< Mateyu 13 >
1 Tsiku lomwelo Yesu anatuluka mʼnyumba ndipo anakhala mʼmbali mwa nyanja.
På hin dag gik Jesus ud af Huset og satte sig ved Søen.
2 Magulu a anthu anasonkhana mozungulira ndipo Iye analowa mʼbwato nakhala pansi ndipo anthu onse anayimirira ku mtunda.
Og store Skarer samlede sig om ham, så han gik om Bord i et Skib og satte sig; og hele Skaren stod på Strandbredden.
3 Pamenepo Iye anawawuza zinthu zambiri mʼmafanizo ndi kuti, “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake.
Og han talte meget til dem i Lignelser og sagde: "Se, en Sædemand gik ud at så.
4 Akufesa, zina zinagwera mʼmbali mwa njira ndipo mbalame zinabwera ndi kuzidya.
Og idet han såede, faldt noget ved Vejen; og Fuglene kom og åde det op.
5 Zina zinagwa pamalo a miyala pamene panalibe dothi lambiri. Zinamera mofulumira chifukwa panalibe dothi lambiri.
Og noget faldt på Stengrund, hvor det ikke havde megen Jord; og det voksede straks op, fordi det ikke havde dyb Jord.
6 Koma dzuwa litakwera, mbewu zinapserera ndipo zinawuma chifukwa zinalibe mizu.
Men da Solen kom op, blev det svedet af, og fordi det ikke havde Rod, visnede det.
7 Mbewu zina zinagwa pa minga ndipo mingayo inayanga ndi kuzirepheretsa kukula.
Og noget faldt iblandt Torne; og Tornene voksede op og kvalte det.
8 Koma mbewu zina zinagwa pa nthaka yabwino ndipo zinabala zipatso 100, zina 60 ndipo zinanso makumi atatu mwa zimene zinafesedwa.
Og noget faldt i god Jord og bar Frugt, noget hundrede, noget tresindstyve, noget tredive Fold.
9 Amene ali ndi makutu amve.”
Den, som har Øren, han høre!"
10 Ophunzira anabwera kwa Iye ndikumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani Inu mukuyankhula kwa anthu mʼmafanizo?”
Og Disciplene gik hen og sagde til ham: "Hvorfor taler du til dem i Lignelser?"
11 Iye anayankha kuti, “Nzeru zakudziwa zinsinsi za ufumu wakumwamba zapatsidwa kwa inu koma osati kwa iwo.
Men han svarede og sagde til dem: "Fordi det er eder givet at kende Himmeriges Riges Hemmeligheder; men dem er det ikke givet.
12 Aliyense amene ali nazo adzapatsidwa zowonjezera ndipo iye adzakhala nazo zambiri. Aliyense amene alibe, ngakhale zimene ali nazo adzamulanda.
Thi den, som har, ham skal der gives, og han skal få Overflod; men den, som ikke har, fra ham skal endog det tages, som han har.
13 Ichi ndi chifukwa chake ndimayankhula kwa iwo mʼmafanizo: “Ngakhale akupenya koma saona, ngakhale akumva koma samvetsetsa kapena kuzindikira.
Derfor taler jeg til dem i Lignelser, fordi de skønt seende dog ikke se, og hørende dog ikke høre og forstå ikke heller.
14 Mwa iwo zimene ananenera Yesaya zikwaniritsidwa: “‘Kumva mudzamva koma osamvetsetsa. Kupenya mudzapenya koma osaona kanthu.
Og på dem opfyldes Esajas's Profeti, som siger: Med eders Øren skulle I høre og dog ikke forstå og se med eders Øjne og dog ikke se.
15 Pakuti mtima wa anthu awa ndi wokanika, mʼmakutu mwawo ndi mogontha, ndipo atsinzina kuti asaone kanthu. Mwina angapenye ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi nzeru zawo ndi kutembenuka, Ineyo nʼkuwachiritsa.’
Thi dette Folks Hjerte er blevet sløvet, og med Ørene høre de tungt, og deres Øjne have de tillukket, for at de ikke skulle se med Øjnene og høre med Ørene og forstå med Hjertet og omvende sig, på jeg kunde helbrede dem.
16 Koma maso anu ndi odala chifukwa amapenya ndi makutu anu chifukwa amamva.
Men salige ere eders Øjne, fordi de se, og eders Øren, fordi de høre.
17 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama anafuna kuona zimene inu mukupenya koma sanazione ndi kumva zimene inu mukumva koma sanazimve.
Thi sandelig, siger jeg eder, mange Profeter og retfærdige attråede at se, hvad I se, og så det ikke; og at høre, hvad I høre, og hørte det ikke.
18 “Tamverani tsono zimene fanizo la wofesa litanthauza:
Så hører nu I Lignelsen om Sædemanden!
19 Pamene aliyense akumva uthenga wa ufumu koma sawuzindikira, woyipayo amabwera ndi kuchotsa zimene zafesedwa mu mtima mwake. Iyi ndi mbewu yofesedwa mʼmbali mwa njira.
Når nogen hører Rigets Ord og ikke forstår det, da kommer den Onde og river det bort, som er sået i hans Hjerte; denne er det, som blev sået ved Vejen.
20 Zimene zinafesedwa pa malo amiyala ndi munthu amene amamva mawu ndi kuwalandira msanga ndi chimwemwe.
Men det, som blev sået på Stengrund, er den, som hører Ordet og straks modtager det med Glæde.
21 Koma popeza alibe muzu, iwo amakhala nthawi yochepa. Pamene vuto kapena zunzo libwera chifukwa cha mawu, iye amagwa mofulumira.
Men han har ikke Rod i sig og holder kun ud til en Tid; men når der kommer Trængsel eller Forfølgelse for Ordets Skyld, forarges han straks.
22 Zimene zinafesedwa pakati pa minga, ndi munthu amene amamva mawu koma nkhawa za moyo uno ndi chinyengo cha chuma zimalepheretsa mawuwo kuti abale chipatso. (aiōn )
Men det, som blev sået iblandt Torne, er den, som hører Ordet, og Verdens Bekymring og Rigdommens Forførelse kvæler Ordet, og det bliver uden Frugt. (aiōn )
23 Koma zimene zinafesedwa pa nthaka yabwino, ndi munthu amene amamva mawu ndipo amawazindikira. Iye amabala zipatso zokwanira 100, zina 60 ndipo zinanso makumi atatu mwa zimene zinafesedwa.”
Men det, som blev sået i god Jord, er den, som hører Ordet og forstår det, og som så bærer Frugt, en hundrede, en tresindstyve, en tredive Fold."
24 Yesu anawawuza fanizo lina kuti: “Ufumu wakumwamba ufanana ndi munthu amene anafesa mbewu zabwino mʼmunda mwake.
En anden Lignelse fremsatte han for dem og sagde: "Himmeriges Rige lignes ved et Menneske, som såede god Sæd i sin Mark.
25 Koma aliyense akugona usiku mdani wake anabwera ndi kufesa namsongole pakati pa tirigu ndipo anachoka.
Men medens Folkene sov, kom hans Fjende og såede Ugræs iblandt Hveden og gik bort.
26 Pamene tirigu anamera ndi kutulutsa ngala, namsongole anaonekanso.
Men da Sæden spirede frem og bar Frugt, da kom også Ugræsset til Syne.
27 “Antchito ake anabwera kwa iye ndi kuti, ‘Bwana, kodi simunafese mbewu zabwino mʼmunda mwanu? Nanga namsongole wachokera kuti?’
Og Husbondens Tjenere kom til ham og sagde: Herre, såede du ikke god Sæd i din Mark? Hvor har den da fået Ugræsset fra?
28 “Iye anayankha kuti, ‘Ndi mdani amene anachita izi.’ “Antchito anamufunsa iye kuti, ‘Kodi mufuna kuti tipite tikamuzule?’
Men han sagde til dem: Det har et fjendsk Menneske gjort. Da sige Tjenerne til ham: Vil du da, at vi skulle gå hen og sanke det sammen?
29 “Iye anakana nati, ‘Ayi. Chifukwa pamene mukuzula namsongoleyo mwina inu mungazulire pamodzi ndi tirigu.
Men han siger: Nej, for at I ikke, når I sanke Ugræsset sammen, skulle rykke Hveden op tillige med det.
30 Zisiyeni zonse zikulire pamodzi mpaka nthawi yokolola. Pa nthawi imeneyo ndidzawuza okolola kuti: Poyamba sonkhanitsani namsongole ndi kumumanga mʼmitolo kuti atenthedwe, kenaka sonkhanitsani tirigu ndi kumuyika mʼnkhokwe yanga.’”
Lader dem begge vokse tilsammen indtil Høsten; og i Høstens Tid vil jeg sige til Høstfolkene: Sanker først Ugræsset sammen og binder det i Knipper for at brænde det, men samler Hveden i min Lade!"
31 Iye anawawuza fanizo lina kuti, “Ufumu wakumwamba uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake.
En anden Lignelse fremsatte han for dem og sagde: "Himmeriges Rige ligner et Sennepskorn, som en Mand tog og såede i sin Mark.
32 Ngakhale mbewuyi ndi yayingʼono mwa mbewu zanu zonse za mʼmunda, imakula ndi kukhala mtengo kotero kuti mbalame zamlengalenga zimabwera ndi kupumula mʼnthambi zake.”
Dette er vel mindre end alt andet Frø; men når det er vokset op, er det støre end Urterne og bliver et Træ, så at Himmelens Fugle komme og bygge Rede i dets Grene."
33 Iye anawawuzanso fanizo lina nati: “Ufumu wakumwamba ufanana ndi yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza mu ufa wambiri mpaka wonse unafufuma.”
En anden Lignelse talte han til dem: "Himmeriges Rige ligner en Surdejg, som en Kvinde tog og lagde ned i tre Mål Mel, indtil det blev syret alt sammen."
34 Yesu anayankhula zinthu zonsezi kwa gulu la anthu mʼmafanizo ndipo Iye sananene kalikonse kwa iwo osagwiritsa ntchito fanizo.
Alt dette talte Jesus til Skarerne i Lignelser, og uden Lignelse talte han intet til dem,
35 Kotero zinakwaniritsidwa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri kuti, “Ndidzatsekula pakamwa panga ndi mafanizo, ndidzawulula zinthu zobisika chiyambire kukhazikidwa kwa dziko lapansi.”
for at det skulde opfyldes, som er talt ved Profeten, der siger: "Jeg vil oplade min Mund i Lignelser; jeg vil udsige det, som har været skjult fra Verdens Grundlæggelse."
36 Kenaka Iye anasiya gulu la anthu ndi kukalowa mʼnyumba. Ophunzira ake anapita kwa Iye nati, “Timasulireni fanizo la namsongole mʼmunda.”
Da forlod han Skarerne og gik ind i Huset; og hans Disciple kom til ham og sagde: "Forklar os Lignelsen om Ugræsset på Marken!"
37 Iye anayankha nati, “Munthu amene anafesa mbewu yabwino ndi Mwana wa Munthu.
Men han svarede og sagde: "Den, som sår den gode Sæd, er Menneskesønnen,
38 Munda ndi dziko lapansi ndipo mbewu yabwino ndi ana a ufumu. Namsongole ndi ana a woyipayo.
og Marken er Verden, og den gode Sæd er Rigets Børn, men Ugræsset er den Ondes Børn,
39 Ndipo amene anafesa namsongole ndi Satana. Kukolola ndiko kutha kwa dzikoli ndipo otuta ndi angelo. (aiōn )
og Fjenden, som såede det, er Djævelen; og Høsten er Verdens Ende; og Høstfolkene ere Engle. (aiōn )
40 “Monga momwe namsongole azulidwa ndi kutenthedwa ndi moto, momwemonso kudzakhala pakutha kwa dziko. (aiōn )
Ligesom nu Ugræsset sankes sammen og opbrændes med Ild, således skal det ske ved Verdens Ende. (aiōn )
41 Mwana wa Munthu adzatumiza angelo ake ndipo iwo adzachotsa mu ufumu wake chilichonse chochimwitsa ndi onse amene amachita zoyipa.
Menneskesønnen skal udsende sine Engle, og de skulle sanke ud af hans Rige alle Forargelserne og dem, som gøre Uret;
42 Adzawaponya mʼngʼanjo yamoto kumene kudzakhala kulira ndi kukuta mano.
og de skulle kaste dem i Ildovnen; der skal være Gråd og Tænders Gnidsel.
43 Pamenepo olungama adzawala ngati dzuwa mu ufumu wa Atate awo. Amene ali ndi makutu amve.”
Da skulle de retfærdige skinne som Solen i deres Faders Rige. Den. som har Øren, han høre!
44 “Ufumu wakumwamba ufanana ndi chuma chobisika mʼmunda. Munthu atachipeza anachibisanso ndipo ndi chimwemwe anapita nakagulitsa zonse anali nazo, nakagula mundawo.
Himmeriges Rige ligner en Skat. som er skjult i en Mark, og en Mand fandt og skjulte den, og af Glæde over den går han hen og sælger alt, hvad han har, og køber den Mark.
45 “Komanso Ufumu wakumwamba ufanana ndi wogulitsa malonda amene amafuna ngale zabwino.
Atter ligner Himmeriges Rige en Købmand, som søgte efter skønne Perler;
46 Atapeza imodzi ya mtengowapatali, iye anapita nakagulitsa chilichonse anali nacho ndi kukayigula.”
og da han fandt een meget kostbar Perle, gik han hen og solgte alt, hvad han havde, og købte den.
47 “Komanso Ufumu wakumwamba ufanana ndi khoka limene linaponyedwa mʼnyanja ndipo linakola mitundu yonse ya nsomba.
Atter ligner Himmeriges Rige et Vod, som blev kastet i Havet og samlede Fisk af alle Slags.
48 Litadzaza, asodzi analikokera ku mtunda. Pomwepo anakhala pansi nasonkhanitsa nsomba zabwino mʼmadengu koma zoyipa anazitaya.
Og da det var blevet fuldt, drog man det op på Strandbredden og satte sig og sankede de gode sammen i Kar, men kastede de rådne ud.
49 Umu ndi mmene kudzakhalira pakutha kwa dziko. Angelo adzabwera ndi kulekanitsa oyipa ndi olungama. (aiōn )
Således skal det gå til ved Verdens Ende. Englene skulle gå ud og skille de onde fra de retfærdige (aiōn )
50 Ndipo oyipa adzawaponya mʼngʼanjo ya moto kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
og kaste dem i Ildovnen; der skal være Gråd og Tænders Gnidsel.
51 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi mwamvetsetsa zonsezi?” Iwo anayankha kuti, “Inde.”
Have I forstået alt dette?" De sige til ham: "Ja."
52 Iye anawawuza kuti, “Chifukwa chake mphunzitsi aliyense wa malamulo amene walangizidwa za ufumu wakumwamba ali ngati mwini nyumba amene amatulutsa chuma chatsopano komanso chakale.”
Men han sagde til dem: "Derfor er hver skriftklog, som er oplært for Himmeriges Rige, ligesom en Husbond, der tager nyt og gammelt frem af sit Forråd."
53 Yesu atatsiriza mafanizowa anachoka kumeneko.
Og det skete, da Jesus havde fuldendt disse Lignelser, drog han bort derfra.
54 Atafika ku mudzi kwawo anayamba kuphunzitsa mʼmasunagoge awo ndipo iwo anadabwa nati, “Munthu uyu anayitenga kuti nzeru iyi ndi mphamvu zodabwitsazi?
Og han kom til sin Fædrene by og lærte dem i deres Synagoge, så at de bleve slagne af Forundring og sagde: "Hvorfra har han denne Visdom og de kraftige Gerninger?
55 Kodi si mwana wa wopala matabwa? Kodi dzina la amayi ake si Mariya ndipo kodi abale ake si Yakobo, Yosefe, Simoni ndi Yudasi?
Er denne ikke Tømmermandens Søn? Hedder ikke hans Moder Maria og hans Brødre Jakob og Josef og Simon og Judas?
56 Kodi alongo ake onse sali ndi ife? Tsono ndi kuti kumene anazitenga zinthu izi?”
Og hans Søstre, ere de ikke alle hos os? Hvorfra har han alt dette?"
57 Ndipo iwo anakhumudwa chifukwa cha Iye. Koma Yesu anawawuza kuti, “Mneneri sapatsidwa ulemu ku mudzi kwawo ndi ku nyumba kwawo.”
Og de forargedes på ham. Men Jesus sagde til dem: "En Profet er ikke foragtet uden i sit eget Fædreland og i sit Hus,"
58 Ndipo Iye sanachite zodabwitsa zambiri kumeneko chifukwa cha kusowa kwa chikhulupiriro kwawo.
Og han gjorde ikke mange kraftige Gerninger der for deres Vantros Skyld.