdož přisahá skrze nebe, přisahá skrze trůn Boží, i skrze toho, kterýž na něm sedí.
23 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo.
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, že dáváte desátky z máty a z kopru a z kmínu, a opouštíte to, což těžšího jest v Zákoně, totiž soud a milosrdenství a věrnost. Tyto věci měli jste činiti a oněch neopouštěti.
24 Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.
Vůdcové slepí, kteříž cedíte komára, velblouda pak požíráte.
25 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa.
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, že čistíte po vrchu konvice a mísy, a vnitř plno jest loupeže a nestředmosti.
26 Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.
Farizee slepče, vyčisť prve to, což vnitř jest v konvi a v míse, aby i to, což jest zevnitř, bylo čisto.
27 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse.
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, nebo jste se připodobnili hrobům zbíleným, kteříž ač se zdadí zevnitř krásní, ale vnitř jsou plní kostí umrlčích i vší nečistoty.
28 Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.
Tak i vy zevnitř zajisté zdáte se lidem spravedliví, ale vnitř plní jste pokrytství a nepravosti.
29 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama.
Běda vám, zákoníci a farizeové pokrytci, neboť vzděláváte hroby proroků a ozdobujete hroby spravedlivých,
30 Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’
A říkáte: Kdybychom byli za dnů otců našich, nebyli bychom účastníci jejich ve krvi proroků.
31 Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.
Protož osvědčujete sami proti sobě, že jste synové těch, kteříž proroky zmordovali.
32 Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!
I vy také naplňte míru otců svých.
33 “Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna )
Hadové, plémě ještěrčí, i jakž byste ušli odsudku do pekelného ohně? (Geenna )
34 Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina.
Protož aj, já posílám k vám proroky a moudré a učitele, a vy z těch některé zmordujete a ukřižujete, a některé z nich bičovati budete v školách vašich, a budete je honiti z města do města,
35 Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu.
Aby přišla na vás všeliká krev spravedlivá, vylitá na zemi, od krve Abele spravedlivého, až do krve Zachariáše syna Barachiášova, kteréhož jste zabili mezi chrámem a oltářem.
36 Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.
Amen pravím vám: Přijdou tyto všecky věci na pokolení toto.
37 “Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune.
Jeruzaléme, Jeruzaléme, mordéři proroků, a kterýž kamenuješ ty, jenž byli k tobě posíláni, kolikrát jsem chtěl shromážditi dítky tvé, tak jako slepice shromažďuje kuřátka svá pod křídla, a nechtěli jste.
38 Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja.
Aj, zanecháváť se vám dům váš pustý.
39 Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’”
Neboť pravím vám, že mne již více nikoli neuzříte od této chvíle, až i díte: Požehnaný, jenž se béře ve jménu Páně.