< Marko 6 >
1 Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
And he went out from there, and came into his fatherland, and his disciples follow him.
2 Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
And having become sabbath, he began to teach in the synagogue. And many who heard him were astonished, saying, How are these things in this man? and, What is the wisdom that was given to him, and such mighty works happen by his hands?
3 Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
Is this not the carpenter, the son of Mary, and brother of James and Joses and Judah and Simon? And are not his sisters here with us? And they were offended by him.
4 Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
But Jesus said to them, A prophet is not without honor, except in his fatherland, and among his kin, and in his house.
5 Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
And he could do no mighty work there, none, except having laid his hands upon a few feeble men he healed them.
6 Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
And he marveled because of their unbelief. And he went around the villages teaching.
7 Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
And he summons the twelve, and began to send them forth in pairs. And he gave them authority over the unclean spirits.
8 Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
And he commanded them that they should take up nothing for the way, except only a staff-no scrip, no bread, no copper in the belt-
9 Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
but shod with sandals, and, Do not wear two coats.
10 Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
And he said to them, Wherever ye enter into a house, lodge there until ye depart from there.
11 Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
And as many as might not receive you nor hear you, as ye depart from there, shake off the dust under your feet for a testimony to them. Truly I say to you, it will be more tolerable for Sodom or Gomorrah in the day of judgment than for that city.
12 Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
And having departed, they preached that men should repent.
13 Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
And they cast out many demons, and anointed many feeble men with olive oil, and healed them.
14 Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
And king Herod heard, for his name had become well known. And he said, John, the man who immerses, was raised from the dead, and because of this the powers work in him.
15 Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
Others said, He is Elijah, and others said, He is a prophet, like one of the prophets.
16 Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
But Herod, when he heard, said, This is John whom I beheaded. He was raised from the dead.
17 Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
For Herod himself having sent forth, he arrested John, and bound him in prison because of Herodias, his brother Philip's wife, because he married her.
18 Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
For John said to Herod, It is not permitted for thee to have thy brother's wife.
19 Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
And Herodias was resentful toward him, and wanted to kill him. And she could not,
20 chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
for Herod feared John, knowing him to be a righteous and holy man, and he protected him. And having heard of him-the many things he was doing-he even heard of him gladly.
21 Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
And having become an opportune day, when Herod on his birthday made a dinner for his chiefs, and the high captains, and the leading men of Galilee,
22 Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
and the daughter of her (of Herodias) having come in and danced, and having pleased Herod and those who sat with the king, he said to the maiden, Ask of me whatever thou may want, and I will give to thee.
23 Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
And he swore to her, Whatever thou may ask of me, I will give to thee, as much as half of my kingdom.
24 Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
And having gone out, she said to her mother, What shall I ask? And she said, The head of John the immerser.
25 Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
And having come in straightaway with haste to the king, she asked, saying, I want that thou may give me, of it on a platter, the head of John the immerser.
26 Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
And the king, who became exceeding sorry, did not want to refuse her because of the oaths, and of those dining together.
27 Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
And straightaway having sent an executioner, the king commanded his head to be brought. And having departed, he beheaded him in the prison,
28 nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
and brought his head on a platter, and gave it to the maiden. And the maiden gave it to her mother.
29 Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
And when his disciples heard, they came and took up his corpse, and laid it in a sepulcher.
30 Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
And the apostles gather together to Jesus, and reported all to him, and how many things they did, and how many things they taught.
31 Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
And he said to them, Come ye yourselves in private into a desolate place, and rest a while. For there were many coming and going, and they had no opportunity even to eat.
32 Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
And they departed in the boat to a desolate place in private.
33 Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
And they saw them going. And many recognized him, and ran together on foot there from all the cities. And they went before them, and came together to him.
34 Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
And Jesus having come out, he saw a great multitude. And he felt compassion toward them, because they were as sheep not having a shepherd. And he began to teach them many things.
35 Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
And now many an hour having come to pass, his disciples having come to him, they say, The place is desolate, and it is now many an hour.
36 Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
Send them away, so that after going into the fields and villages around, they may buy loaves for themselves, for they do not have what they may eat.
37 Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
But having answered, he said to them, Give ye them to eat. And they say to him, After departing, shall we buy loaves of two hundred denarii, and give them to eat?
38 Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
And he says to them, How many loaves have ye? Go and see. And when they knew, they say, Five, and two fishes.
39 Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
And he commanded them to sit down, all by companies upon the green grass.
40 Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
And they sat down in groups, by hundreds and by fifties.
41 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
And after taking the five loaves and the two fishes, having looked up to heaven, he blessed, and broke the loaves in pieces, and he gave to the disciples so that they might set before them. And he distributed the two fishes to them all.
42 Onse anadya ndipo anakhuta,
And they all ate, and were filled.
43 ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
And they took up fragments, twelve baskets full, and from the fishes.
44 Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
And those who ate the loaves were five thousand men.
45 Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
And straightaway he compelled his disciples to enter into the boat, and to go ahead to the other side, to Bethsaida, while he himself would send the crowd away.
46 Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
And after sending them away, he departed onto the mountain to pray.
47 Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
And having become evening, the boat was in the midst of the sea, and he alone on the land.
48 Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
And he saw them toiling in rowing, for the wind was against them. And about the fourth watch of the night he comes to them, walking on the sea, and wanted to passed by them.
49 koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
But they, when they saw him walking on the sea, supposed it to be a ghost, and cried out.
50 pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
For they all saw him, and were troubled. And straightaway he spoke with them, and says to them, Cheer up. It is I, fear not.
51 Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
And he went up to them into the boat, and the wind ceased. And they were exceedingly amazed in themselves, extraordinarily so. And they wondered,
52 popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
for they did not understand about the loaves, for their heart was hardened.
53 Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
And having crossed over, they came to the land of Gennesaret, and moored to the shore.
54 Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
And when they came out of the boat, straightaway, having recognized him,
55 Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
after running around that whole region around, they began to carry about on beds those who were faring badly, where they heard he was there.
56 Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.
And wherever he entered, into villages or cities or fields, they laid those who were feeble in the marketplaces, and besought him that if they might but touch the hem of his garment. And as many as touched him were being healed.