< Marko 8 >
1 Mʼmasiku amenewo gulu lina lalikulu la anthu linasonkhana. Popeza iwo analibe chakudya, Yesu anayitana ophunzira ake nati kwa iwo,
Тими днями, як було пребагато народу й не мали що їсти, покликавши Ісус учеників своїх, рече їм:
2 “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala ali ndi Ine masiku atatuwa ndipo alibe chakudya.
Жаль мені народу, що вже три днї пробувають зо мною, і не мають що їсти;
3 Ngati nditawawuza kuti apite kwawo ali ndi njala, iwo adzakomoka mʼnjira chifukwa ena a iwo achokera kutali.”
А коли відпущу їх голодних до домівок їх, помлїють в дорозі; деякі бо з них здалека поприходили.
4 Ophunzira ake anayankha nati, “Kodi ndi kuti kuthengo kuno kumene munthu angapeze buledi okwanira kuwadyetsa?”
І відказали Йому ученики Його: Звідкіля ж сих зможе хто тут нагодувати хлібом у пустині?
5 Yesu anafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
І питав їх: Скільки маєте хлібів? Вони ж кажуть: Сїм.
6 Iye anawuza gulu la anthu kuti likhale pansi. Atatenga malofu a buledi asanu ndi awiri, anayamika, nawanyema ndipo anapatsa ophunzira ake kuti agawire anthu, ndipo iwo anatero.
І звелів Він народові сїдати на землі; і взявши сім хлїбів, оддавши хвалу, ламав і давав ученикам своїм, щоб клали перед ними; і клади перед народом.
7 Analinso ndi tinsomba tochepa; Iye anayamikanso chifukwa cha nsombazo. Ndipo anawuza ophunzira kuti awagawire.
І мали рибок кілька; й поблагословивши, казав покласти й те.
8 Anthu anadya ndipo anakhuta. Atamaliza, ophunzira anatola buledi ndi nsomba zotsalira ndi kudzaza madengu asanu ndi awiri.
Їли ж і наситились, і назбирали останків ламаного сім кошів.
9 Panali amuna pafupifupi 4,000. Ndipo atawawuza kuti apite kwawo,
Було ж тих, що їли, з чотири тисячі; і відпустив їх.
10 analowa mʼbwato pamodzi ndi ophunzira ake napita ku dera la Dalamanuta.
І, зараз увійшовши в човен з учениками своїми, прибув у сторони Далманутанські.
11 Afarisi anabwera nayamba kumufunsa Yesu. Pomuyesa Iye, anamufunsa za chizindikiro chochokera kumwamba.
І вийшли Фарисеї, та й почали перепитуватись із Ним, допевняючись у Него ознаки з неба, спокушуючи Його.
12 Ndipo anatsitsa moyo nati, “Nʼchifukwa chiyani mʼbado uno ukufuna chizindikiro chodabwitsa? Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe chizindikiro chidzapatsidwa kwa iwo.”
І зітхнувша Він духом своїм, рече: Чого кодло се ознаки шукає? Істино глаголю вам: Не дасть ся кодлу сьому ознака.
13 Ndipo anawasiya, nalowanso mʼbwato ndi kuwolokera tsidya lina.
І, оставивши їх, увійшов знов у човен, і поплив на той бік.
14 Ophunzira anayiwala kutenga buledi, kupatula buledi mmodzi yekha amene anali naye mʼbwato.
І забули взяти хлїба, й опріч одного хлїба не мали з собою в човнї.
15 Yesu anawachenjeza kuti, “Samalani ndipo onetsetsani yisiti wa Afarisi ndi wa Herode.”
І наказував їм, глаголючи: Гледїть, остерегайтесь квасу Фарисейського й квасу Іродового.
16 Iwo anakambirana wina ndi mnzake ndipo anati, “Ndi chifukwa choti tilibe buledi.”
І міркували вони між собою, кажучи: Се, що хлїба не маємо.
17 Yesu atadziwa zokambirana zawo anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe buledi? Kodi inu simukuonabe kapena kuzindikira? Kodi mitima yanu ndi yowumitsidwa?
І зрозумівши Ісус, рече їм: Чого міркуєте, що хлїба не маєте? Невже ж ви ще не постерегаєте й не розумієте? Чи ще затверділе маєте серце ваше?
18 Kodi muli ndi maso ndipo simukuona, ndi makutu ndipo mukulephera kumva? Kodi simukukumbukira?
Очі мавши, не бачите? й, уші мавши, не чуєте, й вже не памятаєте?
19 Pamene ndinagawa malofu asanu a buledi kwa anthu 5,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Khumi ndi awiri.”
Як пять хлїбів ламав я на пять тисяч, скільки кошиків повних ламаного назбирали ви? Кажуть Йому: Дванайцять.
20 “Ndipo pamene ndinagawa malofu asanu ndi awiri a buledi, kwa anthu 4,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
Як же сїм на чотирі тисячі, скільки кошів повних ламаного назбирали ви? Вони кажуть: Сїм.
21 Iye anawafunsa kuti, “Kodi simumvetsetsabe?”
І рече їм: Як же ви не розумієте?
22 Iwo anafika ku Betisaida, ndipo anthu ena anabweretsa munthu wosaona ndipo anamupempha Yesu kuti amukhudze.
І приходить у Витсаїду; й приводять Йому слїпого, й просять Його, щоб до него приторкнув ся.
23 Iye anagwira dzanja la munthu wosaonayo napita naye kunja kwa mudzi. Atalavulira mʼmaso a munthuyo ndi kumusanjika manja, Yesu anafunsa kuti, “Kodi ukuona kalikonse?”
І взявши за руку слїпого, вивів його осторонь села; й, плюнувши на очі його, положив руки на него, й спитав його, чи що бачить.
24 Iye anakweza maso nati, “Ndikuona anthu; akuoneka ngati mitengo imene ikuyendayenda.”
І, позирнувши вгору, каже: Бачу людей, що мов дерева ходять.
25 Kenakanso Yesu anayika manja ake mʼmaso a munthuyo. Ndipo maso ake anatsekuka, naonanso, ndipo anaona zonse bwinobwino.
Опісля знов положив руки на очі його, й заставив його позирнути вгору; і сцїлив ся він, і бачив ясно все.
26 Yesu anamuwuza kuti apite kwawo nati, “Usapite mʼmudzimo.”
І відослав його до домівки його, глаголючи: Анї в село не входь, анї розказуй нікому в селї.
27 Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
І вийшов Ісус і ученики Його у села Кесариї Филипової, і дорогою питав учеників своїх, глаголючи їм: Хто я, - кажуть люде?
28 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati ndinu mmodzi wa aneneri.”
Вони ж одказали: Йоан Хреститель; а инші: Ілия; инші ж: Один з пророків.
29 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu, mumati ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu.”
А він рече їм: Ви ж, хто скажете? Озвав ся ж Петр і каже Йому: Ти єси Христос.
30 Yesu anawachenjeza kuti asawuze wina aliyense za Iye.
І наказав їм, щоб нікому не казали про Него.
31 Iye anayamba kuwaphunzitsa kuti, “Mwana wa Munthu ayenera kumva zowawa zambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe, ndi aphunzitsi a malamulo, ndi kuti ayenera kuphedwa ndipo patatha masiku atatu adzaukanso.”
І почав навчати їх, що мусить Син чоловічий багато терпіти, й відцурають ся Його старші, та архиєреї, та письменники, і вбють, і в третій день воскресне Він.
32 Izi anaziyankhula momveka bwino, ndipo Petro anamutengera pambali ndipo anayamba kumudzudzula.
І явно слово гляголав. І взявши Його Петр, почав докоряти Йому.
33 Koma Yesu atatembenuka ndi kuyangʼana ophunzira ake, anamudzudzula Petro nati, “Choka pamaso panga Satana! Suganizira zinthu za Mulungu koma za anthu.”
Він же, обернувшись і поглянувши на учеників своїх, докорив Петру, глаголючи: Іди геть, сатано: бо мислиш не про Боже, а про чоловіче.
34 Kenaka anayitana gulu la anthu pamodzi ndi ophunzira ake nati: “Ngati wina aliyense afuna kunditsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake ndi kunditsata.
І, прикликавши народ укупі з учениками своїми, рече їм: Хто хоче йти за мною, нехай одречеть ся себе, й візьме хрест свій, та й іде слідом за мною.
35 Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine ndi cha Uthenga Wabwino, adzawupulumutsa.
Хто бо хоче душу свою спасти, погубить її; хто ж погубить душу свою задля мене та євангелиї, той спасе її.
36 Kodi munthu adzapindulanji akalandira dziko lonse lapansi, koma ndi kutaya moyo wake?
Що бо за користь чоловікові, коли здобуде сьвіт увесь, а занапастить душу свою?
37 Kapena nʼchiyani chomwe munthu angapereke chosinthana ndi moyo wake?
Або що дасть чоловік у замін душі своєї?
38 Ngati wina achita manyazi chifukwa cha Ine ndi mawu anga mu mʼbado uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wa Atate ake pamodzi ndi angelo oyera.”
Хто бо соромити меть ся мене й моїх словес між кодлом сим перелюбним і грішним, і Син чоловічий соромити меть ся його, як прийде в славі Отця свого з ангелами сьвятими.