< Mateyu 14 >
1 Pa nthawi imeneyo Mfumu Herode anamva za mbiri ya Yesu.
Того ча́су прочув Ірод чотиривла́сник чутки́ про Ісуса,
2 Ndipo iye anati kwa antchito ake, “Uyu ndi Yohane Mʼbatizi; iye wauka kwa akufa! Ichi ndi chifukwa chake mphamvu zodabwitsa zikugwira ntchito mwa iye.”
і сказав своїм слу́гам: „Це Іван Христитель, — він із мертвих воскрес, і тому́ чуда тво́ряться ним“.
3 Pakuti Herode anamugwira Yohane ndi kumumanga ndipo anamuyika mʼndende chifukwa cha Herodia mkazi wa mʼbale wake Filipo.
Бо Ірод схопи́в був Івана, і зв'язав його, і посадив у в'язни́цю через Іродія́ду, дружи́ну брата свого Пилипа.
4 Chifukwa Yohane anakhala akunena kwa iye kuti, “Sichololedwa kwa inu kutenga mkaziyo.”
Бо до нього Іван говорив: „Не годи́ться тобі її мати! “
5 Herode anafuna kupha Yohane koma iye anaopa anthu chifukwa anamuyesa iye mneneri.
І хотів Ірод смерть заподі́яти йому, та боявся наро́ду, бо того за пророка вважали.
6 Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodia anavina pamaso pa anthu ndipo anasangalatsa kwambiri.
А як був день наро́дження Ірода, танцювала посеред гостей дочка Іродія́дина, та й Іродові догоди́ла.
7 Kotero Herode analonjeza ndi lumbiro kumupatsa chilichonse chimene mwanayo angamupemphe.
Тому́ під прися́гою він обіцявся їй дати, чого тільки попросить вона.
8 Ndipo atamupangira amayi ake anati, “Mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
А вона, за намовою матері своєї: „Дай мені — проказала — отут на полу́миску голову Івана Христителя!“
9 Mfumuyo inamva chisoni koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo amene anali pa phwando lake analamulira kuti chofuna chake chipatsidwe;
І цар засмутився, але́ через клятву та тих, хто сидів при столі з ним, звелів дати.
10 ndipo anakadula mutu wa Yohane mʼndende.
І послав стяти Івана в в'язни́ці.
11 Mutu wake anawubweretsa mʼmbale ndi kumupatsa mtsikanayo amene anawutengera kwa amayi ake.
І прине́сли на полу́мискові його голову, та й дали́ дівчині, а та відне́сла її своїй матері.
12 Ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo wake ndi kukawuyika mʼmanda. Pomwepo iwo anapita kukamuwuza Yesu.
А учні його прибули́, взяли тіло, і поховали його, та прийшли й сповістили Ісуса.
13 Yesu atamva zimene zinachitika, anachoka pa bwato mwachinsinsi kupita kumalo a yekha. Magulu a anthu atamva izi anamutsatira Iye poyenda pansi kuchokera ku mizinda.
Як Ісус те почув, Він відплив звідти чо́вном у місце пустинне й самотнє. І, прочувши, наро́д із міст пішов пі́шки за Ним.
14 Yesu atafika ku mtunda, ndi kuona gulu lalikulu la anthu, Iye anamva nawo chifundo ndipo anachiritsa odwala awo.
І, як вийшов Ісус, Він побачив багато наро́ду, — і змилосе́рдивсь над ними, і їхніх слаби́х уздоро́вив.
15 Kutayamba mdima, ophunzira anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kutchire ndipo kwayamba kale kuda. Awuzeni anthu azipita kuti afike ku midzi ndi kukadzigulira zakudya.”
А коли настав вечір, підійшли Його учні до Нього й сказали: „ Тут місце пустинне, і година вже пі́зня; відпусти наро́д, — хай по селах розі́йдуться, і куплять пожи́ви собі“.
16 Yesu anawayankha kuti, “Sikofunika kuti azipita. Inuyo muwapatse kanthu kuti adye.”
А Ісус їм сказав: „Непотрібно відхо́дити їм, — нагодуйте їх ви!“
17 Iwo anayankha kuti, “Tili ndi malofu asanu okha a buledi ndi nsomba ziwiri.”
Вони ж кажуть Йому: „Не маємо чим тут, — тільки п'я́теро хліба й дві рибі“.
18 Koma Iye anati, “Bweretsani kwa Ine.”
А Він відказав: „Принесіть Мені їх сюди“.
19 Analamula anthu kuti akhale pansi pa udzu ndipo anatenga buledi musanu ndi nsomba ziwiri nayangʼana kumwamba, nayamika nagawa bulediyo. Kenaka anapereka bulediyo kwa ophunzira ake ndipo ophunzirawo anagawira anthu.
І, звелівши на́товпові посідати на траві, Він узяв п'ятеро хліба й дві рибі, спогля́нув на небо, поблагословив й поламав ті хліби́, і дав учням, а учні наро́дові.
20 Onse anadya nakhuta ndipo ophunzira anatola zotsalira ndi kudzaza madengu khumi ndi awiri.
І всі їли й наси́тились, а з кусків позосталих назбирали двана́дцятеро повних кошів.
21 Chiwerengero cha amene anadya kupatulako amayi ndi ana chinali pafupifupi amuna 5,000.
Їдців же було мужа тисяч із п'ять, крім жіно́к і дітей.
22 Nthawi yomweyo anawawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita kutsidya lina pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita kwawo.
І зараз звелів Ісус учням до чо́вна сідати, і перепли́сти на той бік раніше Його, аж поки наро́д Він відпу́стить.
23 Atatha kuwawuza kuti azipita kwawo, Iye anakwera ku phiri yekha kukapemphera. Pamene kumada anali kumeneko yekha.
Відпусти́вши ж народ, Він на го́ру пішов помолитися насамоті́; і як вечір настав, був там Сам.
24 Pamenepo nʼkuti bwato litapita patali pangʼono kuchokera ku mtunda ndipo linavutika ndi mafunde chifukwa mphepo inkawomba mokumana nalo.
А чо́вен вже був на сере́дині моря, і кидали хвилі його, бо вітер зірвавсь супроти́вний.
25 Pa ora lachinayi usiku, Yesu anabwera kwa iwo akuyendabe pa nyanja.
А о четвертій сторо́жі нічній Ісус підійшов до них, іду́чи по морю.
26 Ophunzira atamuona akuyenda pa nyanja, anaopa nati, “Ndi mzukwa!” Ndipo analira chifukwa cha mantha.
Як побачили ж учні, що йде Він по морю, то настра́шилися та й казали: „Мара́!“І від стра́ху вони закричали...
27 Koma Yesu nthawi yomweyo anawawuza kuti, “Limbani mtima! Ndine, musaope.”
А Ісус до них зараз озвався й сказав: „Заспокойтесь, — це Я, не лякайтесь!“
28 Petro anayankha nati, “Ambuye ngati ndinu, mundiwuze ndibwere kuli inuko pa madzipo.”
Петро ж відповів і сказав: „Коли, Господи, Ти́ це, то звели, щоб прийшов я до Тебе по воді“.
29 Iye anati, “Bwera.” Pamenepo Petro anatuluka mʼbwato ndipo anayenda pa madzi kupita kwa Yesu.
А Він відказав йому: „Іди“. І, вилізши з чо́вна, Петро став іти по воді, і пішов до Ісуса.
30 Koma ataona mphepo, iye anachita mantha ndipo anayamba kumira, nafuwula nati, “Ambuye ndipulumutseni!”
Але, бачачи велику бурю, злякався, і зачав потопа́ти, і скричав: „Рятуй мене, Господи!“
31 Ndipo mofulumira Yesu anatambasula dzanja lake namugwira iye, nati, “Iwe wachikhulupiriro chochepa, bwanji unakayika?”
І зараз Ісус простяг руку й схопи́в його, і каже до нього: „Маловірний, чого́ усумни́вся?“
32 Ndipo atalowa mʼbwato mphepo inaleka.
Як до чо́вна ж вони ввійшли, буря вщу́хнула.
33 Pamenepo amene anali mʼbwato anamulambira Iye, nati, “Zoonadi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”
А приявні в чо́вні вклонились Йому та сказали: „Ти справді Син Божий!“
34 Atawoloka, anafika ku Genesareti.
Перепливши ж вони, прибули́ в землю Генісаре́тську.
35 Anthu akumeneko atamuzindikira Yesu, iwo anatumiza mawu kwa onse ozungulira deralo. Anthu anabwera ndi odwala awo onse kwa Iye.
А люди тієї місцевости, пізнавши Його, сповістили по всій тій око́лиці, і до Нього прине́сли всіх хворих.
36 Ndipo anamupempha alole kuti akhudze mphonje ya mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachiritsidwa.
І благали Його, щоб бодай доторкнутися кра́ю одежі Його. А хто доторкавсь, — уздоро́влений був.