< Mateyu 12 >

1 Pa nthawi imeneyo Yesu anadutsa pakati pa minda ya tirigu pa tsiku la Sabata. Ophunzira ake anamva njala nayamba kuthyola ngala za tirigu nʼkumadya.
در یکی از آن روزها، عیسی در روز شبّات با شاگردان خود از میان کشتزارهای گندم می‌گذشت. شاگردانش که گرسنه بودند، شروع به چیدن خوشه‌های گندم و خوردن دانه‌های آن کردند.
2 Afarisi ataona zimenezi anati kwa Iye, “Taonani! Ophunzira anu akuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata.”
اما فریسی‌ها وقتی این را دیدند، اعتراض‌کنان گفتند: «ببین، شاگردان تو با خوشه‌چینی در روز شبّات، احکام مذهبی را زیر پا می‌گذارند.»
3 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene anachita Davide pamene iye ndi anzake anamva njala?
عیسی در پاسخ فرمود: «مگر در کتب مقدّس نخوانده‌اید که وقتی داوود پادشاه و یارانش گرسنه بودند، چه کردند؟
4 Analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo iye ndi anzakewo anadya buledi wopatulika amene sikunali kololedwa kwa iwo kudya koma ansembe okha.
او وارد معبد شد و خودش و همراهانش با خوردن گِرده‌های نان حضور، احکام مذهبی را زیر پا گذاشتند، زیرا فقط کاهنان اجازه داشتند از آن نان بخورند.
5 Kodi simunawerenge mʼmalamulo kuti pa Sabata ansembe mʼNyumba ya Mulungu amaphwanya lamulo la Sabata komabe sawayesa olakwa?
یا مگر در توراتِ موسی نخوانده‌اید که کاهنانی که در معبد مشغول خدمت هستند، اجازه دارند حتی در روز شبّات نیز کار کنند؟
6 Ine ndikuwuzani kuti wamkulu kuposa Nyumba ya Mulunguyo ali pano.
به شما می‌گویم در اینجا کسی هست که از معبد نیز بزرگتر است.
7 Ngati mukanadziwa zomwe mawu awa atanthauza, ‘Ine ndifuna chifundo osati nsembe,’ inu simukanatsutsa osalakwa.
اما اگر معنی این جمله از کتب مقدّس را درک می‌کردید که می‌فرماید:”من از شما انتظار دارم رحم داشته باشید، نه اینکه قربانی تقدیم کنید“، در آن صورت، شاگردان مرا که خطایی نکرده‌اند محکوم نمی‌کردید.
8 Pakuti Mwana wa Munthu ndiye Mbuye wa Sabata.”
زیرا پسر انسان، صاحب اختیار شبّات نیز هست.»
9 Atachoka kumeneko anakalowa mʼsunagoge mwawo.
آنگاه عیسی به کنیسۀ آنها رفت،
10 Ndipo mʼmenemo munali munthu wolumala dzanja. Pofuna chifukwa chokamunenezera, iwo anamufunsa Yesu kuti, “Kodi nʼkololedwa kuchiritsa munthu tsiku la Sabata?”
و در آنجا مردی را دید که دستش از کار افتاده بود. فریسی‌ها از عیسی پرسیدند: «آیا شریعت به شخص اجازه می‌دهد در روز شبّات کسی را شفا دهد؟» البته آنها قصد داشتند از پاسخ او بهانه‌ای بیابند تا بر او اتهام وارد سازند.
11 Iye anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu ali ndi nkhosa nigwera mʼdzenje tsiku la Sabata, kodi simudzayigwira ndi kuyitulutsa kunja?
عیسی در پاسخ فرمود: «اگر یکی از شما گوسفندی داشته باشد که در روز شبّات در گودالی بیفتد، آیا برای بیرون آوردن آن، کاری انجام نخواهید داد؟
12 Nanga munthu sali oposa nkhosa kwambiri! Chifukwa chake nʼkololedwa kuchita zabwino pa Sabata.”
اما ارزش انسان چقدر بیشتر از گوسفند است! پس طبق شریعت انجام کار نیک در روز شبّات روا است!»
13 Pamenepo Yesu anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola ndipo linakhala monga linalili kale.
آنگاه به آن مرد گفت: «دستت را دراز کن!» و وقتی چنین کرد، آن دستش نیز مانند دست دیگرش سالم شد.
14 Koma Afarisi anatuluka kunja ndi kukonza njira yoti amuphere.
پس از آن فریسی‌ها بیرون رفتند و جلسه تشکیل دادند تا برای قتل او توطئه بچینند.
15 Podziwa zimenezi, Yesu anachoka kumalo amenewo. Ambiri anamutsata Iye ndipo anachiritsira odwala awo onse
اما عیسی که از توطئۀ آنان آگاه بود، آن ناحیه را ترک گفت، و عدهٔ زیادی به دنبال او روانه شدند. او تمام بیماران ایشان را شفا بخشید،
16 nawachenjeza kuti asamuwulule kuti yani.
اما با تأکید از آنها خواست تا به دیگران نگویند که او کیست.
17 Uku kunali kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,
و به این ترتیب، پیشگویی اشعیای نبی دربارۀ او به انجام رسید، که می‌فرماید:
18 “Taonani mnyamata wanga amene ndinamusankha, Wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye. Pa Iye ndidzayika Mzimu wanga, ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.
«این است خدمتگزار من، که او را برگزیده‌ام. او محبوب من است و مایۀ خشنودی من. روح خود را بر او خواهم نهاد، و او عدل و انصاف را به قومها اعلان خواهد کرد.
19 Sadzalimbana, sadzafuwula, ngakhale mmodzi sadzamva mawu ake mʼmakwalala.
او نخواهد جنگید و فریاد نخواهد زد و صدایش را در کوی و برزن بلند نخواهد کرد.
20 Bango lophwanyika sadzalithyola, ndi nyale yofuka sadzayizimitsa, kufikira Iye adzatumiza chiweruziro chikagonjetse.
نِیِ خردشده را نخواهد شکست، و شعلۀ شمعی را که سوسو می‌زند، خاموش نخواهد کرد. او سرانجام عدل و انصاف را به پیروزی خواهد رساند.
21 Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lake.”
و نامش مایهٔ امید همۀ قومها خواهد بود.»
22 Pomwepo anthu anabwera naye kwa Yesu munthu wogwidwa ndi chiwanda amene anali wosaona ndi wosamva ndipo Yesu anamuchiritsa kotero kuti atatha anayamba kumva ndi kuona.
سپس، مرد دیوزده‌ای را نزدش آوردند که هم کور بود و هم لال. عیسی او را شفا بخشید، به‌طوری که توانست هم حرف بزند و هم ببیند.
23 Anthu onse anadabwa ndipo anati, “Kodi uyu ndi kukhala mwana wa Davide?”
مردم همه تعجب کردند و گفتند: «آیا ممکن است که عیسی، همان پسر داوود و مسیح موعود باشد؟»
24 Koma Afarisi atamva zimenezi, anati, “Uyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mkulu wa ziwandazo.”
اما وقتی خبر این معجزه به گوش فریسیان رسید، گفتند: «او ارواح پلید را به قدرت شیطان، رئیس ارواح پلید، بیرون می‌راند.»
25 Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse ukagawanika mwa iwo udzawonongeka ndi mzinda uliwonse kapena banja likagawanika, mwa izo zokha sizidzayima.
عیسی از افکار ایشان آگاهی یافت و فرمود: «هر مملکتی که دچار جنگ داخلی شود، نابودی‌اش حتمی است. شهر یا خانه‌ای نیز که در آن در اثر دشمنی‌ها تفرقه ایجاد گردد، از هم فرو خواهد پاشید.
26 Ngati Satana atulutsa Satana, iye adzigawa yekha. Nanga ufumu wake ungayime bwanji?
حال اگر شیطان بخواهد شیطان را بیرون کند، به این معنی است که تجزیه شده و با خودش می‌جنگد. پس چگونه حکومتش پایدار خواهد ماند؟
27 Ndipo ngati Ine nditulutsa ziwanda ndi Belezebule, anthu anu amatulutsa ziwandazo ndi chiyani? Potero tsono adzakhala oweruza anu.
و اگر قدرت من از شیطان است، تکلیف مریدان شما چه خواهد شد، زیرا ایشان نیز ارواح پلید اخراج می‌کنند؟ از این رو، ایشان شما را به خاطر حرفی که زدید، محکوم خواهند ساخت!
28 Koma ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi Mzimu wa Mulungu, pamenepo ufumu wa Mulungu wafika pa inu.
اما اگر من به‌وسیلهٔ روح خدا، ارواح پلید را بیرون می‌کنم، پس بدانید که ملکوت خدا به میان شما آمده است.
29 “Kapenanso wina aliyense angathe bwanji kulowa mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kunyamulamo zinthu zake, sipokhapo atayamba wamanga munthu wa mphamvuyo? Pamenepo iye akhoza kuba mʼnyumbamo.
و نیز چگونه امکان دارد شخص به خانۀ مردی قوی مانند شیطان داخل شود و اموال او را غارت کند؟ فقط شخصی نیرومندتر از او می‌تواند چنین کند، کسی که بتواند او را ببندد و بعد خانه‌اش را غارت کند.
30 “Iye amene sali ndi Ine atsutsana nane ndipo iye amene sasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amamwaza.
«هر که با من نباشد، بر ضد من است، و هر که با من کار نکند، در واقع علیه من کار می‌کند.
31 Ndipo potero Ine ndikuwuzani inu, tchimo lililonse ndi cha mwano chilichonse zidzakhululukidwa kwa anthu koma chamwano cha pa Mzimu Woyera, sichidzakhululukidwa.
«پس به شما می‌گویم، هر نوع گناه و هر کفری قابل بخشایش است – به‌جز کفر به روح‌القدس که هرگز آمرزیده نخواهد شد.
32 Aliyense amene anena mawu otsutsana ndi Mwana wa Munthu adzakhululukidwa koma aliyense wonena motsutsana ndi Mzimu Woyera sadzakhululukidwa mu mʼbado uno kapena umene ukubwerawo. (aiōn g165)
هر سخنی که برضد پسر انسان گفته شود، قابل بخشایش است، اما هر که برضد روح‌القدس سخن گوید، هرگز آمرزیده نخواهد شد، نه در این دنیا، و نه در دنیای بعد. (aiōn g165)
33 “Mtengo wabwino umabala zipatso zabwino ndipo mtengo woyipa umabalanso zipatso zoyipa, pajatu mtengo umadziwika ndi zipatso zake.
«درخت را از میوه‌اش می‌توان شناخت. اگر درخت خوب باشد، میوه‌اش نیز خوب خواهد بود. و اگر درخت بد باشد، میوه‌اش هم بد خواهد بود.
34 Ana anjoka inu, woyipa inu, mungathe bwanji kuyankhula kanthu kalikonse kabwino? Pakuti pakamwa pamayankhula zosefuka kuchokera mu mtima.
ای افعی‌زاده‌ها! شما که باطن‌تان اینقدر بد است، چگونه می‌توانید سخنان نیکو و درست بر زبان بیاورید؟ زیرا زبان از آنچه دل از آن پر است، سخن می‌گوید.
35 Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zomwe zili mumtima mwake ndipo munthu woyipa amatulutsanso zinthu zoyipa zomwe zili mwa iye.
شخص نیکو از خزانۀ دل نیکویش، چیزهای نیکو بیرون می‌آوَرَد، و انسان شریر از خزانۀ دل بدش، چیزهای شریرانه.
36 Ine ndikukuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro munthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mawu aliwonse wopanda pake amene anayankhula.
این را نیز به شما می‌گویم که انسان برای هر سخن پوچ که بر زبان می‌راند، باید در روز داوری به خدا حساب پس بدهد.
37 Pakuti ndi mawu anu mudzapezeka osalakwa ndiponso ndi mawu anu mudzapezeka olakwa.”
پس گفته‌هایتان یا شما را تبرئه خواهند کرد، یا محکوم.»
38 Pamenepo ena mwa Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anati kwa Iye, “Aphunzitsi, tikufuna tione chizindikiro chodabwitsa kuchokera kwa Inu.”
روزی برخی از علمای دین و عده‌ای از فریسی‌ها نزد عیسی آمدند و گفتند: «استاد، می‌خواهیم آیتی به ما نشان بدهی تا اقتدار خود را ثابت کنی.»
39 Iye anayankha kuti, “Mʼbado woyipa ndi wachigololo ufunsa za chizindikiro chodabwitsa! Koma ndi chimodzi chomwe sichidzapatsidwa kwa inu kupatula chizindikiro cha mneneri Yona.
اما عیسی پاسخ داد و فرمود: «نسل شریر و زناکار آیتی می‌طلب! اما تنها آیتی که به ایشان می‌دهم، آیت یونس نبی است.
40 Pakuti monga Yona anali mʼmimba mwa nsomba yayikulu masiku atatu, usana ndi usiku, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala masiku atatu, usana ndi usiku, mʼkati mwa nthaka.
زیرا همان‌طور که یونس سه روز و سه شب در شکم آن ماهی بزرگ ماند، پسر انسان نیز سه روز و سه شب در دل زمین خواهد ماند.
41 Anthu a ku Ninive adzayimirira pachiweruzo ndi mʼbado uwu ndi kuwutsutsa pakuti iwo analapa Yona atalalikira ndipo tsopano wamkulu kuposa Yona ali pano.
در روز داوری، مردم نینوا بر ضد این نسل به پا خاسته، آن را محکوم خواهند ساخت، زیرا ایشان با شنیدن موعظهٔ یونس توبه کردند. و اکنون کسی بزرگتر از یونس در اینجا هست، اما حاضر نیستید توبه کنید.
42 Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira pa tsiku lachiweruzo ndi mʼbado uwu ndipo idzawutsutsa pakuti inachokera kumathero a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni, ndipo pano pali woposa Solomoni.
در روز داوری، ملکهٔ سبا برخواهد خاست و مردم این دوره و زمانه را محکوم خواهد ساخت، زیرا او با زحمت فراوان، راهی دراز را پیمود تا بتواند سخنان حکیمانۀ سلیمان را بشنود. اما شخصی برتر از سلیمان در اینجاست، اما چه کم هستند کسانی که به او گوش می‌دهند.
43 “Pamene mzimu woyipa utuluka mwa munthu, umadutsa malo wopanda madzi kufunafuna malo opumulira ndipo suwapeza.
«وقتی یک روح پلید، کسی را ترک می‌کند، به صحراهای بی‌آب می‌رود تا جایی برای استراحت بیابد، اما نمی‌یابد.
44 Pamenepo umati, ‘Ndidzabwerera ku nyumba yanga komwe ndinatuluka.’ Pamene ufika, upeza mopanda kanthu, mosesedwa ndi mokonzedwa bwino.
پس می‌گوید:”به شخصی که از او درآمدم، باز می‌گردم.“پس باز می‌گردد و می‌بیند که خانۀ قبلی‌اش خالی، جاروشده و مرتب است.
45 Kenaka umapita kukatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa uwowo ndipo imapita ndi kukakhala mʼmenemo. Choncho khalidwe lotsiriza la munthu uyu limakhala loyipa kwambiri kuposa loyambalo. Umo ndi mmene zidzakhalire ndi mʼbado oyipawu.”
سپس هفت روح دیگر پیدا می‌کند که از خودش هم پلید‌تر هستند، و وارد آن شخص شده، در آنجا زندگی می‌کنند. به این ترتیب، وضع آن شخص بدتر از قبل می‌شود. تجربۀ این نسل شریر نیز چنین خواهد بود.»
46 Pamene Yesu anali kuyankhulabe ndi gulu la anthu, amayi ndi abale ake anayimirira kunja, akufuna kuyankhulana naye.
در همان حال که عیسی با جماعت سخن می‌گفت، مادر و برادرانش بیرون ایستاده بودند و می‌خواستند با او صحبت کنند.
47 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunjaku akufuna kuyankhulana nanu.”
پس شخصی به او گفت: «مادر و برادرانت بیرون ایستاده‌اند و می‌خواهند با تو صحبت کنند.»
48 Iye anayankha kuti, “Amayi anga ndani ndipo abale anga ndi ndani?”
عیسی در پاسخ فرمود: «مادر من کیست؟ برادرانم چه کسانی هستند؟»
49 Ndipo akuloza ophunzira ake, Iye anati, “Awa ndiwo amayi anga ndi abale anga.
سپس به شاگردانش اشاره کرد و گفت: «اینها هستند مادر و برادران من.
50 Pakuti aliyense amene achita chifuniro cha Atate anga akumwamba ndiye mʼbale wanga, mlongo wanga ndi amayi anga.”
هر که ارادۀ پدر آسمانی مرا به‌جا آوَرَد، او برادر و خواهر و مادر من است!»

< Mateyu 12 >