< Marko 9 >
1 Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”
И глаголаше им: аминь глаголю вам, яко суть нецыи от зде стоящих, иже не имут вкусити смерти, дондеже видят Царствие Божие пришедшее в силе.
2 Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo.
И по шести днех поят Иисус Петра и Иакова и Иоанна, и возведе их на гору высоку особь едины: и преобразися пред ними.
3 Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi.
И ризы Его быша блещащяся, белы зело яко снег, яцехже не может белилник убелити на земли.
4 Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.
И явися им Илиа с Моисеем: и беста со Иисусом глаголюща.
5 Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
И отвещав Петр глагола Иисусови: Равви, добро есть нам зде быти: и сотворим кровы три, Тебе един, и Моисееви един, и Илии един.
6 (Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).
Не ведяше бо, что рещи: бяху бо пристрашни.
7 Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”
И бысть облак осеняя их: и прииде глас из облака, глаголя: Сей есть Сын Мой возлюбленный, Того послушайте.
8 Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.
И внезапу воззревше, ктому ни когоже видеша, токмо Иисуса единаго с собою.
9 Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa.
Сходящым же им с горы, запрети им, да ни комуже поведят, яже видеша, токмо егда Сын Человеческий из мертвых воскреснет.
10 Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”
И слово удержаша в себе, стязающеся, что есть, еже из мертвых воскреснути.
11 Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”
И вопрошаху Его глаголюще: како глаголют книжницы, яко Илии подобает приити прежде?
12 Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa?
Он же отвещав рече им: Илиа убо пришед прежде, устроит вся: и како есть писано о Сыне Человечестем, да много постраждет и уничижен будет:
13 Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”
но глаголю вам, яко и Илиа прииде, и сотвориша ему, елика хотеша, якоже есть писано о нем.
14 Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo.
И пришед ко учеником, виде народ мног о них и книжники стязающяся с ними.
15 Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.
И абие весь народ видев Его ужасеся, и пририщуще целоваху Его.
16 Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”
И вопроси книжники: что стязаетеся к себе?
17 Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula.
И отвещав един от народа рече: Учителю, приведох сына моего к Тебе, имуща духа нема:
18 Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”
и идеже колиждо имет его, разбивает его, и пены тещит, и скрежещет зубы своими, и оцепеневает: и рех учеником Твоим, да изженут его, и не возмогоша.
19 Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”
Он же отвещав ему глагола: о, роде неверен, доколе в вас буду? Доколе терплю вы? Приведите его ко Мне.
20 Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.
И приведоша его к Нему. И видев Его, абие дух стрясе его: и пад на земли, валяшеся, пены тещя.
21 Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?” Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono,
И вопроси отца его: колико лет есть, отнележе сие бысть ему? Он же рече: издетска:
22 wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”
и многажды во огнь вверже его и в воды, да погубит его: но аще что можеши, помози нам, милосердовав о нас.
23 Yesu anati, “‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”
Иисус же рече ему: еже аще что можеши веровати, вся возможна верующему.
24 Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”
И абие возопив отец отрочате, со слезами глаголаше: верую, Господи: помози моему неверию.
25 Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”
Видев же Иисус, яко срищется народ, запрети духу нечистому, глаголя ему: душе немый и глухий, Аз ти повелеваю: изыди из него и ктому не вниди в него.
26 Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.”
И возопив и много пружався, изыде: и бысть яко мертв, якоже мнозем глаголати, яко умре.
27 Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.
Иисус же емь его за руку, воздвиже его: и воста.
28 Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”
И вшедшу Ему в дом, ученицы Его вопрошаху Его единаго: яко мы не возмогохом изгнати его?
29 Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”
И рече им: сей род ничимже может изыти, токмо молитвою и постом.
30 Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali,
И оттуду изшедше, идяху сквозе Галилею: и не хотяше, да кто увесть.
31 chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.”
Учаше бо ученики Своя и глаголаше им, яко Сын Человеческий предан будет в руце человечесте, и убиют Его: и убиен быв, в третий день воскреснет.
32 Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.
Они же не разумеваху глаголгола и бояхуся Его вопросити.
33 Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?”
И прииде в Капернаум: и в дому быв, вопрошаше их: что на пути в себе помышлясте?
34 Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.
Они же молчаху: друг ко другу бо стязашася на пути, кто (есть) болий.
35 Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”
И сед пригласи обанадесяте и глагола им: аще кто хощет старей быти, да будет всех менший и всем слуга.
36 Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti,
И приимь отроча, постави е посреде их: и объемь е, рече им:
37 “Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”
иже аще едино таковых отрочат приимет во имя Мое, Мене приемлет: и иже Мене приемлет, не Мене приемлет, но Пославшаго Мя.
38 Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”
Отвеща Ему Иоанн, глаголя: Учителю, видехом некоего именем Твоим изгоняща бесы, иже не ходит по нас: и возбранихом ему, яко не последует нам.
39 Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine,
Иисус же рече: не браните ему: никтоже бо есть, иже сотворит силу о имени Моем, и возможет вскоре злословити Мя.
40 pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu.
Иже бо несть на вы, по вас есть.
41 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”
Иже бо аще напоит вы чашею воды во имя Мое, яко Христовы есте, аминь глаголю вам, не погубит мзды своея.
42 “Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake.
И иже аще соблазнит единаго от малых сих верующих в Мя, добрее есть ему паче, аще облежит камень жерновный о выи его, и ввержен будет в море.
43 Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna )
И аще соблажняет тя рука твоя, отсецы ю: добрее ти есть беднику в живот внити, неже обе руце имущу внити в геенну, во огнь неугасающий, (Geenna )
44 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
идеже червь их не умирает, и огнь не угасает.
45 Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna )
И аще нога твоя соблажняет тя, отсецы ю: добрее ти есть внити в живот хрому, неже две нозе имущу ввержену быти в геенну, во огнь неугасающий, (Geenna )
46 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
идеже червь их не умирает, и огнь не угасает.
47 Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna )
И аще око твое соблажняет тя, исткни е: добрее ти есть со единем оком внити в Царствие Божие, неже две оце имущу ввержену быти в геенну огненную, (Geenna )
48 kumene “‘mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima.’
идеже червь их не умирает, и огнь не угасает.
49 Aliyense adzayesedwa ndi moto.
Всяк бо огнем осолится, и всяка жертва солию осолится.
50 “Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”
Добро соль: аще же соль не слана будет, чим осолится? Имейте соль в себе, и мир имейте между собою.