< Mateyu 2 >

1 Atabadwa Yesu mʼBetelehemu wa ku Yudeya, mʼnthawi ya mfumu Herode, Anzeru a kummawa anabwera ku Yerusalemu
Or, lorsque Jésus naquit à Bethléem de Judée, du temps du roi Hérode, voici que des mages venus d'Orient se rendirent à Jérusalem, en disant:
2 nafunsa kuti, “Ali kuti amene wabadwa kukhala mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kummawa ndipo tabwera kudzamupembedza.”
« Où est celui qui est né roi des Juifs? Car nous avons vu son étoile en Orient, et nous sommes venus nous prosterner devant lui. »
3 Mfumu Herode atamva zimenezi, anavutika mu mtima kwambiri pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu.
Lorsque le roi Hérode entendit cela, il fut troublé, et tout Jérusalem avec lui.
4 Ndipo anayitanitsa anthu onse, akulu ansembe ndi aphunzitsi amalamulo nawafunsa kuti, “Kodi Khristu adzabadwira kuti?”
Rassemblant tous les chefs des prêtres et les scribes du peuple, il leur demanda où le Christ devait naître.
5 Ndipo anamuyankha kuti, “Ku Betelehemu wa ku Yudeya chifukwa izi ndi zimene mneneri analemba kuti,
Ils lui répondirent: A Bethléhem de Judée, car ceci est écrit par le prophète,
6 “‘Koma iwe Betelehemu, chigawo cha Yudeya, sindiwe wamngʼonongʼono mwa olamulira a Yudeya; pakuti otsogolera adzachokera mwa iwe, amene adzaweta anthu anga Aisraeli.’”
« Toi, Bethléem, terre de Judée. ne sont en rien les moindres parmi les princes de Juda; car de toi sortira un gouverneur qui sera le berger de mon peuple, Israël. »
7 Pomwepo Herode anawayitanira mseri Anzeruwo nawafunsitsa nthawi yeniyeni yomwe nyenyeziyo inaoneka.
Alors Hérode appela secrètement les sages, et il apprit d'eux à quelle heure exactement l'étoile était apparue.
8 Ndipo anawatumiza ku Betelehemu nawawuza kuti, “Pitani mukafufuze za mwanayo mosamalitsa. Ndipo mukamupeza mudzandiwuze kuti inenso ndikamupembedze.”
Il les envoya à Bethléem et leur dit: « Allez chercher le petit enfant. Quand vous l'aurez trouvé, faites-moi signe, afin que je vienne moi aussi l'adorer. »
9 Atamva mawu a mfumu, ananyamuka ulendo wawo, ndipo taonani nyenyezi anayiona kummawa ija, inawatsogolera mpaka inayima pamwamba pa nyumba yomwe munali mwanayo.
Après avoir entendu le roi, ils s'en allèrent. Et voici, l'étoile qu'ils avaient vue à l'orient les précédait, jusqu'à ce qu'elle vienne se placer au-dessus du lieu où était le petit enfant.
10 Pamene iwo anaona nyenyeziyo, anasangalala kwambiri.
Quand ils virent l'étoile, ils se réjouirent d'une très grande joie.
11 Pofika ku nyumbayo, anaona mwanayo pamodzi ndi amayi ake Mariya, ndipo anagwada namulambira Iye. Pomwepo anamasula chuma chawo ndi kupereka mphatso zawo za ndalama zagolide, lubani ndi mure.
Ils entrèrent dans la maison et virent le petit enfant avec Marie, sa mère; ils se prosternèrent et l'adorèrent. Ouvrant leurs trésors, ils lui offrirent des présents: de l'or, de l'encens et de la myrrhe.
12 Ndipo atachenjezedwa mʼmaloto kuti asapitenso kwa Herode, anabwerera ku dziko la kwawo podzera njira ina.
Ayant été avertis en songe de ne pas retourner auprès d'Hérode, ils s'en retournèrent dans leur pays par un autre chemin.
13 Atachoka, taonani mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto nati, “Tadzuka, tenga mwanayo pamodzi ndi amayi ake ndipo muthawire ku Igupto. Mukakhale kumeneko mpaka nditakuwuza pakuti Herode adzafunafuna mwanayo kuti amuphe.”
Or, quand ils furent partis, voici qu'un ange du Seigneur apparut en songe à Joseph, en disant: « Lève-toi, prends le petit enfant et sa mère, fuis en Égypte, et restes-y jusqu'à ce que je te le dise, car Hérode cherchera le petit enfant pour le faire périr. »
14 Atadzuka, Yosefe anatenga mwanayo ndi amayi ake usiku omwewo napita ku Igupto,
Il se leva, prit de nuit le petit enfant et sa mère, et s'en alla en Égypte,
15 nakhala kumeneko mpaka Herode atamwalira. Ndipo zinakwaniritsidwa zomwe ananena Ambuye mwa mneneri kuti, “Ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.”
où il resta jusqu'à la mort d'Hérode, afin que s'accomplît ce que le Seigneur avait annoncé par le prophète: « J'ai appelé mon fils hors d'Égypte. »
16 Herode atazindikira kuti Anzeruwo anamupusitsa, anakwiya kwambiri. Ndipo anatumiza anthu kukapha ana onse aamuna a mʼBetelehemu ndi midzi yozungulira amene anali a zaka ziwiri kapena zocheperapo, molingana ndi nthawi imene Anzeruwo anamuwuza.
Alors Hérode, voyant qu'on se moquait de lui par les sages, fut extrêmement irrité, et il envoya tuer tous les enfants mâles qui étaient à Bethléem et dans toute la campagne environnante, depuis l'âge de deux ans et au-dessous, selon le temps exact qu'il avait appris des sages.
17 Pamenepo, zimene ananena mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa:
Alors s'accomplit ce qui avait été annoncé par Jérémie, le prophète, en ces termes,
18 “Kulira kukumveka ku Rama, kubuma ndi kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake; sakutonthozeka, chifukwa ana akewo palibe.”
« Une voix se fit entendre à Rama, des lamentations, des pleurs et un grand deuil, Rachel pleurant ses enfants; elle ne serait pas réconfortée, car ils ne sont plus. »
19 Atamwalira Herode, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto ku Igupto
Mais lorsque Hérode fut mort, voici qu'un ange du Seigneur apparut en songe à Joseph en Égypte, et dit:
20 nanena kuti, “Nyamuka, tenga mwanayo ndi amayi ake ndipo mupite ku dziko la Israeli, popeza amene anafuna moyo wa mwanayo anamwalira.”
« Lève-toi, prends le petit enfant et sa mère, et va dans le pays d'Israël, car ceux qui en voulaient à la vie du petit enfant sont morts. »
21 Tsono Yosefe atadzuka anatenga mwanayo ndi amayi ake kupita ku dziko la Israeli.
Il se leva, prit le petit enfant et sa mère, et se rendit dans le pays d'Israël.
22 Koma atamva kuti Arikelao akulamulira mu Yudeya mʼmalo mwa abambo ake, Herode, anaopa kupitako. Atachenjezedwa mʼmaloto, anapita ku Galileya,
Mais, ayant appris qu'Archélaüs régnait en Judée à la place d'Hérode, son père, il eut peur de s'y rendre. Averti en songe, il se retira dans la région de la Galilée,
23 ndipo anakakhazikika mu mzinda wa Nazareti. Pamenepo zinakwaniritsidwa zonenedwa ndi aneneri kuti, “Adzatchedwa Mnazareti.”
et vint s'établir dans une ville appelée Nazareth, afin que s'accomplisse ce qui avait été annoncé par les prophètes: il sera appelé Nazaréen.

< Mateyu 2 >