< Mateyu 17 >

1 Patapita masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo, ndi Yohane mʼbale wa Yakobo pa okha ndipo anakwera nawo pa phiri lalitali.
Lemva kwensuku eziyisithupha uJesu wathatha uPetro loJakobe loJohane umfowabo, wasekhwela labo entabeni ende bebodwa.
2 Pamenepo Iye anasinthika maonekedwe ake pamaso pawo. Nkhope yake inawala ngati dzuwa ndipo zovala zake zinayera kuti mbuu.
Waseguqulwa isimo phambi kwabo, njalo ubuso bakhe bakhanya njengelanga, lezembatho zakhe zaba mhlophe njengokukhanya.
3 Nthawi yomweyo Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo akuyankhulana ndi Yesu.
Futhi khangela, kwasekubonakala kubo uMozisi loElija, bekhuluma laye.
4 Petro anati kwa Yesu, “Ambuye ndi bwino kuti ife tikhale pano. Ngati mufuna ndidzamanga misasa itatu umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
UPetro wasephendula wathi kuJesu: Nkosi, kuhle ukuthi sibe lapha. Uba uthanda, asakhe lapha amadumba amathathu, elinye ngelakho, lelinye ngelikaMozisi, lelinye ngelikaElija.
5 Iye akuyankhulabe, mtambo owala unawaphimba, ndipo mawu ochokera mu mtambo anati, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimukonda ndipo ndikondwera naye kwambiri. Mumumvere Iye!”
Kwathi esakhuluma, khangela, iyezi elikhanyayo labasibekela; futhi khangela, ilizwi laphuma eyezini, lisithi: Lo uyiNdodana yami ethandekayo, engithokoza ngayo; zwanini yona.
6 Ophunzira atamva zimenezi, anachita mantha nagwa pansi chafufumimba.
Sebezwile abafundi, bawa phansi ngobuso babo, besaba kakhulu.
7 Ndipo Yesu anabwera nawakhudza nati, “Dzukani, musaope.”
Kodwa uJesu weza wabathinta wathi: Sukumani lingesabi.
8 Atayangʼana, sanaone wina aliyense kupatula Yesu yekha.
Sebephakamisile amehlo abo, kababonanga muntu, ngaphandle kukaJesu yedwa.
9 Akutsika ku phiriko, Yesu anawalamula kuti, “Musawuze wina aliyense zimene mwaona, mpaka Mwana wa Munthu ataukitsidwa kwa akufa.”
Sebesehla entabeni, uJesu wabalaya, wathi: Lingatsheli muntu lowombono, ize ivuke kwabafileyo iNdodana yomuntu.
10 Ophunzira anamufunsa Iye kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kukhala woyamba kubwera?”
Abafundi bakhe basebembuza bathi: Pho batsholoni ababhali ukuthi uElija ufanele ukufika kuqala?
11 Yesu anayankha kuti, “Kunena zoona, Eliya adzayenera kubwera ndipo adzakonza zinthu zonse.
UJesu wasephendula wathi kubo: UElija uzafika kuqala isibili, uzabuyisela zonke izinto;
12 Koma Ine ndikuwuzani inu kuti Eliya anabwera kale koma iwo sanamuzindikire ndipo anachita naye chilichonse chimene anafuna. Momwemonso iwo adzazunza Mwana wa Munthu.”
kodwa ngitsho kini ukuthi uElija sewafika, kodwa kabamazanga, kodwa benza kuye konke ababekuthanda; ngokunjalo leNdodana yomuntu izahlutshwa yibo.
13 Pamenepo ophunzira anazindikira kuti amawawuza za Yohane Mʼbatizi.
Abafundi basebeqedisisa ukuthi wakhuluma labo ngoJohane uMbhabhathizi.
14 Atafika ku gulu la anthu, munthu wina anamuyandikira Yesu ndi kugwada pamaso pake.
Kwathi sebefikile exukwini, kweza kuye umuntu waguqa phambi kwakhe wathi:
15 Iye anati, “Ambuye, muchitireni chifundo mwana wanga akudwala matenda akugwa ndipo akuvutika kwambiri. Kawirikawiri iye amagwa pa moto kapena mʼmadzi.
Nkosi, akuhawukele indodana yami, ngoba ilesithuthwane iyahlupheka kakhulu; ngoba iwele kanengi emlilweni, futhi kanengi emanzini.
16 Ine ndinabwera naye kwa ophunzira anu koma alephera kumuchiritsa.”
Njalo ngiyilethe kubafundi bakho, kodwa bebengelakho ukuyisilisa.
17 Yesu anayankha nati, “Haa, mʼbado wosakhulupirira ndi wokhota maganizo! Kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Ndidzapirira nanu mpaka liti? Bwera nayeni kwa Ine mnyamatayo.”
UJesu wasephendula wathi: O sizukulwana esingelakholo lesonakeleyo, koze kube nini ngilani? Koze kube nini ngilibekezelela? Mletheni kimi lapha.
18 Yesu anadzudzula chiwandacho ndipo chinatuluka mwa mnyamatayo ndipo anachira nthawi yomweyo.
UJesu waselikhuza, idimoni laseliphuma kuyo, umntwana wasesila kusukela kulelohola.
19 Pamenepo ophunzira anabwera kwa Yesu mwamseri ndi kumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani ife tinalephera kutulutsa chiwandacho?”
Abafundi basebesiza kuJesu bebodwa bathi: Kungani thina sehlulekile ukulikhupha?
20 Iye anayankha kuti, “Chifukwa inu muli ndi chikhulupiriro chachingʼono. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro monga kambewu ka mpiru, mukhoza kunena ndi phiri ili kuti, ‘Choka apa nupite apo,’ ndipo lidzachoka. Palibe kanthu kamene kadzakukanikani.
UJesu wasesithi kubo: Kungenxa yokungakholwa kwenu. Ngoba ngiqinisile ngithi kini: Aluba lilokholo olunjengohlamvu lwemasitedi, lizakuthi kulintaba: Suka lapha uye laphaya; njalo izasuka; futhi kaliyikwehlulwa lutho.
21 Chiwanda cha mtundu uwu sichingachoke chabe koma ndi pemphero ndi kusala kudya.”
Kodwa loluhlobo kaluphumi ngaphandle kwangomkhuleko langokuzila ukudla.
22 Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Iye anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.
Besahlezi eGalili, uJesu wathi kubo: INdodana yomuntu isizanikelwa ezandleni zabantu,
23 Iwo adzamupha koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.” Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chisoni.
njalo bazayibulala, kodwa ngosuku lwesithathu izavuswa. Basebedabuka kakhulu.
24 Yesu ndi ophunzira ake atafika ku Kaperenawo, wolandira msonkho wa ku Nyumba ya Mulungu anabwera kwa Petro namufunsa kuti, “Kodi aphunzitsi anu sapereka msonkho wa Nyumba ya Mulungu?”
Kwathi sebefikile eKapenawume, abemukela umthelo beza kuPetro bathi: Umfundisi wenu katheli yini?
25 Iye anayankha kuti, “Inde amapereka.” Petro atalowa mʼnyumba, Yesu ndiye anayamba kuyankhula. Ndipo anamufunsa kuti, “Ukuganiza bwanji Simoni, kodi mafumu a dziko lapansi amalandira msonkho kuchokera kwa ana awo kapena kwa ena?”
Wathi: Yebo. Esengenile endlini, uJesu wamandulela wathi: Ucabangani, Simoni? Amakhosi omhlaba emukela kubani imfanelo kumbe imithelo? Kumadodana abo yini, kumbe kwabezizwe?
26 Petro anayankha kuti, “Kuchokera kwa ena.” Yesu ananena kwa iye kuti, “Ndiye kuti ana sapereka.”
UPetro wathi kuye: Kwabezizwe. UJesu wathi kuye: Ngakho-ke amadodana akhululekile.
27 Koma kuti ife tisawakhumudwitse pita ku nyanja kaponye mbedza yako. Katenge nsomba imene ukayambe kuyikola; kayitsekule kukamwa ndipo ukapezamo ndalama. Katenge ndalamayo ndi kukapereka msonkho wanga ndi wanu.
Kodwa-ke ukuze singabakhubekisi, hamba uye elwandle uphose ingwegwe, uthathe inhlanzi ezaphuma kuqala; kuzakuthi usuvule umlomo wayo uzathola imali; uyithathe ubanike ibe ngeyami leyakho.

< Mateyu 17 >