< Marko 9 >

1 Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”
And He said unto them, Verily I tell you, that there are some of those who stand here, that shall not taste of death, till they have seen the kingdom of God come with power.
2 Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo.
And after six days Jesus taketh with Him Peter, and James, and John, and bringeth them up by themselves to a high mountain apart; and was transfigured before them:
3 Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi.
and his raiment shone, being exceeding white as snow, so as no fuller on earth can whiten.
4 Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.
And there appeared unto them Elias with Moses, and they were talking with Jesus.
5 Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
Then said Peter to Jesus, Master, it is good for us to be here: let us make three tabernacles; one for Thee, and one for Moses, and one for Elias:
6 (Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).
for he knew not what to say, for they were sore afraid.
7 Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”
And there was a cloud overshadowing them, and a voice came out of the cloud, saying, This is my beloved Son, hear ye Him.
8 Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.
And immediately looking round about, they saw no more of any one, but Jesus alone with them.
9 Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa.
And as they came down from the mountain, He charged them to tell no one what they had seen, till after the Son of man were risen from the dead.
10 Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”
And they laid hold on that expression, querying among themselves, what means the rising from the dead?
11 Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”
Then they asked Him, saying, Why do the scribes say, that Elias must come first?
12 Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa?
And He answered and told them, Elias doth indeed come first, and settle all things: He told them likewise how it is written of the Son of man, that he must suffer many things and be used contemptuously.
13 Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”
But I tell you, that Elias is come, and they have done to him whatever they would, as it is written of him.
14 Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo.
And when He came to the other disciples, He saw a great multitude about them, and the scribes disputing with them.
15 Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.
And immediately all the people, when they saw Him, were astonished; and running to Him, saluted Him.
16 Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”
And he asked the scribes, What are ye disputing about?
17 Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula.
And one of the multitude answered, and said, Master I have brought unto thee my son, who is possessed by a dumb spirit:
18 Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”
and wherever it seizeth him, it convulseth him; and he fometh, and gnasheth his teeth, and thus he pineth away: and I desired thy disciples to cast him out, and they could not.
19 Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”
And He answered and said, O unbelieving generation, how long shall I be with you? how long shall I bear with you? bring him to me.
20 Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.
And they brought him to Him: and as soon as he saw Him, immediately the spirit threw him into convulsions: and he fell upon the ground, and rolled about foming.
21 Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?” Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono,
And He asked his father, How long is it since this befel him? And he said, From a child.
22 wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”
And it has often thrown him both into the fire and into the waters to destroy him. But if thou canst do any thing, have compassion on us and help us.
23 Yesu anati, “‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”
And Jesus said unto him, If thou canst believe, all things are possible to him that believeth.
24 Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”
And the father of the child immediately cried out and said with tears, Lord, I believe, help thou my unbelief.
25 Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”
when Jesus saw the people flock together, He rebuked the impure spirit, and said to him, Thou dumb and deaf spirit, I command thee, Come out of him, and enter no more into him.
26 Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.”
And when he had rored and vehemently convulsed him, he came out of him: and the child was as one dead, so that many said, that he was dead.
27 Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.
But Jesus took him by the hand and lifted him up, and he arose.
28 Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”
And when He was come into the house, his disciples asked Him in private, Why could not we cast him out?
29 Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”
And He said unto them, This kind cannot be cast out, but by prayer and fasting.
30 Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali,
And they departed from thence and passed through Galilee, and He was not willing that any should know it;
31 chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.”
for He was instructing his disciples, and told them, the Son of man is going to be delivered into the hands of men, and they will put Him to death; and on the third day, after his being put to death, He will rise again.
32 Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.
But they knew not his meaning, and were afraid to ask Him.
33 Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?”
And he came to Capernaum; and when He was in the house, He asked them, What were ye disputing about among yourselves by the way?
34 Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.
But they held their peace; for they had been disputing with each other by the way who should be the greatest.
35 Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”
So He sat down and called the twelve, and saith unto them, If any one would be first, let him be last of all, and servant of all.
36 Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti,
And He took a child and set him in the midst of them, and taking him in his arms He said unto them,
37 “Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”
Whoever shall receive one of these little children in my name, receiveth me; and whosoever receiveth me, receiveth not me only, but Him that sent me.
38 Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”
But John answered Him and said, Master, we saw one casting out demons in thy name, who doth not follow us; and we forbade him, because he followeth not us.
39 Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine,
But Jesus said, Forbid him not: for there is no one, that worketh a miracle in my name, and can presently speak evil of me:
40 pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu.
for he that is not against us, is for us.
41 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”
For whosoever shall give you but a cup of water to drink, for my sake; because ye are Christ's, I assure you, he shall not lose his reward.
42 “Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake.
And whosoever shall cause one of these little ones, that believe in me, to offend, it were better for him, if a milstone were laid upon his neck, and he were cast into the sea.
43 Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna g1067)
And if thy hand cause thee to offend, cut it off: it is better for thee to enter into life maimed, than having two hands, to go into hell, into the fire that will never be extinguished; (Geenna g1067)
44 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
where their worm dieth not, and the fire is not quenched.
45 Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna g1067)
And if thy foot cause thee to offend, cut it off: it is better for thee to enter into life lame, than having two feet to be cast into hell, into the inextinguishable fire; (Geenna g1067)
46 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
where their worm dieth not, and the fire is not quenched.
47 Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna g1067)
And if thine eye cause thee to offend, cast it out: it is better for thee to enter into the kingdom of God with one eye, than having two eyes to be cast into hell-fire; (Geenna g1067)
48 kumene “‘mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima.’
where their worm dieth not, and the fire is not quenched.
49 Aliyense adzayesedwa ndi moto.
For every one shall be as it were salted by fire, and every sacrifice shall be seasoned as with salt.
50 “Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”
Salt is useful, but if the salt become insipid, wherewith will ye season it? Have salt therefore in yourselves, and as a proof of it be at peace one with another.

< Marko 9 >