< Marko 8 >

1 Mʼmasiku amenewo gulu lina lalikulu la anthu linasonkhana. Popeza iwo analibe chakudya, Yesu anayitana ophunzira ake nati kwa iwo,
In those days, there being, again a large multitude, and they not having any thing to eat, calling near the disciples, he saith unto them—
2 “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala ali ndi Ine masiku atatuwa ndipo alibe chakudya.
I am moved with compassion towards the multitude, because, already three days, abide they with me, and they have nothing to eat;
3 Ngati nditawawuza kuti apite kwawo ali ndi njala, iwo adzakomoka mʼnjira chifukwa ena a iwo achokera kutali.”
and, if dismiss them fasting unto their home, they will be exhausted in the way, —and, certain of them, are, from afar.
4 Ophunzira ake anayankha nati, “Kodi ndi kuti kuthengo kuno kumene munthu angapeze buledi okwanira kuwadyetsa?”
And his disciples answered him—Whence shall any one be able, here, to fill, these, with bread, in a desert?
5 Yesu anafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
And he was questioning them—How many loaves have ye? and they said—Seven.
6 Iye anawuza gulu la anthu kuti likhale pansi. Atatenga malofu a buledi asanu ndi awiri, anayamika, nawanyema ndipo anapatsa ophunzira ake kuti agawire anthu, ndipo iwo anatero.
And he sendeth word to the multitude, to fall back upon the ground. And, taking the seven loaves, giving thanks, he brake, and was giving unto his disciples, that they might be setting before them; and they set before the multitude.
7 Analinso ndi tinsomba tochepa; Iye anayamikanso chifukwa cha nsombazo. Ndipo anawuza ophunzira kuti awagawire.
And they had a few small fishes; and, blessing them, he bade them set, these also, before them.
8 Anthu anadya ndipo anakhuta. Atamaliza, ophunzira anatola buledi ndi nsomba zotsalira ndi kudzaza madengu asanu ndi awiri.
And they did eat, and were filled, and took up remainders of broken pieces, seven hampers.
9 Panali amuna pafupifupi 4,000. Ndipo atawawuza kuti apite kwawo,
Now they were about four thousand; and he dismissed them.
10 analowa mʼbwato pamodzi ndi ophunzira ake napita ku dera la Dalamanuta.
And, straightway, entering into the boat with his disciples, he came into the parts of Dalmanutha;
11 Afarisi anabwera nayamba kumufunsa Yesu. Pomuyesa Iye, anamufunsa za chizindikiro chochokera kumwamba.
and forth came the Pharisees, and began discussing with him, seeking of him, a sign from the heaven, testing him.
12 Ndipo anatsitsa moyo nati, “Nʼchifukwa chiyani mʼbado uno ukufuna chizindikiro chodabwitsa? Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe chizindikiro chidzapatsidwa kwa iwo.”
And, deeply sighing in his spirit, he saith—Why, doth this generation seek, a sign? Verily, I say—there shall, not be given, to this generation, a sign.
13 Ndipo anawasiya, nalowanso mʼbwato ndi kuwolokera tsidya lina.
And leaving them, again, embarking, he departed unto the other side.
14 Ophunzira anayiwala kutenga buledi, kupatula buledi mmodzi yekha amene anali naye mʼbwato.
And they forgot to take loaves, and, save one loaf, they had nothing with them in the boat.
15 Yesu anawachenjeza kuti, “Samalani ndipo onetsetsani yisiti wa Afarisi ndi wa Herode.”
And he began charging them, saying—Mind! beware of the leaven of the Pharisees, and of the leaven of Herod!
16 Iwo anakambirana wina ndi mnzake ndipo anati, “Ndi chifukwa choti tilibe buledi.”
And they began deliberating one with another, because they had no loaves.
17 Yesu atadziwa zokambirana zawo anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukukambirana kuti mulibe buledi? Kodi inu simukuonabe kapena kuzindikira? Kodi mitima yanu ndi yowumitsidwa?
And, taking note, he saith unto them—Why do ye deliberate, because ye have no, loaves? Not yet perceive ye, neither understand, —keep ye your hearts, hardened?
18 Kodi muli ndi maso ndipo simukuona, ndi makutu ndipo mukulephera kumva? Kodi simukukumbukira?
Eyes having, see ye not? and ears having, hear ye not? and remember ye not
19 Pamene ndinagawa malofu asanu a buledi kwa anthu 5,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Khumi ndi awiri.”
when, the five loaves, I brake unto the five thousand, how many baskets, full of broken pieces, ye took up? They say unto him—Twelve, —
20 “Ndipo pamene ndinagawa malofu asanu ndi awiri a buledi, kwa anthu 4,000, ndi madengu angati amene munatoleramo buledi ndi nsomba zotsalira?” Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri.”
When the seven, unto the four thousand, how many hampers, full measure, of broken pieces, ye took up? And they say unto him—Seven. And he was saying unto them—
21 Iye anawafunsa kuti, “Kodi simumvetsetsabe?”
Not yet, do ye understand?
22 Iwo anafika ku Betisaida, ndipo anthu ena anabweretsa munthu wosaona ndipo anamupempha Yesu kuti amukhudze.
And they come into Bethsaida. And they bring unto him one blind, and beseech him that him, he would touch.
23 Iye anagwira dzanja la munthu wosaonayo napita naye kunja kwa mudzi. Atalavulira mʼmaso a munthuyo ndi kumusanjika manja, Yesu anafunsa kuti, “Kodi ukuona kalikonse?”
And, laying hold of the hand of the blind man, he brought him forth outside the village, and, spitting into his eyes, laying his hands upon him, he was asking him—Anything, seest thou?
24 Iye anakweza maso nati, “Ndikuona anthu; akuoneka ngati mitengo imene ikuyendayenda.”
and, looking up, he was saying—I see men, because, like trees, I behold them walking
25 Kenakanso Yesu anayika manja ake mʼmaso a munthuyo. Ndipo maso ake anatsekuka, naonanso, ndipo anaona zonse bwinobwino.
Then again, put he his hands upon his eyes, and he saw clearly, and was restored, and was seeing distinctly, in broad splendour, all things together.
26 Yesu anamuwuza kuti apite kwawo nati, “Usapite mʼmudzimo.”
And he sent him away unto his house, saying—Not even into the village, mayest thou enter.
27 Yesu ndi ophunzira ake anapita ku midzi yozungulira Kaisareya wa Filipo. Ali panjira, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati ndine yani?”
And forth went Jesus and his disciples, into the villages of Caesarea of Philip. And, in the way, he was questioning his disciples, saying unto them—Who, are men saying that I am?
28 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati ndinu mmodzi wa aneneri.”
And they answered him, saying—John the Immerser, and, others, Elijah, —and, others, One of the prophets.
29 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu, mumati ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu.”
And, he, went on to question them—But, who, say, ye, that I am? Peter, answering, saith unto him—Thou, art, the Christ.
30 Yesu anawachenjeza kuti asawuze wina aliyense za Iye.
And he straitly charged them, that, no one, they should tell concerning him.
31 Iye anayamba kuwaphunzitsa kuti, “Mwana wa Munthu ayenera kumva zowawa zambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe, ndi aphunzitsi a malamulo, ndi kuti ayenera kuphedwa ndipo patatha masiku atatu adzaukanso.”
And he began to be teaching them—The Son of Man, must needs suffer many things, and be rejected by the Elders and the High-priests and the Scribes, —and be slain; and, after three days, arise.
32 Izi anaziyankhula momveka bwino, ndipo Petro anamutengera pambali ndipo anayamba kumudzudzula.
And, openly, was he speaking the word. And Peter, taking him aside, began to rebuke him.
33 Koma Yesu atatembenuka ndi kuyangʼana ophunzira ake, anamudzudzula Petro nati, “Choka pamaso panga Satana! Suganizira zinthu za Mulungu koma za anthu.”
But, he, turning round and looking upon his disciples, rebuked Peter, and saith—Withdraw behind me, Satan! because thou art not regarding the things, of God, but the things, of men.
34 Kenaka anayitana gulu la anthu pamodzi ndi ophunzira ake nati: “Ngati wina aliyense afuna kunditsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kunyamula mtanda wake ndi kunditsata.
And, calling near the multitude with his disciples, he said unto them—If anyone willeth, after me, to come, let him deny himself, and take up his cross, and be following me.
35 Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine ndi cha Uthenga Wabwino, adzawupulumutsa.
For, whosoever willeth, his own life, to save, shall lose it, but, whosoever shall lose his life for the sake [of me and] of the glad-message, shall save it;
36 Kodi munthu adzapindulanji akalandira dziko lonse lapansi, koma ndi kutaya moyo wake?
For, what doth it profit a man, to gain the whole world, and be made to forfeit his life?
37 Kapena nʼchiyani chomwe munthu angapereke chosinthana ndi moyo wake?
For what can a man, give, in exchange for his life?
38 Ngati wina achita manyazi chifukwa cha Ine ndi mawu anga mu mʼbado uno wachigololo ndi wochimwa, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wa Atate ake pamodzi ndi angelo oyera.”
For, whosoever shall be ashamed of me and of my words, in this adulterous and sinful generation, the Son of Man also, will be ashamed, of him, whensoever he shall come, in the glory of his Father, with the holy messengers.

< Marko 8 >