< Mateyu 17 >

1 Patapita masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo, ndi Yohane mʼbale wa Yakobo pa okha ndipo anakwera nawo pa phiri lalitali.
And after six days, Jesus took with him Peter and James and John his brother, and led them up into a high mountain apart:
2 Pamenepo Iye anasinthika maonekedwe ake pamaso pawo. Nkhope yake inawala ngati dzuwa ndipo zovala zake zinayera kuti mbuu.
and he was transfigured before them: and his face did shine as the sun, and his clothing was white as the light.
3 Nthawi yomweyo Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo akuyankhulana ndi Yesu.
And behold, there appeared to them Moses and Elijah, talking with him.
4 Petro anati kwa Yesu, “Ambuye ndi bwino kuti ife tikhale pano. Ngati mufuna ndidzamanga misasa itatu umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
And Peter answered and said to Jesus: Lord, it is good for us to be here; if thou wilt, let us make here three tents, one for thee, and one for Moses, and one for Elijah.
5 Iye akuyankhulabe, mtambo owala unawaphimba, ndipo mawu ochokera mu mtambo anati, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimukonda ndipo ndikondwera naye kwambiri. Mumumvere Iye!”
While he was yet speaking, behold, a bright cloud overshadowed them; and lo, a voice from the cloud, saying: This is my beloved Son, in whom I delight; hear him.
6 Ophunzira atamva zimenezi, anachita mantha nagwa pansi chafufumimba.
And when the disciples heard it, they fell on their faces, and were greatly afraid.
7 Ndipo Yesu anabwera nawakhudza nati, “Dzukani, musaope.”
And Jesus came and touched them, and said: Arise and be not afraid.
8 Atayangʼana, sanaone wina aliyense kupatula Yesu yekha.
And when they lifted up their eyes, they saw no one but Jesus.
9 Akutsika ku phiriko, Yesu anawalamula kuti, “Musawuze wina aliyense zimene mwaona, mpaka Mwana wa Munthu ataukitsidwa kwa akufa.”
And as they came down from the mountain, Jesus charged them, saying: Tell the vision to no one, till the Son of man has risen from the dead.
10 Ophunzira anamufunsa Iye kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kukhala woyamba kubwera?”
And his disciples asked him, saying: Why then do the scribes say that Elijah must come first?
11 Yesu anayankha kuti, “Kunena zoona, Eliya adzayenera kubwera ndipo adzakonza zinthu zonse.
Jesus answered and said to them: Elijah, indeed, comes first, and he will restore all things.
12 Koma Ine ndikuwuzani inu kuti Eliya anabwera kale koma iwo sanamuzindikire ndipo anachita naye chilichonse chimene anafuna. Momwemonso iwo adzazunza Mwana wa Munthu.”
But I say to you, That Elijah has already come, and they did not recognize him, but did to him what they wished; so also shall the Son of man suffer at their hands.
13 Pamenepo ophunzira anazindikira kuti amawawuza za Yohane Mʼbatizi.
Then, the disciples understood that he spoke to them of John the Immerser.
14 Atafika ku gulu la anthu, munthu wina anamuyandikira Yesu ndi kugwada pamaso pake.
And when they had come to the multitude, there came to him a man who knelt to him,
15 Iye anati, “Ambuye, muchitireni chifundo mwana wanga akudwala matenda akugwa ndipo akuvutika kwambiri. Kawirikawiri iye amagwa pa moto kapena mʼmadzi.
and said: Lord, have mercy on my son; for he is a lunatic, and suffers grievously; for he often falls into the fire, and often into the water.
16 Ine ndinabwera naye kwa ophunzira anu koma alephera kumuchiritsa.”
And I brought him to thy disciples, and they were not able to cure him.
17 Yesu anayankha nati, “Haa, mʼbado wosakhulupirira ndi wokhota maganizo! Kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Ndidzapirira nanu mpaka liti? Bwera nayeni kwa Ine mnyamatayo.”
Jesus answered and said: O faithless and perverse generation, how long shall I be with you? How long shall I bear with you? Bring him hither to me.
18 Yesu anadzudzula chiwandacho ndipo chinatuluka mwa mnyamatayo ndipo anachira nthawi yomweyo.
And Jesus rebuked the demon, and he came out of him: and the child was cured from that hour.
19 Pamenepo ophunzira anabwera kwa Yesu mwamseri ndi kumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani ife tinalephera kutulutsa chiwandacho?”
Then the disciples came to Jesus privately, and said: Why were we not able to cast him out?
20 Iye anayankha kuti, “Chifukwa inu muli ndi chikhulupiriro chachingʼono. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro monga kambewu ka mpiru, mukhoza kunena ndi phiri ili kuti, ‘Choka apa nupite apo,’ ndipo lidzachoka. Palibe kanthu kamene kadzakukanikani.
And Jesus said to them: Because of your unbelief. For verily I say to you, If you have faith like a grain of mustard-seed, you shall say to this mountain, Be removed from this place to that, and it shall be removed: and nothing shall be impossible for you.
21 Chiwanda cha mtundu uwu sichingachoke chabe koma ndi pemphero ndi kusala kudya.”
But this kind does not go out but by prayer and fasting.
22 Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Iye anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.
And as they were making their journey in Galilee, Jesus said to them: The Son of man is about to be delivered into the hands of men;
23 Iwo adzamupha koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.” Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chisoni.
and they will kill him, and on the third day he will be raised again. And they were very sad.
24 Yesu ndi ophunzira ake atafika ku Kaperenawo, wolandira msonkho wa ku Nyumba ya Mulungu anabwera kwa Petro namufunsa kuti, “Kodi aphunzitsi anu sapereka msonkho wa Nyumba ya Mulungu?”
And when they had come into Capernaum, those who collected the didrachma came to Peter, and said: Does not your teacher pay the didrachma?
25 Iye anayankha kuti, “Inde amapereka.” Petro atalowa mʼnyumba, Yesu ndiye anayamba kuyankhula. Ndipo anamufunsa kuti, “Ukuganiza bwanji Simoni, kodi mafumu a dziko lapansi amalandira msonkho kuchokera kwa ana awo kapena kwa ena?”
He said: Yes. And when he had come into the house, before he had spoken, Jesus said to him: What think you, Simon? From whom do the kings of the earth collect tax or tribute? From their own sons, or from the sons of others?
26 Petro anayankha kuti, “Kuchokera kwa ena.” Yesu ananena kwa iye kuti, “Ndiye kuti ana sapereka.”
Peter said to him: From the sons of others. Jesus said to him: Then are their own sons free.
27 Koma kuti ife tisawakhumudwitse pita ku nyanja kaponye mbedza yako. Katenge nsomba imene ukayambe kuyikola; kayitsekule kukamwa ndipo ukapezamo ndalama. Katenge ndalamayo ndi kukapereka msonkho wanga ndi wanu.
But that we may give them no offense, go to the sea, and throw in a hook, and take the fish that comes up first; and when you have opened his mouth, you will find a stater; take that, and give to them for me and you.

< Mateyu 17 >