< Mateyu 20 >
1 “Ufumu wakumwamba uli ngati mwini munda amene anapita mmawa kukalemba anthu aganyu kuti akagwire ntchito mʼmunda wake wa mpesa.
"For the Kingdom of the Heavens is like an employer who went out early in the morning to hire men to work in his vineyard,
2 Anagwirizana kuwalipira dinari monga malipiro a tsiku limodzi ndipo anawatumiza mʼmunda wake wamphesa.
and having made an agreement with them for a shilling a day, sent them into his vineyard.
3 “Nthawi 9 koloko mmawa, anatulukanso naona ena atayimirira pa msika akungokhala.
About nine o'clock he went out and saw others loitering in the market-place.
4 Anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa, ndipo ndidzakulipirani malipiro oyenera.’
To these also he said, "'You also, go into the vineyard, and whatever is right I will give you.'
5 Ndipo anapita. “Anatulukanso nthawi ya 12 koloko masana, ndi nthawi ya 3 koloko masananso nachita chimodzimodzi.
"So they went. Again about twelve, and about three o'clock, he went out and did the same.
6 Nthawi ya 5 koloko madzulo anatulukanso ndipo anapeza enanso atangoyimirira. Anawafunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mukungoyimirira pano tsiku lonse osagwira ntchito?’
And going out about five o'clock he found others loitering, and he asked them, "'Why have you been standing here all day long, doing nothing?'
7 “Iwo anayankha kuti, ‘Chifukwa palibe munthu amene watilemba ganyu.’ “Iye anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa.’
"'Because no one has hired us,' they replied. "'You also, go into the vineyard,' he said.
8 “Ndipo pofika madzulo, mwini munda wamphesa anayitana kapitawo wake nati, ‘Itana antchito ndipo uwapatse malipiro awo, kuyambira omalizira aja mpaka oyamba.’
"When evening came, the master said to his steward, "'Call the men and pay them their wages. Begin with the last set and finish with the first.'
9 “Antchito amene anawalemba ganyu pa 5 koloko masana anafika ndipo aliyense analandira dinari.
"When those came who had begun at five o'clock, they received a shilling apiece;
10 Ndipo atabwera kwa amene analembedwa poyamba anayembekezera kuti alandira zambiri. Koma aliyense wa iwo analandira dinari.
and when the first came, they expected to get more, but they also each got the shilling.
11 Atalandira, anayamba kuderera kwa mwini mundayo.
So when they had received it, they grumbled against the employer, saying,
12 Iwo anati, ‘Anthu amene munawalemba pomalizira agwira ntchito ora limodzi, ndipo mwawafananitsa ndi ife amene tathyoka nayo ntchito ndi kutentha kwa dzuwa tsiku lonse.’
"'These who came last have done only one hour's work, and you have put them on a level with us who have worked the whole day and have borne the scorching heat.'
13 “Koma iye anamuyankha mmodzi wa iwo nati, ‘Bwenzi, ine sikuti sindinachite chilungamo. Kodi sunavomereze kuti ugwira ntchito ndi kulandira dinari?
"'My friend,' he answered to one of them, 'I am doing you no injustice. Did you not agree with me for a shilling?
14 Tenga malipiro ako pita. Ndikufuna kumupatsa munthu amene ndinamulemba pomaliza mofanana ndi mmene ndakupatsira iwe.
Take your money and go. I choose to give this last comer just as much as I give you.
15 Kodi ndilibe ufulu wochita zimene ndikufuna ndi ndalama zanga? Kapena ukuyipidwa chifukwa ndine wopereka mowolowamanja?’
Have I not a right to do what I choose with my own property? Or are you envious because I am generous?'
16 “Momwemo omalizira adzakhala oyamba ndipo oyamba adzakhala omalizira.”
"So the last shall be first, and the first last."
17 Tsopano pamene Yesu ankapita ku Yerusalemu, anatengera pambali ophunzira ake khumi ndi awiriwo nati kwa iwo,
Jesus was now going up to Jerusalem, and He took the twelve disciples aside by themselves, and on the way He said to them,
18 “Tikupita ku Yerusalemu, ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo adzamuweruza kuti aphedwe,
"We are going up to Jerusalem, and there the Son of Man will be betrayed to the High Priests and Scribes. They will condemn Him to death,
19 ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina kuti amunyoze ndi kumukwapula ndi kumupachika. Pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa!”
and hand Him over to the Gentiles to be made sport of and scourged and crucified; and on the third day He will be raised to life."
20 Amayi a ana a Zebedayo anabwera ndi ana ake kwa Yesu, nagwada pansi namupempha Iye.
Then the mother of the sons of Zabdi came to Him with her sons, and knelt before Him to make a request of Him.
21 Yesu anawafunsa kuti, “Mukufuna chiyani?” Amayiwo anati, “Lolani kuti ana anga awiriwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja ndi wina ku dzanja lanu lamazere mu ufumu wanu.”
"What is it you desire?" He asked. "Command," she replied, "that these my two sons may sit one at your right hand and one at your left in your Kingdom."
22 Yesu anawawuza kuti, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungathe kumwera chikho chimene ndidzamwera Ine?” Iwo anayankha nati, “Inde tingathe.”
"None of you know what you are asking for," said Jesus; "can you drink out of the cup from which I am about to drink?" "We can," they replied.
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi mudzamwera chikho changa, koma kuti mudzakhale ku dzanja langa lamanja kapena lamazere si kwa Ine kupereka. Malo awa ndi a iwo amene anakonzeredweratu ndi Atate anga.”
"You shall drink out of my cup," He said, "but a seat at my right hand or at my left it is not for me to allot, but it belongs to those for whom it has been prepared by my Father."
24 Ophunzira khumi aja, anawapsera mtima abale awiriwo.
The other ten heard of this, and their indignation was aroused against the two brothers.
25 Yesu anawayitana onse pamodzi nati, “Mukudziwa kuti olamulira a mitundu ina ali ndi mphamvu pa iwo, ndipo akuluakulu awo amawalamulira.
But Jesus called them to Him, and said, "You know that the rulers of the Gentiles lord it over them, and their great men exercise authority over them.
26 Siziyenera kutero ndi inu. Mʼmalo mwake, aliyense amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu akhale wotumikira wanu.
Not so shall it be among you; but whoever desires to be great among you shall be your servant,
27 Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu.
and whoever desires to be first among you shall be your bondservant;
28 Momwenso Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kukhala dipo la anthu ambiri.”
just as the Son of Man came not to be served but to serve, and to give His life as the redemption-price for many."
29 Pamene Yesu ndi ophunzira ake ankachoka ku Yeriko, gulu lalikulu la anthu linawatsata.
As they were leaving Jericho, an immense crowd following Him,
30 Amuna awiri osaona anakhala mʼmbali mwa msewu, ndipo pamene anamva kuti Yesu akudutsa anafuwula kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
two blind men sitting by the roadside heard that it was Jesus who was passing by, and cried aloud, "Sir, Son of David, pity us."
31 Gulu la anthulo linawadzudzula iwo ndi kuwawuza kuti akhale chete, koma anafuwulitsabe kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”
The people angrily tried to silence them, but they cried all the louder. "O Sir, Son of David, pity us," they said.
32 Yesu anayima ndi kuwayitana ndipo anawafunsa kuti, “Mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
So Jesus stood still and called to them. "What shall I do for you?" He asked.
33 Anamuyankha nati, “Ambuye, tikufuna tione!”
"Sir, let our eyes be opened," they replied.
34 Yesu anamva nawo chifundo ndipo anakhudza maso awo. Nthawi yomweyo anaona namutsata Iye.
Moved with compassion, Jesus touched their eyes, and immediately they regained their sight and followed Him.