< Marko 8 >
1 Mʼmasiku amenewo gulu lina lalikulu la anthu linasonkhana. Popeza iwo analibe chakudya, Yesu anayitana ophunzira ake nati kwa iwo,
In those days, there being again a very great multitude, and they having nothing to eat, Jesus called his disciples to Him,
2 “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala ali ndi Ine masiku atatuwa ndipo alibe chakudya.
and saith unto them, I have compassion on the multitude, for they have now been with me three days, and have nothing to eat:
3 Ngati nditawawuza kuti apite kwawo ali ndi njala, iwo adzakomoka mʼnjira chifukwa ena a iwo achokera kutali.”
and if I send them away fasting to their own home, they will faint by the way; for some of them are come from far.
4 Ophunzira ake anayankha nati, “Kodi ndi kuti kuthengo kuno kumene munthu angapeze buledi okwanira kuwadyetsa?”
And his disciples answered Him, From whence can one satisfy these people with bread here in a desert?
5 Yesu anafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
And He asked them, How many loaves have ye? and they said, Seven.
6 Iye anawuza gulu la anthu kuti likhale pansi. Atatenga malofu a buledi asanu ndi awiri, anayamika, nawanyema ndipo anapatsa ophunzira ake kuti agawire anthu, ndipo iwo anatero.
And He ordered the people to sit down upon the ground: and taking the seven loaves, He gave thanks and brake them, and gave to his disciples to set before them; and they did set them before the multitude.
7 Analinso ndi tinsomba tochepa; Iye anayamikanso chifukwa cha nsombazo. Ndipo anawuza ophunzira kuti awagawire.
And they had a few small fishes: and He blessed them, and bid them set them also before the people.
8 Anthu anadya ndipo anakhuta. Atamaliza, ophunzira anatola buledi ndi nsomba zotsalira ndi kudzaza madengu asanu ndi awiri.
And they did eat and were satisfied: and they took up what were left, to wit of fragments seven baskets:
9 Panali amuna pafupifupi 4,000. Ndipo atawawuza kuti apite kwawo,
and they that had eaten were about four thousand. And then He dismissed them.
10 analowa mʼbwato pamodzi ndi ophunzira ake napita ku dera la Dalamanuta.
And going directly on board a ship with his disciples, He came into the parts of Dalmanutha:
11 Afarisi anabwera nayamba kumufunsa Yesu. Pomuyesa Iye, anamufunsa za chizindikiro chochokera kumwamba.
and the pharirisees came forth, and began to dispute with Him, desiring of Him a sign from heaven, tempting Him.
12 Ndipo anatsitsa moyo nati, “Nʼchifukwa chiyani mʼbado uno ukufuna chizindikiro chodabwitsa? Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe chizindikiro chidzapatsidwa kwa iwo.”
And He sighing deeply in his spirit, saith, Why doth this generation require a sign? Verily I tell you, There shall no sign be given to this generation.
13 Ndipo anawasiya, nalowanso mʼbwato ndi kuwolokera tsidya lina.
So He left them, and went on board the ship again, and departed to the other side.
14 Ophunzira anayiwala kutenga buledi, kupatula buledi mmodzi yekha amene anali naye mʼbwato.
And his disciples had forgot to take bread, neither had they any more than one loaf with them in the ship.
15 Yesu anawachenjeza kuti, “Samalani ndipo onetsetsani yisiti wa Afarisi ndi wa Herode.”
And therefore as He was giving them a charge, saying, Take heed, beware of the leaven of the pharisees, and of the leaven of Herod,
16 Iwo anakambirana wina ndi mnzake ndipo anati, “Ndi chifukwa choti tilibe buledi.”
they argued one with another, saying, It is because we have no bread.
17 Yesu atadziwa zokambirana zawo anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe buledi? Kodi inu simukuonabe kapena kuzindikira? Kodi mitima yanu ndi yowumitsidwa?
And Jesus knowing it saith unto them, What are ye reasoning about? because ye have no bread? Do ye not yet discern nor understand? have ye your heart still hardened?
18 Kodi muli ndi maso ndipo simukuona, ndi makutu ndipo mukulephera kumva? Kodi simukukumbukira?
Have ye eyes, and do not see? and having ears, hear ye not? and do ye not remember?
19 Pamene ndinagawa malofu asanu a buledi kwa anthu 5,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Khumi ndi awiri.”
When I brake the five loaves among five thousand, how many baskets full of fragments did ye take up? They answer, Twelve.
20 “Ndipo pamene ndinagawa malofu asanu ndi awiri a buledi, kwa anthu 4,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
And when I divided the seven among four thousand, how many baskets full of fragments took ye up? and they said, Seven.
21 Iye anawafunsa kuti, “Kodi simumvetsetsabe?”
And He said unto them, How is it then that ye do not understand?
22 Iwo anafika ku Betisaida, ndipo anthu ena anabweretsa munthu wosaona ndipo anamupempha Yesu kuti amukhudze.
Then He cometh to Bethsaida, where they brought to Him a blind man, and begged of Him that He would touch him.
23 Iye anagwira dzanja la munthu wosaonayo napita naye kunja kwa mudzi. Atalavulira mʼmaso a munthuyo ndi kumusanjika manja, Yesu anafunsa kuti, “Kodi ukuona kalikonse?”
And He took the blind man by the hand, and led him out of the town; and having spit on his eyes, He laid his hands upon him, and asked him, If he saw any thing.
24 Iye anakweza maso nati, “Ndikuona anthu; akuoneka ngati mitengo imene ikuyendayenda.”
And he looked up, and said, I see men (as it were trees) walking.
25 Kenakanso Yesu anayika manja ake mʼmaso a munthuyo. Ndipo maso ake anatsekuka, naonanso, ndipo anaona zonse bwinobwino.
Then He put his hands again upon his eyes, and made him look up: and he was restored to sight, and saw them all plainly.
26 Yesu anamuwuza kuti apite kwawo nati, “Usapite mʼmudzimo.”
And He sent him away to his house, and said, Neither go into the town, nor tell any one in the town.
27 Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
Then Jesus and his disciples went out into the towns of Cesarea Philippi: and by the way He asked his disciples, saying, Whom do men say that I am?
28 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati ndinu mmodzi wa aneneri.”
And they answered, Some say, John the baptist; and others, Elias; and others, One of the prophets.
29 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu, mumati ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu.”
And He saith unto them, But whom say ye that I am? Peter answered and saith, Thou art the Christ.
30 Yesu anawachenjeza kuti asawuze wina aliyense za Iye.
And He charged them, that they should say this to no one concerning Him:
31 Iye anayamba kuwaphunzitsa kuti, “Mwana wa Munthu ayenera kumva zowawa zambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe, ndi aphunzitsi a malamulo, ndi kuti ayenera kuphedwa ndipo patatha masiku atatu adzaukanso.”
and began to tell them, that the Son of man must suffer much; and be rejected by the elders, and chief priests, and scribes; and be put to death: and after three days rise again.
32 Izi anaziyankhula momveka bwino, ndipo Petro anamutengera pambali ndipo anayamba kumudzudzula.
And this He spake plainly and openly. Upon which Peter began to rebuke Him.
33 Koma Yesu atatembenuka ndi kuyangʼana ophunzira ake, anamudzudzula Petro nati, “Choka pamaso panga Satana! Suganizira zinthu za Mulungu koma za anthu.”
But He turned about and looking on his disciples reproved Peter, saying, Get thee behind me Satan; for thou savourest not the things of God, but the things that be of men.
34 Kenaka anayitana gulu la anthu pamodzi ndi ophunzira ake nati: “Ngati wina aliyense afuna kunditsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake ndi kunditsata.
And calling the people and his disciples to Him, He said unto them, Whosoever is willing to come after me, let him deny himself, and take up his cross, and follow me:
35 Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine ndi cha Uthenga Wabwino, adzawupulumutsa.
for he that would save his life, shall lose it; but he that would lose his life for my sake and the gospel's, shall save it.
36 Kodi munthu adzapindulanji akalandira dziko lonse lapansi, koma ndi kutaya moyo wake?
For what shall it profit a man, if he gain the whole world, and lose his own soul?
37 Kapena nʼchiyani chomwe munthu angapereke chosinthana ndi moyo wake?
or what shall a man give as a ransom for his soul?
38 Ngati wina achita manyazi chifukwa cha Ine ndi mawu anga mu mʼbado uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wa Atate ake pamodzi ndi angelo oyera.”
for whosoever shall be ashamed of me, and of my words, in this degenerate and sinful age, of him will the Son of man be also ashamed, when He cometh in the glory of his Father, with the holy angels.