< Marko 3 >

1 Nthawi inanso analowa mʼsunagoge, ndipo munthu wa dzanja lolumala anali momwemo.
အနန္တရံ ယီၑုး ပုန ရ္ဘဇနဂၖဟံ ပြဝိၐ္ဋသ္တသ္မိန် သ္ထာနေ ၑုၐ္ကဟသ္တ ဧကော မာနဝ အာသီတ်၊
2 Ena a iwo anafunafuna chifukwa chakuti akamuneneze Yesu, potero anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angamuchiritse tsiku la Sabata.
သ ဝိၑြာမဝါရေ တမရောဂိဏံ ကရိၐျတိ နဝေတျတြ ဗဟဝသ္တမ် အပဝဒိတုံ ဆိဒြမပေက္ၐိတဝန္တး၊
3 Yesu anati kwa munthu wolumala dzanjayo, “Imirira, bwera kuno kutsogolo.”
တဒါ သ တံ ၑုၐ္ကဟသ္တံ မနုၐျံ ဇဂါဒ မဓျသ္ထာနေ တွမုတ္တိၐ္ဌ၊
4 Ndipo Yesu anawafunsa kuti, “Kodi chololedwa ndi chiyani pa tsiku la Sabata: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kupha?” Koma iwo anakhala chete.
တတး ပရံ သ တာန် ပပြစ္ဆ ဝိၑြာမဝါရေ ဟိတမဟိတံ တထာ ဟိ ပြာဏရက္ၐာ ဝါ ပြာဏနာၑ ဧၐာံ မဓျေ ကိံ ကရဏီယံ? ကိန္တု တေ နိးၑဗ္ဒာသ္တသ္ထုး၊
5 Yesu anawayangʼana ndi mkwiyo ndipo powawidwa mtima chifukwa cha mitima yawo yowuma anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola, ndipo dzanja lake linachira.
တဒါ သ တေၐာမန္တးကရဏာနာံ ကာဌိနျာဒ္ဓေတော ရ္ဒုးခိတး ကြောဓာတ် စရ္တုဒၑော ဒၖၐ္ဋဝါန် တံ မာနုၐံ ဂဒိတဝါန် တံ ဟသ္တံ ဝိသ္တာရယ, တတသ္တေန ဟသ္တေ ဝိသ္တၖတေ တဒ္ဓသ္တော'နျဟသ္တဝဒ် အရောဂေါ ဇာတး၊
6 Kenaka Afarisi anatuluka nayamba kukonza chiwembu ndi Aherode mmene angamuphere Yesu.
အထ ဖိရူၑိနး ပြသ္ထာယ တံ နာၑယိတုံ ဟေရောဒီယဲး သဟ မန္တြယိတုမာရေဘိရေ၊
7 Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata.
အတဧဝ ယီၑုသ္တတ္သ္ထာနံ ပရိတျဇျ ၑိၐျဲး သဟ ပုနး သာဂရသမီပံ ဂတး;
8 Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni.
တတော ဂါလီလျိဟူဒါ-ယိရူၑာလမ်-ဣဒေါမ်-ယရ္ဒန္နဒီပါရသ္ထာနေဘျော လောကသမူဟသ္တသျ ပၑ္စာဒ် ဂတး; တဒနျး သောရသီဒနေား သမီပဝါသိလောကသမူဟၑ္စ တသျ မဟာကရ္မ္မဏာံ ဝါရ္တ္တံ ၑြုတွာ တသျ သန္နိဓိမာဂတး၊
9 Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize.
တဒါ လောကသမူဟၑ္စေတ် တသျောပရိ ပတတိ ဣတျာၑင်္ကျ သ နာဝမေကာံ နိကဋေ သ္ထာပယိတုံ ၑိၐျာနာဒိၐ္ဋဝါန်၊
10 Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze.
ယတော'နေကမနုၐျာဏာမာရောဂျကရဏာဒ် ဝျာဓိဂြသ္တား သရွွေ တံ သ္ပြၐ္ဋုံ ပရသ္ပရံ ဗလေန ယတ္နဝန္တး၊
11 Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!”
အပရဉ္စ အပဝိတြဘူတာသ္တံ ဒၖၐ္ဋွာ တစ္စရဏယေား ပတိတွာ ပြောစဲး ပြောစုး, တွမီၑွရသျ ပုတြး၊
12 Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.
ကိန္တု သ တာန် ဒၖဎမ် အာဇ္ဉာပျ သွံ ပရိစာယိတုံ နိၐိဒ္ဓဝါန်၊
13 Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye.
အနန္တရံ သ ပရွွတမာရုဟျ ယံ ယံ ပြတိစ္ဆာ တံ တမာဟူတဝါန် တတသ္တေ တတ္သမီပမာဂတား၊
14 Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira
တဒါ သ ဒွါဒၑဇနာန် သွေန သဟ သ္ထာတုံ သုသံဝါဒပြစာရာယ ပြေရိတာ ဘဝိတုံ
15 ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda.
သရွွပြကာရဝျာဓီနာံ ၑမနကရဏာယ ပြဘာဝံ ပြာပ္တုံ ဘူတာန် တျာဇယိတုဉ္စ နိယုက္တဝါန်၊
16 Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro);
တေၐာံ နာမာနီမာနိ, ၑိမောန် သိဝဒိပုတြော
17 Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu);
ယာကူဗ် တသျ ဘြာတာ ယောဟန် စ အာန္ဒြိယး ဖိလိပေါ ဗရ္ထလမယး,
18 Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote,
မထီ ထောမာ စ အာလ္ဖီယပုတြော ယာကူဗ် ထဒ္ဒီယး ကိနာနီယး ၑိမောန် ယသ္တံ ပရဟသ္တေၐွရ္ပယိၐျတိ သ ဤၐ္ကရိယောတီယယိဟူဒါၑ္စ၊
19 ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
သ ၑိမောနေ ပိတရ ဣတျုပနာမ ဒဒေါ် ယာကူဗျောဟန္ဘျာံ စ ဗိနေရိဂိၑ် အရ္ထတော မေဃနာဒပုတြာဝိတျုပနာမ ဒဒေါ်၊
20 Pambuyo pake Yesu analowa mʼnyumba, ndipo gulu la anthu linasonkhananso, kotero kuti Iye pamodzi ndi ophunzira ake sanapeze mpata kuti adye.
အနန္တရံ တေ နိဝေၑနံ ဂတား, ကိန္တု တတြာပိ ပုနရ္မဟာန် ဇနသမာဂမော 'ဘဝတ် တသ္မာတ္တေ ဘောက္တုမပျဝကာၑံ န ပြာပ္တား၊
21 Anthu a ku banja lake atamva zimenezi, anapita kuti akamutenga, pakuti ankanena kuti, “Wazungulira mutu.”
တတသ္တသျ သုဟၖလ္လောကာ ဣမာံ ဝါရ္တ္တာံ ပြာပျ သ ဟတဇ္ဉာနောဘူဒ် ဣတိ ကထာံ ကထယိတွာ တံ ဓၖတွာနေတုံ ဂတား၊
22 Ndipo aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anati, “Iye wagwidwa ndi Belezebabu! Ndi ulamuliro wa mkulu wa ziwanda akutulutsa ziwanda.”
အပရဉ္စ ယိရူၑာလမ အာဂတာ ယေ ယေ'ဓျာပကာသ္တေ ဇဂဒုရယံ ပုရုၐော ဘူတပတျာဗိၐ္ဋသ္တေန ဘူတပတိနာ ဘူတာန် တျာဇယတိ၊
23 Pamenepo Yesu anawayitana nawayankhula mʼmafanizo nati: “Kodi Satana angatulutse bwanji Satana?
တတသ္တာနာဟူယ ယီၑု ရ္ဒၖၐ္ဋာန္တဲး ကထာံ ကထိတဝါန် ၑဲတာန် ကထံ ၑဲတာနံ တျာဇယိတုံ ၑက္နောတိ?
24 Ngati ufumu ugawanikana mwa iwo okha, ufumu umenewo sungakhalitse.
ကိဉ္စန ရာဇျံ ယဒိ သွဝိရောဓေန ပၖထဂ် ဘဝတိ တရှိ တဒ် ရာဇျံ သ္ထိရံ သ္ထာတုံ န ၑက္နောတိ၊
25 Ngati nyumba igawanikana mwa iyo yokha, nyumba imeneyo singathe kuyima.
တထာ ကသျာပိ ပရိဝါရော ယဒိ ပရသ္ပရံ ဝိရောဓီ ဘဝတိ တရှိ သောပိ ပရိဝါရး သ္ထိရံ သ္ထာတုံ န ၑက္နောတိ၊
26 Ndipo ngati Satana adzitsutsa yekha sangathe kuyima; ulamuliro wake watha.
တဒွတ် ၑဲတာန် ယဒိ သွဝိပက္ၐတယာ ဥတ္တိၐ္ဌန် ဘိန္နော ဘဝတိ တရှိ သောပိ သ္ထိရံ သ္ထာတုံ န ၑက္နောတိ ကိန္တူစ္ဆိန္နော ဘဝတိ၊
27 Kunena zoona, palibe munthu angalowe mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kutenga katundu wake pokhapokha atayamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Pamenepo akhoza kumubera.
အပရဉ္စ ပြဗလံ ဇနံ ပြထမံ န ဗဒ္ဓါ ကောပိ တသျ ဂၖဟံ ပြဝိၑျ ဒြဝျာဏိ လုဏ္ဌယိတုံ န ၑက္နောတိ, တံ ဗဒွွဲဝ တသျ ဂၖဟသျ ဒြဝျာဏိ လုဏ္ဌယိတုံ ၑက္နောတိ၊
28 Ndikukuwuzani zoona kuti machimo onse ndi zamwano zonse za anthu zidzakhululukidwa,
အတောဟေတော ရျုၐ္မဘျမဟံ သတျံ ကထယာမိ မနုၐျာဏာံ သန္တာနာ ယာနိ ယာနိ ပါပါနီၑွရနိန္ဒာဉ္စ ကုရွွန္တိ တေၐာံ တတ္သရွွေၐာမပရာဓာနာံ က္ၐမာ ဘဝိတုံ ၑက္နောတိ,
29 koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
ကိန္တု ယး ကၑ္စိတ် ပဝိတြမာတ္မာနံ နိန္ဒတိ တသျာပရာဓသျ က္ၐမာ ကဒါပိ န ဘဝိၐျတိ သောနန္တဒဏ္ဍသျာရှော ဘဝိၐျတိ၊ (aiōn g165, aiōnios g166)
30 Ananena izi chifukwa anati, “Ali ndi mzimu woyipa.”
တသျာပဝိတြဘူတော'သ္တိ တေၐာမေတတ္ကထာဟေတေား သ ဣတ္ထံ ကထိတဝါန်၊
31 Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye.
အထ တသျ မာတာ ဘြာတၖဂဏၑ္စာဂတျ ဗဟိသ္တိၐ္ဌနတော လောကာန် ပြေၐျ တမာဟူတဝန္တး၊
32 Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, “Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani.”
တတသ္တတ္သန္နိဓော် သမုပဝိၐ္ဋာ လောကာသ္တံ ဗဘာၐိရေ ပၑျ ဗဟိသ္တဝ မာတာ ဘြာတရၑ္စ တွာမ် အနွိစ္ဆန္တိ၊
33 Iye anafunsa kuti, “Amayi ndi abale anga ndi ndani?”
တဒါ သ တာန် ပြတျုဝါစ မမ မာတာ ကာ ဘြာတရော ဝါ ကေ? တတး ပရံ သ သွမီပေါပဝိၐ္ဋာန် ၑိၐျာန် ပြတိ အဝလောကနံ ကၖတွာ ကထယာမာသ
34 Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, “Awa ndi amayi anga ndi abale anga!
ပၑျတဲတေ မမ မာတာ ဘြာတရၑ္စ၊
35 Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga.”
ယး ကၑ္စိဒ် ဤၑွရသျေၐ္ဋာံ ကြိယာံ ကရောတိ သ ဧဝ မမ ဘြာတာ ဘဂိနီ မာတာ စ၊

< Marko 3 >