< Mateyu 16 >

1 Afarisi ndi Asaduki anabwera kwa Yesu ndi kumuyesa pomufunsa kuti awaonetse chizindikiro chochokera kumwamba.
Here the Pharisees and Sadducees came to Him; and, to make trial of Him, they asked Him to show them a sign in the sky.
2 Iye anayankha kuti, “Kunja kukamada, inu mumati, kudzakhala nyengo yabwino popeza thambo ndi lofiira.
He replied, "In the evening you say, 'It will be fine weather, for the sky is red;'
3 Ndipo mmawa mumati, ‘Lero kudzakhala mvula yamphepo popeza thambo ndi lofiira ndi mitambo ya mvula.’ Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a thambo koma simungathe kutanthauzira zizindikiro za nthawi.
and in the morning, 'It will be rough weather to-day, for the sky is red and murky.' You learn how to distinguish the aspect of the heavens, but the signs of the times you cannot.
4 Mʼbado woyipa ndi wachigololo umafuna chizindikiro chodabwitsa koma palibe ngakhale chimodzi chidzapatsidwa kupatula chizindikiro cha Yona.” Pamenepo Yesu anawasiya nachoka.
A wicked and faithless generation are eager for a sign; but none shall be given to them except the sign of Jonah." and He left them and went away.
5 Koma atawoloka nyanja, ophunzira anayiwala kutenga buledi.
When the disciples arrived at the other side of the Lake, they found that they had forgotten to bring any bread;
6 Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani, khalani tcheru ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
and when Jesus said to them, "See to it: beware of the yeast of the Pharisees and Sadducees,"
7 Iwo anakambirana pakati pawo za izi ndipo anati, “Ichi nʼchifukwa chakuti sitinatenge buledi aliyense.”
they reasoned among themselves, saying, "It is because we have not brought any bread."
8 Yesu atadziwa zokambirana zawo, anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukukambirana zakuti, ‘mulibe buledi?’ Inu achikhulupiriro chochepa.
Jesus perceived this and said, "Why are you reasoning among yourselves, you men of little faith, because you have no bread?
9 Kodi inu simukumvetsetsabe? Kodi simukukumbukira za buledi musanu amene anadya anthu 5,000 ndi madengu amene munadzaza?
Do you not yet understand? nor even remember the 5,000 and the five loaves, and how many basketfuls you carried away,
10 Kapena buledi musanu ndi muwiri amene anadya anthu 4,000, nanga ndi madengu angati amene munadzaza?
nor the 4,000 and the seven loaves, and how many hampers you carried away?
11 Zitheka bwanji kuti inu simukumvetsetsa kuti Ine sindinkayankhula nanu za buledi? Koma inu chenjerani ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
How is it you do not understand that it was not about bread that I spoke to you? But beware of the yeast of the Pharisees and Sadducees."
12 Kenaka iwo anazindikira kuti Iye samawawuza kuti achenjere ndi yisiti wa buledi koma ndi chiphunzitso cha Afarisi ndi Asaduki.
Then they perceived that He had not warned them against bread-yeast, but against the teaching of the Pharisees and Sadducees.
13 Yesu atafika ku chigawo cha Kaisareya Filipo, Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Kodi anthu amati Mwana wa Munthu ndi ndani?”
When He arrived in the neighbourhood of Caesarea Philippi, Jesus questioned His disciples. "Who do people say that the Son of Man is?" He asked.
14 Iwo anayankha kuti, “Ena amati ndi Yohane Mʼbatizi; ena amati ndi Eliya; komanso ena amati Yeremiya kapena mmodzi wa aneneri.”
"Some say John the Baptist," they replied; "others Elijah; others Jeremiah or one of the Prophets."
15 Iye anafunsa kuti, “Nanga inuyo mumati ndine yani?”
"But you, who do you say that I am?" He asked again.
16 Simoni Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.”
"You," replied Simon Peter, "are the Christ, the Son of the ever-living God."
17 Yesu anati kwa iye, “Ndiwe wodala Simoni mwana wa Yona, popeza si munthu amene anakuwululira izi koma Atate anga akumwamba.
"Blessed are you, Simon Bar-jonah," said Jesus; "for mere human nature has not revealed this to you, but my Father in Heaven.
18 Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. (Hadēs g86)
And I declare to you that you are Peter, and that upon this Rock I will build my Church, and the might of Hades shall not triumph over it. (Hadēs g86)
19 Ine ndidzakupatsa makiyi a Ufumu wakumwamba, ndipo chilichonse chimene iwe udzachimanga pansi pano chidzamangidwanso kumwamba.”
I will give you the keys of the Kingdom of the Heavens; and whatever you bind on earth shall remain bound in Heaven, and whatever you loose on earth shall remain loosed in Heaven."
20 Pamenepo Iye anachenjeza ophunzira ake kuti asawuze wina aliyense kuti ndi Khristu.
Then He urged His disciples to tell no one that He was the Christ.
21 Kuyambira nthawi imeneyo Yesu anayamba kuwafotokozera ophunzira ake kuti Iye ayenera kupita ku Yerusalemu ndi kukazunzidwa kwambiri mʼmanja mwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo kuti ayenera kuphedwa, ndi kuti tsiku lachitatu adzaukitsidwa.
From this time Jesus began to explain to His disciples that He must go to Jerusalem, and suffer much cruelty from the Elders and the High Priests and the Scribes, and be put to death, and on the third day be raised to life again.
22 Petro anamutengera Iye pambali nayamba kumudzudzula kuti, “Dzichitireni chifundo Ambuye, sizingachitike kwa Inu ayi.”
Then Peter took Him aside and began taking Him to task. "Master," he said, "God forbid; this will not be your lot."
23 Yesu anatembenuka nati kwa Petro, “Choka pamaso panga Satana! Iwe ndi chokhumudwitsa kwa Ine; iwe suganizira zinthu za Mulungu koma zinthu za anthu.”
But He turned and said to Peter, "Get behind me, Adversary; you are a hindrance to me, because your thoughts are not God's thoughts, but men's."
24 Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Ngati wina aliyense abwera pambuyo panga ayenera kudzikana ndi kutenga mtanda wake ndi kunditsata Ine.
Then Jesus said to His disciples, "If any one desires to follow me, let him renounce self and take up his cross, and so be my follower.
25 Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupeza.
For whoever desires to save his life shall lose it, and whoever loses his life for my sake shall find it.
26 Kodi munthu adzapindula chiyani ngati atapeza zonse za dziko lapansi nataya moyo wake? Kapena munthu angapereke chiyani chosinthana ndi moyo wake?
Why, what benefit will it be to a man if he gains the whole world but forfeits his life? Or what shall a man give to buy back his life?
27 Pakuti Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate ake ndi angelo ake ndipo pamenepo Iye adzapereka mphotho kwa munthu mofanana ndi zimene anachita.
For the Son of Man is soon to come in the glory of the Father with His angels, and then will He requite every man according to his actions.
28 “Ine ndikuwuzani inu choonadi, ena amene akuyimirira pano sadzalawa imfa asanaone Mwana wa Munthu akudza mu ufumu.”
I solemnly tell you that some of those who are standing here will certainly not taste death till they have seen the Son of Man coming in His Kingdom."

< Mateyu 16 >