< Mateyu 13 >

1 Tsiku lomwelo Yesu anatuluka mʼnyumba ndipo anakhala mʼmbali mwa nyanja.
aparañca tasmin dine yīśuḥ sadmano gatvā saritpate rodhasi samupaviveśa|
2 Magulu a anthu anasonkhana mozungulira ndipo Iye analowa mʼbwato nakhala pansi ndipo anthu onse anayimirira ku mtunda.
tatra tatsannidhau bahujanānāṁ nivahopasthiteḥ sa taraṇimāruhya samupāviśat, tena mānavā rodhasi sthitavantaḥ|
3 Pamenepo Iye anawawuza zinthu zambiri mʼmafanizo ndi kuti, “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake.
tadānīṁ sa dṛṣṭāntaistān itthaṁ bahuśa upadiṣṭavān| paśyata, kaścit kṛṣīvalo bījāni vaptuṁ bahirjagāma,
4 Akufesa, zina zinagwera mʼmbali mwa njira ndipo mbalame zinabwera ndi kuzidya.
tasya vapanakāle katipayabījeṣu mārgapārśve patiteṣu vihagāstāni bhakṣitavantaḥ|
5 Zina zinagwa pamalo a miyala pamene panalibe dothi lambiri. Zinamera mofulumira chifukwa panalibe dothi lambiri.
aparaṁ katipayabījeṣu stokamṛdyuktapāṣāṇe patiteṣu mṛdalpatvāt tatkṣaṇāt tānyaṅkuritāni,
6 Koma dzuwa litakwera, mbewu zinapserera ndipo zinawuma chifukwa zinalibe mizu.
kintu ravāvudite dagdhāni teṣāṁ mūlāpraviṣṭatvāt śuṣkatāṁ gatāni ca|
7 Mbewu zina zinagwa pa minga ndipo mingayo inayanga ndi kuzirepheretsa kukula.
aparaṁ katipayabījeṣu kaṇṭakānāṁ madhye patiteṣu kaṇṭakānyedhitvā tāni jagrasuḥ|
8 Koma mbewu zina zinagwa pa nthaka yabwino ndipo zinabala zipatso 100, zina 60 ndipo zinanso makumi atatu mwa zimene zinafesedwa.
aparañca katipayabījāni urvvarāyāṁ patitāni; teṣāṁ madhye kānicit śataguṇāni kānicit ṣaṣṭiguṇāni kānicit triṁśaguṁṇāni phalāni phalitavanti|
9 Amene ali ndi makutu amve.”
śrotuṁ yasya śrutī āsāte sa śṛṇuyāt|
10 Ophunzira anabwera kwa Iye ndikumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani Inu mukuyankhula kwa anthu mʼmafanizo?”
anantaraṁ śiṣyairāgatya so'pṛcchyata, bhavatā tebhyaḥ kuto dṛṣṭāntakathā kathyate?
11 Iye anayankha kuti, “Nzeru zakudziwa zinsinsi za ufumu wakumwamba zapatsidwa kwa inu koma osati kwa iwo.
tataḥ sa pratyavadat, svargarājyasya nigūḍhāṁ kathāṁ vedituṁ yuṣmabhyaṁ sāmarthyamadāyi, kintu tebhyo nādāyi|
12 Aliyense amene ali nazo adzapatsidwa zowonjezera ndipo iye adzakhala nazo zambiri. Aliyense amene alibe, ngakhale zimene ali nazo adzamulanda.
yasmād yasyāntike varddhate, tasmāyeva dāyiṣyate, tasmāt tasya bāhulyaṁ bhaviṣyati, kintu yasyāntike na varddhate, tasya yat kiñcanāste, tadapi tasmād ādāyiṣyate|
13 Ichi ndi chifukwa chake ndimayankhula kwa iwo mʼmafanizo: “Ngakhale akupenya koma saona, ngakhale akumva koma samvetsetsa kapena kuzindikira.
te paśyantopi na paśyanti, śṛṇvantopi na śṛṇvanti, budhyamānā api na budhyante ca, tasmāt tebhyo dṛṣṭāntakathā kathyate|
14 Mwa iwo zimene ananenera Yesaya zikwaniritsidwa: “‘Kumva mudzamva koma osamvetsetsa. Kupenya mudzapenya koma osaona kanthu.
yathā karṇaiḥ śroṣyatha yūyaṁ vai kintu yūyaṁ na bhotsyatha| netrairdrakṣyatha yūyañca parijñātuṁ na śakṣyatha| te mānuṣā yathā naiva paripaśyanti locanaiḥ| karṇai ryathā na śṛṇvanti na budhyante ca mānasaiḥ| vyāvarttiteṣu citteṣu kāle kutrāpi tairjanaiḥ| mattaste manujāḥ svasthā yathā naiva bhavanti ca| tathā teṣāṁ manuṣyāṇāṁ kriyante sthūlabuddhayaḥ| badhirībhūtakarṇāśca jātāśca mudritā dṛśaḥ|
15 Pakuti mtima wa anthu awa ndi wokanika, mʼmakutu mwawo ndi mogontha, ndipo atsinzina kuti asaone kanthu. Mwina angapenye ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka, Ineyo nʼkuwachiritsa.’
yadetāni vacanāni yiśayiyabhaviṣyadvādinā proktāni teṣu tāni phalanti|
16 Koma maso anu ndi odala chifukwa amapenya ndi makutu anu chifukwa amamva.
kintu yuṣmākaṁ nayanāni dhanyāni, yasmāt tāni vīkṣante; dhanyāśca yuṣmākaṁ śabdagrahāḥ, yasmāt tairākarṇyate|
17 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama anafuna kuona zimene inu mukupenya koma sanazione ndi kumva zimene inu mukumva koma sanazimve.
mayā yūyaṁ tathyaṁ vacāmi yuṣmābhi ryadyad vīkṣyate, tad bahavo bhaviṣyadvādino dhārmmikāśca mānavā didṛkṣantopi draṣṭuṁ nālabhanta, punaśca yūyaṁ yadyat śṛṇutha, tat te śuśrūṣamāṇā api śrotuṁ nālabhanta|
18 “Tamverani tsono zimene fanizo la wofesa litanthauza:
kṛṣīvalīyadṛṣṭāntasyārthaṁ śṛṇuta|
19 Pamene aliyense akumva uthenga wa ufumu koma sawuzindikira, woyipayo amabwera ndi kuchotsa zimene zafesedwa mu mtima mwake. Iyi ndi mbewu yofesedwa mʼmbali mwa njira.
mārgapārśve bījānyuptāni tasyārtha eṣaḥ, yadā kaścit rājyasya kathāṁ niśamya na budhyate, tadā pāpātmāgatya tadīyamanasa uptāṁ kathāṁ haran nayati|
20 Zimene zinafesedwa pa malo amiyala ndi munthu amene amamva mawu ndi kuwalandira msanga ndi chimwemwe.
aparaṁ pāṣāṇasthale bījānyuptāni tasyārtha eṣaḥ; kaścit kathāṁ śrutvaiva harṣacittena gṛhlāti,
21 Koma popeza alibe muzu, iwo amakhala nthawi yochepa. Pamene vuto kapena zunzo libwera chifukwa cha mawu, iye amagwa mofulumira.
kintu tasya manasi mūlāpraviṣṭatvāt sa kiñcitkālamātraṁ sthirastiṣṭhati; paścāta tatkathākāraṇāt kopi klestāḍanā vā cet jāyate, tarhi sa tatkṣaṇād vighnameti|
22 Zimene zinafesedwa pakati pa minga, ndi munthu amene amamva mawu koma nkhawa za moyo uno ndi chinyengo cha chuma zimalepheretsa mawuwo kuti abale chipatso. (aiōn g165)
aparaṁ kaṇṭakānāṁ madhye bījānyuptāni tadartha eṣaḥ; kenacit kathāyāṁ śrutāyāṁ sāṁsārikacintābhi rbhrāntibhiśca sā grasyate, tena sā mā viphalā bhavati| (aiōn g165)
23 Koma zimene zinafesedwa pa nthaka yabwino, ndi munthu amene amamva mawu ndipo amawazindikira. Iye amabala zipatso zokwanira 100, zina 60 ndipo zinanso makumi atatu mwa zimene zinafesedwa.”
aparam urvvarāyāṁ bījānyuptāni tadartha eṣaḥ; ye tāṁ kathāṁ śrutvā vudhyante, te phalitāḥ santaḥ kecit śataguṇāni kecita ṣaṣṭiguṇāni kecicca triṁśadguṇāni phalāni janayanti|
24 Yesu anawawuza fanizo lina kuti: “Ufumu wakumwamba ufanana ndi munthu amene anafesa mbewu zabwino mʼmunda mwake.
anantaraṁ soparāmekāṁ dṛṣṭāntakathāmupasthāpya tebhyaḥ kathayāmāsa; svargīyarājyaṁ tādṛśena kenacid gṛhasthenopamīyate, yena svīyakṣetre praśastabījānyaupyanta|
25 Koma aliyense akugona usiku mdani wake anabwera ndi kufesa namsongole pakati pa tirigu ndipo anachoka.
kintu kṣaṇadāyāṁ sakalalokeṣu supteṣu tasya ripurāgatya teṣāṁ godhūmabījānāṁ madhye vanyayavamabījānyuptvā vavrāja|
26 Pamene tirigu anamera ndi kutulutsa ngala, namsongole anaonekanso.
tato yadā bījebhyo'ṅkarā jāyamānāḥ kaṇiśāni ghṛtavantaḥ; tadā vanyayavasānyapi dṛśyamānānyabhavan|
27 “Antchito ake anabwera kwa iye ndi kuti, ‘Bwana, kodi simunafese mbewu zabwino mʼmunda mwanu? Nanga namsongole wachokera kuti?’
tato gṛhasthasya dāseyā āgamya tasmai kathayāñcakruḥ, he maheccha, bhavatā kiṁ kṣetre bhadrabījāni naupyanta? tathātve vanyayavasāni kṛta āyan?
28 “Iye anayankha kuti, ‘Ndi mdani amene anachita izi.’ “Antchito anamufunsa iye kuti, ‘Kodi mufuna kuti tipite tikamuzule?’
tadānīṁ tena te pratigaditāḥ, kenacit ripuṇā karmmadamakāri| dāseyāḥ kathayāmāsuḥ, vayaṁ gatvā tānyutpāyya kṣipāmo bhavataḥ kīdṛśīcchā jāyate?
29 “Iye anakana nati, ‘Ayi. Chifukwa pamene mukuzula namsongoleyo mwina inu mungazulire pamodzi ndi tirigu.
tenāvādi, nahi, śaṅke'haṁ vanyayavasotpāṭanakāle yuṣmābhistaiḥ sākaṁ godhūmā apyutpāṭiṣyante|
30 Zisiyeni zonse zikulire pamodzi mpaka nthawi yokolola. Pa nthawi imeneyo ndidzawuza okolola kuti: Poyamba sonkhanitsani namsongole ndi kumumanga mʼmitolo kuti atenthedwe, kenaka sonkhanitsani tirigu ndi kumuyika mʼnkhokwe yanga.’”
ataḥ śsyakarttanakālaṁ yāvad ubhayānyapi saha varddhantāṁ, paścāt karttanakāle karttakān vakṣyāmi, yūyamādau vanyayavasāni saṁgṛhya dāhayituṁ vīṭikā badvvā sthāpayata; kintu sarvve godhūmā yuṣmābhi rbhāṇḍāgāraṁ nītvā sthāpyantām|
31 Iye anawawuza fanizo lina kuti, “Ufumu wakumwamba uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake.
anantaraṁ soparāmekāṁ dṛṣṭāntakathāmutthāpya tebhyaḥ kathitavān kaścinmanujaḥ sarṣapabījamekaṁ nītvā svakṣetra uvāpa|
32 Ngakhale mbewuyi ndi yayingʼono mwa mbewu zanu zonse za mʼmunda, imakula ndi kukhala mtengo kotero kuti mbalame zamlengalenga zimabwera ndi kupumula mʼnthambi zake.”
sarṣapabījaṁ sarvvasmād bījāt kṣudramapi sadaṅkuritaṁ sarvvasmāt śākāt bṛhad bhavati; sa tādṛśastaru rbhavati, yasya śākhāsu nabhasaḥ khagā āgatya nivasanti; svargīyarājyaṁ tādṛśasya sarṣapaikasya samam|
33 Iye anawawuzanso fanizo lina nati: “Ufumu wakumwamba ufanana ndi yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza mu ufa wambiri mpaka wonse unafufuma.”
punarapi sa upamākathāmekāṁ tebhyaḥ kathayāñcakāra; kācana yoṣit yat kiṇvamādāya droṇatrayamitagodhūmacūrṇānāṁ madhye sarvveṣāṁ miśrībhavanaparyyantaṁ samācchādya nidhattavatī, tatkiṇvamiva svargarājyaṁ|
34 Yesu anayankhula zinthu zonsezi kwa gulu la anthu mʼmafanizo ndipo Iye sananene kalikonse kwa iwo osagwiritsa ntchito fanizo.
itthaṁ yīśu rmanujanivahānāṁ sannidhāvupamākathābhiretānyākhyānāni kathitavān upamāṁ vinā tebhyaḥ kimapi kathāṁ nākathayat|
35 Kotero zinakwaniritsidwa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri kuti, “Ndidzatsekula pakamwa panga ndi mafanizo, ndidzawulula zinthu zobisika chiyambire kukhazikidwa kwa dziko lapansi.”
etena dṛṣṭāntīyena vākyena vyādāya vadanaṁ nijaṁ| ahaṁ prakāśayiṣyāmi guptavākyaṁ purābhavaṁ| yadetadvacanaṁ bhaviṣyadvādinā proktamāsīt, tat siddhamabhavat|
36 Kenaka Iye anasiya gulu la anthu ndi kukalowa mʼnyumba. Ophunzira ake anapita kwa Iye nati, “Timasulireni fanizo la namsongole mʼmunda.”
sarvvān manujān visṛjya yīśau gṛhaṁ praviṣṭe tacchiṣyā āgatya yīśave kathitavantaḥ, kṣetrasya vanyayavasīyadṛṣṭāntakathām bhavāna asmān spaṣṭīkṛtya vadatu|
37 Iye anayankha nati, “Munthu amene anafesa mbewu yabwino ndi Mwana wa Munthu.
tataḥ sa pratyuvāca, yena bhadrabījānyupyante sa manujaputraḥ,
38 Munda ndi dziko lapansi ndipo mbewu yabwino ndi ana a ufumu. Namsongole ndi ana a woyipayo.
kṣetraṁ jagat, bhadrabījānī rājyasya santānāḥ,
39 Ndipo amene anafesa namsongole ndi Satana. Kukolola ndiko kutha kwa dzikoli ndipo otuta ndi angelo. (aiōn g165)
vanyayavasāni pāpātmanaḥ santānāḥ| yena ripuṇā tānyuptāni sa śayatānaḥ, karttanasamayaśca jagataḥ śeṣaḥ, karttakāḥ svargīyadūtāḥ| (aiōn g165)
40 “Monga momwe namsongole azulidwa ndi kutenthedwa ndi moto, momwemonso kudzakhala pakutha kwa dziko. (aiōn g165)
yathā vanyayavasāni saṁgṛhya dāhyante, tathā jagataḥ śeṣe bhaviṣyati; (aiōn g165)
41 Mwana wa Munthu adzatumiza angelo ake ndipo iwo adzachotsa mu ufumu wake chilichonse chochimwitsa ndi onse amene amachita zoyipa.
arthāt manujasutaḥ svāṁyadūtān preṣayiṣyati, tena te ca tasya rājyāt sarvvān vighnakāriṇo'dhārmmikalokāṁśca saṁgṛhya
42 Adzawaponya mʼngʼanjo yamoto kumene kudzakhala kulira ndi kukuta mano.
yatra rodanaṁ dantagharṣaṇañca bhavati, tatrāgnikuṇḍe nikṣepsyanti|
43 Pamenepo olungama adzawala ngati dzuwa mu ufumu wa Atate awo. Amene ali ndi makutu amve.”
tadānīṁ dhārmmikalokāḥ sveṣāṁ pitū rājye bhāskara̮iva tejasvino bhaviṣyanti| śrotuṁ yasya śrutī āsāte, ma śṛṇuyāt|
44 “Ufumu wakumwamba ufanana ndi chuma chobisika mʼmunda. Munthu atachipeza anachibisanso ndipo ndi chimwemwe anapita nakagulitsa zonse anali nazo, nakagula mundawo.
aparañca kṣetramadhye nidhiṁ paśyan yo gopayati, tataḥ paraṁ sānando gatvā svīyasarvvasvaṁ vikrīya ttakṣetraṁ krīṇāti, sa iva svargarājyaṁ|
45 “Komanso Ufumu wakumwamba ufanana ndi wogulitsa malonda amene amafuna ngale zabwino.
anyañca yo vaṇik uttamāṁ muktāṁ gaveṣayan
46 Atapeza imodzi ya mtengowapatali, iye anapita nakagulitsa chilichonse anali nacho ndi kukayigula.”
mahārghāṁ muktāṁ vilokya nijasarvvasvaṁ vikrīya tāṁ krīṇāti, sa iva svargarājyaṁ|
47 “Komanso Ufumu wakumwamba ufanana ndi khoka limene linaponyedwa mʼnyanja ndipo linakola mitundu yonse ya nsomba.
punaśca samudro nikṣiptaḥ sarvvaprakāramīnasaṁgrāhyānāya̮iva svargarājyaṁ|
48 Litadzaza, asodzi analikokera ku mtunda. Pomwepo anakhala pansi nasonkhanitsa nsomba zabwino mʼmadengu koma zoyipa anazitaya.
tasmin ānāye pūrṇe janā yathā rodhasyuttolya samupaviśya praśastamīnān saṁgrahya bhājaneṣu nidadhate, kutsitān nikṣipanti;
49 Umu ndi mmene kudzakhalira pakutha kwa dziko. Angelo adzabwera ndi kulekanitsa oyipa ndi olungama. (aiōn g165)
tathaiva jagataḥ śeṣe bhaviṣyati, phalataḥ svargīyadūtā āgatya puṇyavajjanānāṁ madhyāt pāpinaḥ pṛthak kṛtvā vahnikuṇḍe nikṣepsyanti, (aiōn g165)
50 Ndipo oyipa adzawaponya mʼngʼanjo ya moto kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
tatra rodanaṁ dantai rdantagharṣaṇañca bhaviṣyataḥ|
51 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi mwamvetsetsa zonsezi?” Iwo anayankha kuti, “Inde.”
yīśunā te pṛṣṭā yuṣmābhiḥ kimetānyākhyānānyabudhyanta? tadā te pratyavadan, satyaṁ prabho|
52 Iye anawawuza kuti, “Chifukwa chake mphunzitsi aliyense wa malamulo amene walangizidwa za ufumu wakumwamba ali ngati mwini nyumba amene amatulutsa chuma chatsopano komanso chakale.”
tadānīṁ sa kathitavān, nijabhāṇḍāgārāt navīnapurātanāni vastūni nirgamayati yo gṛhasthaḥ sa iva svargarājyamadhi śikṣitāḥ svarva upadeṣṭāraḥ|
53 Yesu atatsiriza mafanizowa anachoka kumeneko.
anantaraṁ yīśuretāḥ sarvvā dṛṣṭāntakathāḥ samāpya tasmāt sthānāt pratasthe| aparaṁ svadeśamāgatya janān bhajanabhavana upadiṣṭavān;
54 Atafika ku mudzi kwawo anayamba kuphunzitsa mʼmasunagoge awo ndipo iwo anadabwa nati, “Munthu uyu anayitenga kuti nzeru iyi ndi mphamvu zodabwitsazi?
te vismayaṁ gatvā kathitavanta etasyaitādṛśaṁ jñānam āścaryyaṁ karmma ca kasmād ajāyata?
55 Kodi si mwana wa wopala matabwa? Kodi dzina la amayi ake si Mariya ndipo kodi abale ake si Yakobo, Yosefe, Simoni ndi Yudasi?
kimayaṁ sūtradhārasya putro nahi? etasya mātu rnāma ca kiṁ mariyam nahi? yākub-yūṣaph-śimon-yihūdāśca kimetasya bhrātaro nahi?
56 Kodi alongo ake onse sali ndi ife? Tsono ndi kuti kumene anazitenga zinthu izi?”
etasya bhaginyaśca kimasmākaṁ madhye na santi? tarhi kasmādayametāni labdhavān? itthaṁ sa teṣāṁ vighnarūpo babhūva;
57 Ndipo iwo anakhumudwa chifukwa cha Iye. Koma Yesu anawawuza kuti, “Mneneri sapatsidwa ulemu ku mudzi kwawo ndi ku nyumba kwawo.”
tato yīśunā nigaditaṁ svadeśīyajanānāṁ madhyaṁ vinā bhaviṣyadvādī kutrāpyanyatra nāsammānyo bhavatī|
58 Ndipo Iye sanachite zodabwitsa zambiri kumeneko chifukwa cha kusowa kwa chikhulupiriro kwawo.
teṣāmaviśvāsahetoḥ sa tatra sthāne bahvāścaryyakarmmāṇi na kṛtavān|

< Mateyu 13 >