< Mateyu 1 >
1 Buku lofotokoza za mʼbado wa Yesu Khristu mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu:
O KE kuauhau na ka hanauna o Iesu Kristo, ka mamo a Davida, ka mamo a Aberahama.
2 Abrahamu anabereka Isake, Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka Yuda ndi abale ake.
Na Aberahama o Isaaka; na Isaaka o Iakoba; na Iakoba o Iuda a me kona poe hoahanau;
3 Yuda anabereka Perezi ndi Zara, amene amayi awo anali Tamara. Perezi anabereka Hezironi, Hezironi anabereka Aramu.
Na Iuda laua me Tamara o Paresa a me Zara; na Paresa o Hezerona; na Hezerona o Arama;
4 Aramu anabereka Aminadabu, Aminadabu anabereka Naasoni, Naasoni anabereka Salimoni.
Na Arama o Aminadaba; na Aminadaba o Naasona; na Naasona o Salemona;
5 Salimoni anabereka Bowazi amene amayi ake anali Rahabe, Bowazi anabereka Obedi amene amayi ake anali Rute, Obedi anabereka Yese.
Na Salemona laua me Rahaba o Boaza; na Boaza laua me Ruta o Obeda; na Obeda o Iese;
6 Yese anabereka Mfumu Davide. Ndipo Davide anabereka Solomoni, amene amayi ake anali mkazi wa Uriya.
Na Iese o Davida ke alii; na Davida na ke alii laua me ka wahine a Uria o Solomona;
7 Solomoni anabereka Rehabiamu, Rehabiamu anabereka Abiya, Abiya anabereka Asa,
Na Solomona o Rehoboama; na Rehoboama o Abia; na Abia o Asa;
8 Asa anabereka Yehosafati, Yehosafati anabereka Yoramu, Yoramu anabereka Uziya.
Na Asa o Iosapata; na Iosapata o Iorama; na Iorama o Ozia;
9 Uziya anabereka Yotamu, Yotamu anabereka Ahazi, Ahazi anabereka Hezekiya.
Na Ozia o Iotama, na Iotama o Ahaza; na Ahaza o Hezekia;
10 Hezekiya anabereka Manase, Manase anabereka Amoni, Amoni anabereka Yosiya.
Na Hezekia o Manase; na Manase o Amona; na Amona o Iosia;
11 Yosiya anali atabala Yekoniya ndi abale ake pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babuloni.
Na Iosia o Iekonia a me kona poe hoahanau, i ka manawa o ka lawe ana i Babulona:
12 Ali ku ukapolo ku Babuloni, Yekoniya anabereka Salatieli, Salatieli anabereka Zerubabeli.
A mahope mai o ka lawe ana i Babulona, na Iekonia o Saletiela; na Saletiela o Zerubabela;
13 Zerubabeli anabereka Abiudi, Abiudi anabereka Eliakimu, Eliakimu anabereka Azoro.
Na Zerubabela o Abiuda; na Abiuda o Eliakima; na Eliakima o Azora;
14 Azoro anabereka Zadoki, Zadoki anabereka Akimu, Akimu anabereka Eliudi.
Na Azora o Sadoka; na Sadoka o Akima; na Akima o Eliuda;
15 Eliudi anabereka Eliezara, Eliezara anabereka Matani, Matani anabereka Yakobo.
Na Eliuda o Eleazara; na Eleazara o Mahetana; na Mahetana o Iakoba;
16 Yakobo anabereka Yosefe, mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabereka Yesu wotchedwa Khristu.
Na Iakoba o Iosepa ke kane a Maria nana i hanau o Iesu, i kapaia o Kristo.
17 Kuyambira pa Abrahamu mpaka pa Davide, pali mibado khumi ndi inayi. Ndipo kuyambira pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babuloni, pali mibado khumi ndi inayi. Ndiponso kuyambira nthawi ya ukapolo ku Babuloni mpaka pamene Khristu anabadwa, palinso mibado khumi ndi inayi.
O na banauna a pau mai ia Aberahama mai a hiki ia Davida, he umi ia hanauna a me kumamaha; a mai ia Davida mai a hiki i ka lawe ana i Babulona, he umi ia hanauna a me kumamaha; a mai ka lawe ana aku i Babulona mai, a hiki ia Kristo he umi ia hanauna a me kumamaha.
18 Kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motere: Amayi ake, Mariya, anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanagone malo amodzi, anapezeka ali woyembekezera mwana mwa mphamvu ya Mzimu Woyera.
Penei hoi ka hanau ana o Iesu Kristo: I hoopalau e ia kona makuwahine o Maria na Iosepa, aole nae laua i pili, a ikea oia, ua hapai na ka Uhane Hemolele.
19 Popeza Yosefe mwamuna wake anali munthu wolungama, sanafune kumuchititsa manyazi pomuleka poyera. Choncho anaganiza zomuleka mosaonetsera.
Aka, he kanaka pono kana kane o Iosepa, aole ia i makemake e hoino ia ia ma ke akea; manao iho la ia e kipaku malu ia ia.
20 Koma akuganiza zimenezi, taonani, mngelo wa Ambuye anamuonekera mʼmaloto nati, “Yosefe mwana wa Davide, usaope kumutenga Mariya kukhala mkazi wako, chifukwa mwana akuyembekezerayo ndi wochokera kwa Mzimu Woyera.
A i kona noonoo ana ma ia mau mea, aia hoi, ikeia'ku ka anela a ka Haku e ia ma ka moe, i mai la, E Iosepa, e ka mamo a Davida, mai makau oe ke lawe ia Maria i wahine nau; no ka mea, ua hapai oia na ka Uhane Hemolele.
21 Ndipo adzabala mwana wamwamuna, udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku machimo awo.”
A e hanau mai oia i keikikane, a e kapa aku oe i kona inoa o IESU; no ka mea, e hoola ia i kona poe kanaka mai ko lakou hewa.
22 Zonsezi zinachitika kukwaniritsa zimene Ambuye ananena mwa mneneri kuti,
Ma ia mau mea i ko ai ka mea a ka Haku i olelo mai ai ma ke kaula, i ka i ana mai,
23 “Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”
Aia hoi, e hapai ana kekahi wahine puupaa, a e hanau mai ia i keikikane, a e kapaia kona inoa o Emanuela; o ke ano keia, o ke Akua me kakou.
24 Yosefe atadzuka, anachita zomwe mngelo wa Ambuye uja anamulamulira. Iye anamutenga Mariya kukhala mkazi wake.
A ala ae la o Iosepa mai ka hiamoe ana, hana aku la ia e like me ka ka anela a ka Haku i kauoha mai ai ia ia, a lawe mai la ia i kana wahine;
25 Koma sanagone malo amodzi mpaka mwanayo atabadwa ndipo anamutcha dzina lake Yesu.
Aole nae i moe aku ia ia, a hiki i ka wa i hanau ai oia i kana makahiapo kane, a kapa aku la ia i kona inoa o IESU.