< Marko 8 >

1 Mʼmasiku amenewo gulu lina lalikulu la anthu linasonkhana. Popeza iwo analibe chakudya, Yesu anayitana ophunzira ake nati kwa iwo,
Тими днями, коли було зно́ву багато наро́ду, а їсти не мали чого́, покликав Він у́чнів Своїх та й промовив до них:
2 “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala ali ndi Ine masiku atatuwa ndipo alibe chakudya.
„Жаль мені тих людей, що вже три дні зо Мною знахо́дяться, та їсти не мають чого́.
3 Ngati nditawawuza kuti apite kwawo ali ndi njala, iwo adzakomoka mʼnjira chifukwa ena a iwo achokera kutali.”
А коли відпущу́ їх голодних до їхніх домівок, то осла́бнуть у дорозі, бо деякі з них поприхо́дили зда́лека“.
4 Ophunzira ake anayankha nati, “Kodi ndi kuti kuthengo kuno kumene munthu angapeze buledi okwanira kuwadyetsa?”
І відказали Йому Його у́чні: „Звідки зможе хто нагодувати їх хлібом отут у пустині?
5 Yesu anafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
А Він їх запитав: „Скільки маєте хліба?“Вони ж повідо́мили: „Се́меро“.
6 Iye anawuza gulu la anthu kuti likhale pansi. Atatenga malofu a buledi asanu ndi awiri, anayamika, nawanyema ndipo anapatsa ophunzira ake kuti agawire anthu, ndipo iwo anatero.
Тоді Він народу звелів на землі посідати. І, взявши се́меро хліба, віддавши подяку, Він поламав і дав учням Своїм, щоб роздати. А вони роздавали наро́дові,
7 Analinso ndi tinsomba tochepa; Iye anayamikanso chifukwa cha nsombazo. Ndipo anawuza ophunzira kuti awagawire.
І мали вони трохи ри́бок; і Він їх поблагословив, і роздати звелів також їх.
8 Anthu anadya ndipo anakhuta. Atamaliza, ophunzira anatola buledi ndi nsomba zotsalira ndi kudzaza madengu asanu ndi awiri.
І всі їли й наїлися, а з позосталих кусків сім коші́в назбирали.
9 Panali amuna pafupifupi 4,000. Ndipo atawawuza kuti apite kwawo,
А їдців було тисяч з чотири!
10 analowa mʼbwato pamodzi ndi ophunzira ake napita ku dera la Dalamanuta.
І всів Він негайно до чо́вна з Своїми у́чнями, та й прибув до землі далману́тської.
11 Afarisi anabwera nayamba kumufunsa Yesu. Pomuyesa Iye, anamufunsa za chizindikiro chochokera kumwamba.
І вийшли фарисеї, і почали́ сперечатися з Ним, і, Його випробо́вуючи, хотіли від Нього озна́ки із неба.
12 Ndipo anatsitsa moyo nati, “Nʼchifukwa chiyani mʼbado uno ukufuna chizindikiro chodabwitsa? Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe chizindikiro chidzapatsidwa kwa iwo.”
А Він тяжко зідхнув у Своїм дусі й промовив: „Якої ознаки цей рід вимагає? Поправді кажу́ вам, що родові цьому ознака не буде дана!“
13 Ndipo anawasiya, nalowanso mʼbwato ndi kuwolokera tsidya lina.
І покинув Він їх, усів знову до чо́вна, і на то́й бік відбу́в.
14 Ophunzira anayiwala kutenga buledi, kupatula buledi mmodzi yekha amene anali naye mʼbwato.
І забули вони взяти хліба, і крім одно́го буханця́, у чо́вні не мали з собою нічого.
15 Yesu anawachenjeza kuti, “Samalani ndipo onetsetsani yisiti wa Afarisi ndi wa Herode.”
А Він їм наказував та говорив: „Стережіться уважливо фарисейської розчи́ни й розчини Іродової!“
16 Iwo anakambirana wina ndi mnzake ndipo anati, “Ndi chifukwa choti tilibe buledi.”
Вони ж міркували й казали один до одного, що хліба не мають вони.
17 Yesu atadziwa zokambirana zawo anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe buledi? Kodi inu simukuonabe kapena kuzindikira? Kodi mitima yanu ndi yowumitsidwa?
А Ісус, знавши те, промовляє до них: „Чого́ ви міркуєте, що хліба не маєте? Чи ви ще не знаєте й не розумієте? Чи ще маєте серце своє затверді́лим?
18 Kodi muli ndi maso ndipo simukuona, ndi makutu ndipo mukulephera kumva? Kodi simukukumbukira?
„Мавши очі — не бачите, і мавши ву́ха — не чуєте?“І не пам'ятаєте,
19 Pamene ndinagawa malofu asanu a buledi kwa anthu 5,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Khumi ndi awiri.”
коли п'ять хлібів Я ламав на п'ять тисяч, — скільки повних коші́в із кусків ви зібрали?“Вони кажуть до Нього: „Дванадцять“.
20 “Ndipo pamene ndinagawa malofu asanu ndi awiri a buledi, kwa anthu 4,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
„А як сім на чотири тисячі, — скільки кошиків повних з кусків ви зібрали?“І відказують: „Сім“.
21 Iye anawafunsa kuti, “Kodi simumvetsetsabe?”
І сказав Він до них: „Ви ще не розумієте?“
22 Iwo anafika ku Betisaida, ndipo anthu ena anabweretsa munthu wosaona ndipo anamupempha Yesu kuti amukhudze.
І приходять вони в Віфсаї́ду. І приводять до Нього сліпого, і благають Його, щоб доторкну́вся до нього.
23 Iye anagwira dzanja la munthu wosaonayo napita naye kunja kwa mudzi. Atalavulira mʼmaso a munthuyo ndi kumusanjika manja, Yesu anafunsa kuti, “Kodi ukuona kalikonse?”
І взяв Він сліпого за руку, та й вивів його за село. І посли́нивши очі йому, поклав руки на нього, і питався його, чи що бачить.
24 Iye anakweza maso nati, “Ndikuona anthu; akuoneka ngati mitengo imene ikuyendayenda.”
І, зиркнувши, сказав той: „Я бачу людей, які ходять, немов би дере́ва“.
25 Kenakanso Yesu anayika manja ake mʼmaso a munthuyo. Ndipo maso ake anatsekuka, naonanso, ndipo anaona zonse bwinobwino.
Потім знов Він поклав Свої руки на очі йому, — і прозрі́в той, і одужав, і вира́зно став бачити все!
26 Yesu anamuwuza kuti apite kwawo nati, “Usapite mʼmudzimo.”
І послав Він додому його й наказав: „До села й не заходь, і ніко́му в селі не розповіда́й!“
27 Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
Потому пішов Ісус й у́чні Його до сіл Кесарі́ї Пилипової, а в дорозі питав Своїх у́чнів, говорячи їм: „За кого Мене люди вважають?“
28 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati ndinu mmodzi wa aneneri.”
Вони ж відповіли́ Йому, кажучи: „За Івана Христителя, другі — за Іллю́, а інші — за одно́го з пророків“.
29 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu, mumati ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu.”
І Він запитав їх: „А ви за кого Мене маєте?“Петро Йому в відповідь каже: „Ти — Христос!“
30 Yesu anawachenjeza kuti asawuze wina aliyense za Iye.
І Він заборонив їм, щоб ніко́му про Нього вони не казали!
31 Iye anayamba kuwaphunzitsa kuti, “Mwana wa Munthu ayenera kumva zowawa zambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe, ndi aphunzitsi a malamulo, ndi kuti ayenera kuphedwa ndipo patatha masiku atatu adzaukanso.”
І почав їх навчати, що Синові Лю́дському треба багато страждати, і Його відцураються старші, і первосвященики, і книжники, і Він буде вбитий, — але третього дня Він воскресне.
32 Izi anaziyankhula momveka bwino, ndipo Petro anamutengera pambali ndipo anayamba kumudzudzula.
І те слово казав Він відкрито. А Петро узяв на́бік Його, і Йому́ став перечити.
33 Koma Yesu atatembenuka ndi kuyangʼana ophunzira ake, anamudzudzula Petro nati, “Choka pamaso panga Satana! Suganizira zinthu za Mulungu koma za anthu.”
А Він обернувся й поглянув на у́чнів Своїх, та й Петру докори́в і сказав: „Відступись, сатано, від Мене, бо ду́маєш ти не про Боже, а про лю́дське!“
34 Kenaka anayitana gulu la anthu pamodzi ndi ophunzira ake nati: “Ngati wina aliyense afuna kunditsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake ndi kunditsata.
І Він покликав народ із Своїми у́чнями, та й промовив до них: „Коли хоче хто йти вслід за Мною, хай зречеться самого себе, і хай ві́зьме свого хреста та й за Мною йде!
35 Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine ndi cha Uthenga Wabwino, adzawupulumutsa.
Бо хто хоче душу свою́ зберегти, той погубить її, а хто згубить душу свою ради Мене та Єва́нгелії, той її збереже.
36 Kodi munthu adzapindulanji akalandira dziko lonse lapansi, koma ndi kutaya moyo wake?
Яка ж ко́ристь люди́ні, що здобу́де ввесь світ, але душу свою занапа́стить?
37 Kapena nʼchiyani chomwe munthu angapereke chosinthana ndi moyo wake?
Або що́ назамі́н дасть люди́на за душу свою?
38 Ngati wina achita manyazi chifukwa cha Ine ndi mawu anga mu mʼbado uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wa Atate ake pamodzi ndi angelo oyera.”
Бо хто буде Мене та Моєї науки соро́митися в роді цім перелю́бнім та грішнім, того посоро́миться також Син Лю́дський, як при́йде у славі Свого Отця з ангола́ми святими“.

< Marko 8 >