< Mateyu 22 >

1 Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
Ježíš jim vyprávěl další příběh:
2 “Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
„Když Bůh nabízí účast ve svém království, je jako král, který připravil velkou hostinu při svatbě svého syna.
3 Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
Pozvaných bylo mnoho, ale když pro ně přišli královi poslové, odmítli pozvání.
4 “Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
Král k nim poslal ještě jednou se vzkazem: ‚Je pro vás připravena bohatá hostina, přijďte!‘
5 “Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
Ale pozvaní to vůbec nebrali vážně. Jeden šel za prací na své pole, jiný za obchodem, někteří se dokonce králových poslů zmocnili, ztýrali je a několik jich zabili.
6 Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
7 Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
To krále popudilo, poslal vojsko, dal ty ukrutníky pobít a město vypálit.
8 “Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
Potom řekl svým poslům: ‚Hostina je připravena, ale svatební hosté jí nebyli hodni.
9 Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
Jděte na rozcestí a pozvěte na svatbu každého, koho potkáte.‘
10 Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
Poslové tedy šli a přivedli všechny, které našli, ubohé i slušné, takže svatební síň se zaplnila.
11 “Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
Když vstoupil král, aby hosty přivítal, uviděl jednoho, který nepřijal svatební oděv.
12 Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
Řekl mu: ‚Člověče, jak jsi se odvážil vejít bez svatebních šatů?‘On mlčel.
13 “Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
Král pak rozkázal sluhům: ‚Svažte ho a vyhoďte ven do tmy, kde bude jen nářek a utrpení.
14 “Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
Mnoho je pozvaných, ale těch, kteří skutečně vejdou, je málo.‘“
15 Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
Farizejové se sešli, aby se domluvili na taktice, jak Ježíše chytit do léčky. Chtěli ho vyprovokovat k slovům, kterých by pak mohli použít k obžalobě.
16 Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
Poslali k němu své žáky spolu s Herodovými stoupenci a ti řekli: „Mistře, víme, že jsi čestný a že pravdivě učíš cestě k Bohu, bez ohledu na to, jaké kdo má postavení.
17 Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
Řekni nám: Je správné odvádět římské vládě daň?“
18 Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
Ježíš však prohlédl jejich zlý úmysl. „Vy pokrytci!“zvolal. „Proč se mne snažíte nachytat takovými otázkami?
19 Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
Ukažte mi minci!“Oni mu podali denár.
20 ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
„Čí obraz a jméno je na něm vyraženo?“
21 Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.” Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”
„Císaře, “odpověděli. On jim na to řekl: „Co je tedy císařovo, dávejte císaři, a co je Boží, dávejte Bohu.“
22 Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
Zaskočeni tou odpovědí, odešli.
23 Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
Také za ním přišli saducejové, kteří tvrdí, že vzkříšení z mrtvých je nemožné. Předložili mu nepravděpodobný příběh:
24 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
„Mistře, v Mojžíšově zákoně čteme, že svobodný švagr je povinen vzít si bezdětnou vdovu po svém bratru, aby v dětech zachoval bratrovo jméno.
25 Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
U nás se vyskytl tento případ: Bylo sedm bratrů. První z nich se oženil a potom jako bezdětný zemřel, takže jeho žena se stala manželkou druhého bratra.
26 Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
Tento bratr také zemřel bez dětí, a tak se opakovalo u druhého, třetího – a nakonec u všech sedmi bratrů.
27 Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
Poslední ze všech zemřela i ta žena.
28 Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
Kterému z těch bratrů bude patřit po vzkříšení? Byla přece manželkou všech sedmi!“
29 Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
Ježíš odpověděl: „Mluvíte nesmysly, protože neznáte ani Písmo ani Boží moc.
30 Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
Po vzkříšení zaniknou tělesné vztahy. Lidé nebudou žít v manželství, ale budou tvořit Boží rodinu.
31 Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
A pokud jde o vzkříšení z mrtvých, pak čtěte pozorně Písmo. Jak nazývá Bůh sám sebe?
32 ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
Bůh Abrahamův, Izákův a Jákobův. On není Bohem mrtvých, ale živých.“
33 Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
Tyto Ježíšovy odpovědi udělaly na lidi hluboký dojem.
34 Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
Farizejové se doslechli, jak Ježíš umlčel saduceje.
35 Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
Pověřili jednoho ze svých vykladačů Písma, aby ho vyzkoušel:
36 “Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
„Mistře, které přikázání je v zákoně nejvýznamnější?“
37 Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
Ježíš mu odpověděl: „ ‚Miluj Pána, svého Boha, celým srdcem, duší i myslí.‘
38 Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
To je první a nejdůležitější přikázání.
39 Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
Druhé v pořadí důležitosti je toto: ‚Miluj svého bližního jako sám sebe.‘
40 Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
Na těch dvou přikázáních stojí celý Mojžíšův zákon a odkaz proroků.“
41 Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
Potom Ježíš, obklopen farizeji, se jich zeptal:
42 “Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”
„Co si myslíte o Kristu? Čí je to syn?“Odpověděli: „Davidův.“
43 Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
On na to řekl: „Jak by mohl David svého vlastního potomka nazývat Pánem? Vždyť o něm z podnětu Ducha svatého píše v žalmu:
44 “Ambuye anati kwa Ambuye wanga: ‘Khala pa dzanja langa lamanja mpaka ndiyike adani ako pansi pa mapazi ako.’
‚Bůh řekl mému Pánu: Seď po mé pravici, dokud ti nepodložím tvé nepřátele k nohám.‘
45 Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
Jestliže ho tedy David nazývá svým Pánem, jak může být jeho synem?“
46 Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.
Na to nikdo nedovedl odpovědět a už se mu neodvážili klást další otázky.

< Mateyu 22 >