< Mateyu 19 >

1 Yesu atatsiriza kunena zinthu zimenezi, anachoka ku Galileya ndi kupita ku chigawo cha Yudeya mbali ina ya mtsinje wa Yorodani.
Kui Jeesus lõpetas kõnelemise, lahkus ta Galileast, ning läks Jordani jõe taha Juuda aladele.
2 Magulu akulu a anthu anamutsatira Iye, ndipo iwo anachiritsidwa pomwepo.
Suured rahvahulgad järgisid teda ja ta tegi terveks need, kes rahva seast haiged olid.
3 Afarisi ena anabwera kwa Iye kudzamuyesa. Anamufunsa Iye nati, “Kodi ndikololedwa kuti mwamuna amuleke mkazi wake pa chifukwa china chilichonse?”
Mõned variserid tulid teda proovile panema. „Kas mehel on lubatud oma naisest mingil põhjusel lahutada?“küsisid nad.
4 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge kuti pachiyambi Mulungu analenga iwo, ‘mwamuna ndi mkazi?’
Jeesus vastas: „Kas te ei ole lugenud, et Jumal, kes lõi alguses inimesed, tegi nad meheks ja naiseks?
5 Ndipo anati, ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’
Ta ütles: „Sel põhjusel jätab mees maha oma isa ja ema ning ühineb oma naisega ja nemad kaks saavad üheks.“
6 Motero salinso awiri ayi koma mmodzi. Nʼchifukwa chake chimene Mulungu wachimanga pamodzi munthu wina asachilekanitse.”
Nüüd ei ole nad enam kaks, vaid üks. Keegi ei tohi eraldada seda, mille Jumal on liitnud.“
7 Ndipo iwo anamufunsa nati, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mose analamula kuti mwamuna azipatsa mkazi wake kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa?”
„Miks siis Mooses andis seaduse, et mees võib oma naisest lahutada, kui annab talle lahutustunnistuse, ja ta minema saata?“küsisid nad.
8 Yesu anayankha kuti, “Mose anakulolezani kuti muzisudzula akazi anu chifukwa cha kuwuma mitima kwanu. Koma sizinali chotere kuyambira pachiyambi.
„Teie kalgi südame pärast lubas Mooses teil oma naisest lahutada, aga alguses ei olnud see nii, “vastas Jeesus.
9 Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake, osati chifukwa cha chiwerewere nakakwatira mkazi wina, achita chigololo.”
„Ma ütlen teile, igaüks, kes lahutab oma naisest muidu kui seksuaalse ebamoraalsuse tõttu ja abiellub siis teise naisega, rikub abielu.“
10 Ophunzira ake anati kwa Iye, “Ngati umu ndi mmene zilili pa mwamuna ndi mkazi, kuli bwino kusakwatira.”
„Kui olukord mehe ja naise vahel on selline, siis on parem mitte abielluda!“ütlesid ta jüngrid talle.
11 Yesu anayankha kuti, “Si aliyense amene angavomere chiphunzitso ichi, koma kwa okhawo amene achimvetsetsa.
„Kõik ei suuda seda õpetust vastu võtta, vaid ainult need, kellele see on antud, “lausus Jeesus neile.
12 Pakuti ena ndi akuti sangakwatire chifukwa anabadwa motero, ena ali motero chifukwa chofulidwa ndi anthu ndipo ena anawukana ukwati chifukwa cha ufumu wakumwamba. Iye amene angalandire ichi alandire.”
„Mõni on sündinud eunuhh, mõne on eunuhhiks teinud inimesed ning mõni otsustab olla eunuhh taevariigi pärast. Need, kes suudavad selle vastu võtta, peaks seda tegema.“
13 Pamenepo anabwera nawo ana kwa Yesu kuti awasanjike manja ndi kuwapempherera. Koma ophunzira ake anadzudzula amene anabweretsa anawo.
Inimesed tõid väikesed lapsed tema juurde, et ta neid õnnistaks ja nende eest palvetaks. Kuid jüngrid keelasid neid.
14 Yesu anati, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse pakuti ufumu wakumwamba ndi wa iwo onga anawa.”
Aga Jeesus ütles: „Laske lastel minu juurde tulla. Ärge takistage neid. Taevariik kuulub neile, kes on nendesarnased!“
15 Atasanjika manja ake pa anawo, anachokapo.
Ta pani oma käed nende peale ja õnnistas neid ning siis ta lahkus.
16 Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?” (aiōnios g166)
Üks mees tuli Jeesuse juurde ja küsis temalt: „Õpetaja, mida head ma pean tegema, et igavest elu saada?“ (aiōnios g166)
17 Yesu anayankha kuti, “Ukundifunsiranji Ine za chinthu chimene ndi chabwino? Pali mmodzi yekha amene ndi wabwino. Ngati ukufuna kulowa mʼmoyo wosatha mvera malamulo.”
„Miks sa küsid minult, mis on hea?“vastas Jeesus. „On ainult üks, kes on hea. Aga kui tahad igavest elu saada, siis pea käske.“
18 Mnyamatayo anamufunsa kuti, “Ndi ati?” Yesu anayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni onama,
„Missuguseid?“küsis mees temalt. „Ära tapa, ära riku abielu, ära varasta, ära anna valetunnistust,
19 lemekeza abambo ako ndi amayi ako ndipo konda mnansi wako monga iwe mwini.”
austa oma isa ja ema ning armasta oma kaasinimest nagu iseennast, “vastas Jeesus.
20 Mnyamatayo anati, “Zonsezi ndimazisunga, nanga chatsala ndi chiyani?”
„Olen kõiki neid käske pidanud, “lausus noormees. „Mida ma veel pean tegema?“
21 Yesu anayankha kuti, “Ngati ukufuna kukhala wangwiro, pita kagulitse katundu wako ndi kupereka kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ukakachita zimenezi, ukabwere udzanditsate Ine.”
Jeesus kostis talle: „Kui sa tahad täiuslik olla, siis mine ja müü oma vara ära, anna raha vaestele ja sul on aare taevas. Siis tule ja järgi mind.“
22 Mnyamatayo atamva zimenezi, anachoka mokhumudwa, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
Kui noormees kuulis Jeesuse vastust, läks ta väga kurvalt ära, sest tal oli palju vara.
23 Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti nʼkovuta kuti olemera akalowe mu ufumu wakumwamba.
„Ma räägin teile tõtt, “ütles Jeesus oma jüngritele, „rikastel inimestel on raske taevariiki siseneda.
24 Komanso ndikuwuzani kuti, nʼkwapafupi kuti ngamira idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi kuti wolemera akalowe mu ufumu wa Mulungu.”
Ma ütlen teile ka seda: lihtsam on kaamelil läbi nõelsilma minna, kui rikkal inimesel Jumala riiki siseneda.“
25 Ophunzira atamva zimenezi, anadabwa kwambiri ndipo anamufunsa kuti, “Nanga angapulumuke ndani?”
Kui jüngrid seda kuulsid, olid nad väga üllatunud ja küsisid: „Kes võib siis päästetud saada?“
26 Yesu anawayangʼana iwo nati, “Ndi anthu, izi nʼzosatheka, koma ndi Mulungu zinthu zonse zimatheka.”
Jeesus vaatas neid ja ütles: „Inimlikust vaatenurgast on see võimatu, aga Jumalaga koos on kõik võimalik.“
27 Petro anamuyankha Iye kuti, “Ife tinasiya zonse ndi kukutsatirani Inu! Nanga tsono ife tidzalandira chiyani?”
Peetrus vastas talle: „Vaata, me oleme jätnud kõik maha ja sind järginud. Mis tasu me saame?“
28 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti pa nthawi yokonzanso zinthu zonse, pamene Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake waufumu mu ulemerero wake kumwamba, inu amene mwanditsata Ine mudzakhalanso pa mipando khumi ndi iwiri yaufumu, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
Jeesus vastas: „Ma ütlen teile tõtt: kui kõik on uueks loodud ja inimese Poeg istub oma hiilgaval troonil, siis teie, kes te olete mind järginud, istute ka kaheteistkümnel troonil ning mõistate kohut Iisraeli kaheteistkümne suguharu üle.
29 Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. (aiōnios g166)
Kõik need, kes on minu pärast jätnud maha oma kodu, vennad, õed, isa, ema, lapsed ja põllud, saavad sada korda rohkem tagasi ja igavese elu. (aiōnios g166)
30 Koma ambiri amene ali oyambirira adzakhala omalizira, ndipo ambiri amene ndi omalizira adzakhala oyambirira.”
Sest paljud, kes on esimesed, jäävad viimasteks, ja paljud, kes on viimased, saavad esimesteks.

< Mateyu 19 >