< Mateyu 17 >
1 Patapita masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo, ndi Yohane mʼbale wa Yakobo pa okha ndipo anakwera nawo pa phiri lalitali.
Six day later, Jesus took with Him Peter and the brothers James and John, and brought them up a high mountain to a solitary place.
2 Pamenepo Iye anasinthika maonekedwe ake pamaso pawo. Nkhope yake inawala ngati dzuwa ndipo zovala zake zinayera kuti mbuu.
There in their presence His form underwent a change; His face shone like the sun, and His raiment became as white as the light.
3 Nthawi yomweyo Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo akuyankhulana ndi Yesu.
And suddenly Moses and Elijah appeared to them conversing with Him.
4 Petro anati kwa Yesu, “Ambuye ndi bwino kuti ife tikhale pano. Ngati mufuna ndidzamanga misasa itatu umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
Then Peter said to Jesus, "Master, we are thankful to you that we are here. If you approve, I will put up three tents here, one for you, one for Moses, and one for Elijah."
5 Iye akuyankhulabe, mtambo owala unawaphimba, ndipo mawu ochokera mu mtambo anati, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimukonda ndipo ndikondwera naye kwambiri. Mumumvere Iye!”
He was still speaking when a luminous cloud spread over them; and a voice was heard from within the cloud, which said, "This is My Son dearly beloved, in whom is My delight. Listen to Him."
6 Ophunzira atamva zimenezi, anachita mantha nagwa pansi chafufumimba.
On hearing this voice, the disciples fell on their faces and were filled with terror.
7 Ndipo Yesu anabwera nawakhudza nati, “Dzukani, musaope.”
But Jesus came and touched them, and said, "Rouse yourselves and have no fear."
8 Atayangʼana, sanaone wina aliyense kupatula Yesu yekha.
So they looked up, and saw no one but Jesus.
9 Akutsika ku phiriko, Yesu anawalamula kuti, “Musawuze wina aliyense zimene mwaona, mpaka Mwana wa Munthu ataukitsidwa kwa akufa.”
As they were descending the mountain, Jesus laid a command upon them. "Tell no one," He said, "of the sight you have seen till the Son of Man has risen from among the dead."
10 Ophunzira anamufunsa Iye kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kukhala woyamba kubwera?”
"Why then," asked the disciples, "do the Scribes say that Elijah must first come?"
11 Yesu anayankha kuti, “Kunena zoona, Eliya adzayenera kubwera ndipo adzakonza zinthu zonse.
"Elijah was indeed to come," He replied, "and would reform everything.
12 Koma Ine ndikuwuzani inu kuti Eliya anabwera kale koma iwo sanamuzindikire ndipo anachita naye chilichonse chimene anafuna. Momwemonso iwo adzazunza Mwana wa Munthu.”
But I tell you that he has already come, and they did not recognize him, but dealt with him as they chose. And before long the Son of Man will be treated by them in a similar way."
13 Pamenepo ophunzira anazindikira kuti amawawuza za Yohane Mʼbatizi.
Then it dawned upon the disciples that it was John the Baptist about whom He had spoken to them.
14 Atafika ku gulu la anthu, munthu wina anamuyandikira Yesu ndi kugwada pamaso pake.
When they had returned to the people, there came to Him a man who fell on his knees before Him and besought Him.
15 Iye anati, “Ambuye, muchitireni chifundo mwana wanga akudwala matenda akugwa ndipo akuvutika kwambiri. Kawirikawiri iye amagwa pa moto kapena mʼmadzi.
"Sir," he said, "have pity on my son, for he is an epileptic and is very ill. Often he falls into the fire and often into the water.
16 Ine ndinabwera naye kwa ophunzira anu koma alephera kumuchiritsa.”
I have brought him to your disciples, and they have not been able to cure him."
17 Yesu anayankha nati, “Haa, mʼbado wosakhulupirira ndi wokhota maganizo! Kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Ndidzapirira nanu mpaka liti? Bwera nayeni kwa Ine mnyamatayo.”
"O unbelieving and perverse generation!" replied Jesus; "how long shall I be with you? how long shall I endure you? Bring him to me."
18 Yesu anadzudzula chiwandacho ndipo chinatuluka mwa mnyamatayo ndipo anachira nthawi yomweyo.
Then Jesus reprimanded the demon, and it came out and left him; and the boy was cured from that moment.
19 Pamenepo ophunzira anabwera kwa Yesu mwamseri ndi kumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani ife tinalephera kutulutsa chiwandacho?”
Then the disciples came to Jesus privately and asked Him, "Why could not we expel the demon?"
20 Iye anayankha kuti, “Chifukwa inu muli ndi chikhulupiriro chachingʼono. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro monga kambewu ka mpiru, mukhoza kunena ndi phiri ili kuti, ‘Choka apa nupite apo,’ ndipo lidzachoka. Palibe kanthu kamene kadzakukanikani.
"Because your faith is so small," He replied; "for I solemnly declare to you that if you have faith like a mustard-seed, you shall say to this mountain, 'Remove from this place to that,' and it will remove; and nothing shall be impossible to you.
21 Chiwanda cha mtundu uwu sichingachoke chabe koma ndi pemphero ndi kusala kudya.”
But an evil spirit of this kind is only driven out by prayer and fasting."
22 Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Iye anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.
As they were travelling about in Galilee, Jesus said to them, "The Son of Man is about to be betrayed into the hands of men;
23 Iwo adzamupha koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.” Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chisoni.
they will put Him to death, but on the third day He will be raised to life again." And they were exceedingly distressed.
24 Yesu ndi ophunzira ake atafika ku Kaperenawo, wolandira msonkho wa ku Nyumba ya Mulungu anabwera kwa Petro namufunsa kuti, “Kodi aphunzitsi anu sapereka msonkho wa Nyumba ya Mulungu?”
After their arrival at Capernaum the collectors of the half-shekel came and asked Peter, "Does not your Teacher pay the half-shekel?"
25 Iye anayankha kuti, “Inde amapereka.” Petro atalowa mʼnyumba, Yesu ndiye anayamba kuyankhula. Ndipo anamufunsa kuti, “Ukuganiza bwanji Simoni, kodi mafumu a dziko lapansi amalandira msonkho kuchokera kwa ana awo kapena kwa ena?”
"Yes," he replied, and then went into the house. But before he spoke a word Jesus said, "What think you, Simon? From whom do this world's kings receive customs or capitation tax? from their own children, or from others?"
26 Petro anayankha kuti, “Kuchokera kwa ena.” Yesu ananena kwa iye kuti, “Ndiye kuti ana sapereka.”
"From others," he replied. "Then the children go free," said Jesus.
27 Koma kuti ife tisawakhumudwitse pita ku nyanja kaponye mbedza yako. Katenge nsomba imene ukayambe kuyikola; kayitsekule kukamwa ndipo ukapezamo ndalama. Katenge ndalamayo ndi kukapereka msonkho wanga ndi wanu.
"However, lest we cause them to sin, go and throw a hook into the Lake, and take the first fish that comes up. When you open its mouth, you will find a shekel in it: bring that coin and give it to them for yourself and me."