< Marko 9 >
1 Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”
He went on to say, "In solemn truth I tell you that some of those who are standing here will certainly not taste death till they have seen the Kingdom of God already come in power."
2 Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo.
Six days later, Jesus took with Him Peter, James, and John, and brought them alone, apart from the rest, up a high mountain; and in their presence His appearance underwent a change.
3 Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi.
His garments also became dazzling with brilliant whiteness--such whiteness as no bleaching on earth could give.
4 Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.
Moreover there appeared to them Elijah accompanied by Moses; and the two were conversing with Jesus,
5 Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
when Peter said to Jesus, "Rabbi, we are thankful to you that we are here. Let us put up three tents--one for you, one for Moses, and one for Elijah."
6 (Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).
For he knew not what to say: they were filled with such awe.
7 Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”
Then there came a cloud spreading over them, and a voice issued from the cloud, "This is my Son, dearly loved: listen to Him."
8 Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.
Instantly they looked round, and now they could no longer see any one, but themselves and Jesus.
9 Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa.
As they were coming down from the mountain, He very strictly forbad them to tell any one what they had seen "until after the Son of Man has risen from among the dead."
10 Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”
So they kept the matter to themselves, although frequently asking one another what was meant by the rising from the dead.
11 Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”
They also asked Him, "How is it that the Scribes say that Elijah must first come?"
12 Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa?
"Elijah," He replied, "does indeed come first and reforms everything; but how is it that it is written of the Son of Man that He will endure much suffering and be held in contempt?
13 Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”
Yet I tell you that not only has Elijah come, but they have also done to him whatever they chose, as the Scriptures say about him."
14 Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo.
As they came to rejoin the disciples, they saw an immense crowd surrounding them and a party of Scribes disputing with them.
15 Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.
Immediately the whole multitude on beholding Him were astonished and awe-struck, and yet they ran forward and greeted Him.
16 Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”
"What is the subject you are discussing?" He asked them.
17 Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula.
"Rabbi," answered one of the crowd, "I have brought you my son. He has a dumb spirit in him;
18 Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”
and wherever it comes upon him, it dashes him to the ground, and he foams at the mouth and grinds his teeth, and he is pining away. I begged your disciples to expel it, but they had not the power."
19 Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”
"O unbelieving generation!" replied Jesus; "how long must I be with you? how long must I have patience with you? Bring the boy to me."
20 Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.
So they brought him to Jesus. And the spirit, when he saw Jesus, immediately threw the youth into convulsions, so that he fell on the ground and rolled about, foaming at the mouth.
21 Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?” Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono,
Then Jesus asked the father, "How long has he been like this?" "From early childhood," he said;
22 wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”
"and often it has thrown him into the fire or into pools of water to destroy him. But, if you possibly can, have pity on us and help us."
23 Yesu anati, “‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”
"'If I possibly can!'" replied Jesus; "why, everything is possible to him who believes."
24 Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”
Immediately the father cried out, "I do believe: strengthen my weak faith."
25 Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”
Then Jesus, seeing that an increasing crowd was running towards Him, rebuked the foul spirit, and said to it, "Dumb and deaf spirit, I command you, come out of him and never enter into him again."
26 Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.”
So with a loud cry he threw the boy into fit after fit, and came out. The boy looked as if he were dead, so that most of them said he was dead;
27 Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.
but Jesus took his hand and raised him up, and he stood on his feet.
28 Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”
After the return of Jesus to the house His disciples asked Him privately, "How is it that we could not expel the spirit?"
29 Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”
"An evil spirit of this kind," He answered, "can only be driven out by prayer."
30 Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali,
Departing thence they passed through Galilee, and He was unwilling that any one should know it;
31 chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.”
for He was teaching His disciples, and telling them, "The Son of Man is to be betrayed into the hands of men, and they will put Him to death; and after being put to death, in three days He will rise to life again."
32 Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.
They, however, did not understand what He meant, and were afraid to question Him.
33 Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?”
So they came to Capernaum; and when in the house He asked them, "What were you arguing about on the way?"
34 Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.
But they remained silent; for on the way they had debated with one another who was the chief of them.
35 Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”
Then sitting down He called the Twelve, and said to them, "If any one wishes to be first, he must be last of all and servant of all."
36 Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti,
And taking a young child He made him stand in their midst, then threw His arms round him and said,
37 “Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”
"Whoever for my sake receives one such young child as this, receives me; and whoever receives me, receives not so much me as Him who sent me."
38 Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”
"Rabbi," said John to Him, "we saw a man making use of your name to expel demons, and we tried to hinder him, on the ground that he did not follow us."
39 Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine,
"You should not have tried to hinder him," replied Jesus, "for there is no one who will use my name to perform a miracle and be able the next minute to speak evil of me.
40 pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu.
He who is not against us is for us;
41 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”
and whoever gives you a cup of water to drink because you belong to Christ, I solemnly tell you that he will certainly not lose his reward.
42 “Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake.
"And whoever shall occasion the fall of one of these little ones who believe, he would be better off if, with a millstone round his neck, he were lying at the bottom of the sea.
43 Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna )
If your hand should cause you to sin, cut it off: it would be better for you to enter into Life maimed, than remain in possession of both your hands and go away into Gehenna, into the fire which cannot be put out. (Geenna )
44 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
45 Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna )
Or if your foot should cause you to sin, cut it off: it would be better for you to enter into Life crippled, than remain in possession of both your feet and be thrown into Gehenna. (Geenna )
46 (Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
47 Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna )
Or if your eye should cause you to sin, tear it out. It would be better for you to enter into the Kingdom of God half-blind than remain in possession of two eyes and be thrown into Gehenna, (Geenna )
48 kumene “‘mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima.’
where their worm does not die and the fire does not go out.
49 Aliyense adzayesedwa ndi moto.
Every one, however, will be salted with fire.
50 “Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”
Salt is a good thing, but if the salt should become tasteless, what will you use to give it saltness? Have salt within you and live at peace with one another."