< Marko 3 >
1 Nthawi inanso analowa mʼsunagoge, ndipo munthu wa dzanja lolumala anali momwemo.
Il entra de nouveau dans la synagogue, où se trouvait un homme dont la main était desséchée.
2 Ena a iwo anafunafuna chifukwa chakuti akamuneneze Yesu, potero anamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angamuchiritse tsiku la Sabata.
Ils le surveillaient, pour savoir s'il allait le guérir le jour du sabbat, afin de l'accuser.
3 Yesu anati kwa munthu wolumala dzanjayo, “Imirira, bwera kuno kutsogolo.”
Il dit à l'homme dont la main était desséchée: « Lève-toi. »
4 Ndipo Yesu anawafunsa kuti, “Kodi chololedwa ndi chiyani pa tsiku la Sabata: kuchita chabwino kapena kuchita choyipa, kupulumutsa moyo kapena kupha?” Koma iwo anakhala chete.
Il leur dit: « Est-il permis, le jour du sabbat, de faire du bien ou de faire du mal? De sauver une vie ou de tuer? » Mais ils gardèrent le silence.
5 Yesu anawayangʼana ndi mkwiyo ndipo powawidwa mtima chifukwa cha mitima yawo yowuma anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola, ndipo dzanja lake linachira.
Après les avoir regardés avec colère, attristé par l'endurcissement de leur cœur, il dit à l'homme: « Étends ta main. » Il l'étendit, et sa main fut rendue aussi saine que l'autre.
6 Kenaka Afarisi anatuluka nayamba kukonza chiwembu ndi Aherode mmene angamuphere Yesu.
Les pharisiens sortirent, et aussitôt ils conspirèrent avec les hérodiens contre lui, afin de le faire périr.
7 Yesu anachoka pamodzi ndi ophunzira ake napita ku nyanja, ndipo gulu lalikulu la anthu lochokera ku Galileya linamutsata.
Jésus se retira vers la mer avec ses disciples. Une grande foule le suivit, venant de la Galilée, de la Judée,
8 Atamva zonse zimene amachita, anthu ambiri anabwera kwa Iye kuchokera ku Yudeya, Yerusalemu, Idumeya ndi madera a ku tsidya kwa mtsinje wa Yorodani ndi ozungulira Turo ndi Sidoni.
de Jérusalem, de l'Idumée, au-delà du Jourdain, et des environs de Tyr et de Sidon. Une grande foule, apprenant quelles grandes choses il faisait, vint à lui.
9 Chifukwa cha gulu la anthu, anawuza ophunzira ake kuti apezeretu bwato likhale, kuti anthu angamupanikize.
Il dit à ses disciples de laisser une petite barque près de lui, à cause de la foule, afin qu'elle ne le presse pas.
10 Pakuti anachiritsa ambiri, kotero kuti iwo amene anali ndi matenda amakankhana kutsogolo kuti amukhudze.
Car il avait guéri beaucoup de gens, de sorte que tous ceux qui avaient des maladies se pressaient contre lui pour le toucher.
11 Nthawi iliyonse mizimu yoyipa ikamuona, imagwa pansi pamaso pake ndi kufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!”
Les esprits impurs, dès qu'ils le voyaient, se prosternaient devant lui et s'écriaient: « Tu es le Fils de Dieu! »
12 Koma anayichenjeza mwamphamvu kuti isanene kuti Iye anali ndani.
Il leur recommanda sévèrement de ne pas le faire connaître.
13 Yesu anakwera ku phiri ndipo anayitana amene anawafuna, ndipo anabwera kwa Iye.
Il monta sur la montagne, appela à lui ceux qu'il voulait, et ils allèrent à lui.
14 Iye anasankha khumi ndi awiri, nawayika akhale atumwi; pokhala ndi Iye aziwatuma kukalalikira
Il en établit douze, afin qu'ils fussent avec lui, et qu'il les envoyât prêcher
15 ndi kuti akhale ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda.
et avoir le pouvoir de guérir les maladies et de chasser les démons:
16 Awa ndi khumi ndi awiri amene anawasankha: Simoni (amene anapatsidwa dzina lakuti Petro);
Simon, à qui il donna le nom de Pierre;
17 Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi mʼbale wake Yohane (iwowa anawapatsa dzina lakuti Bowanege, ndiye kuti ana a bingu);
Jacques, fils de Zébédée, et Jean, frère de Jacques, qu'il appela Boanerges, ce qui signifie Fils du tonnerre;
18 Andreya, Filipo, Bartumeyu, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alufeyo, Tadeyo, Simoni Zelote,
André, Philippe, Barthélemy, Matthieu, Thomas, Jacques, fils d'Alphée, Thaddée, Simon le Zélote;
19 ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
et Judas Iscariote, qui le livra aussi. Puis il entra dans une maison.
20 Pambuyo pake Yesu analowa mʼnyumba, ndipo gulu la anthu linasonkhananso, kotero kuti Iye pamodzi ndi ophunzira ake sanapeze mpata kuti adye.
La foule se rassembla de nouveau, de sorte qu'elle ne put même pas manger du pain.
21 Anthu a ku banja lake atamva zimenezi, anapita kuti akamutenga, pakuti ankanena kuti, “Wazungulira mutu.”
Ses amis, l'ayant appris, se mirent à le saisir, car ils disaient: « Il est fou. »
22 Ndipo aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anati, “Iye wagwidwa ndi Belezebabu! Ndi ulamuliro wa mkulu wa ziwanda akutulutsa ziwanda.”
Les scribes qui descendaient de Jérusalem disaient: « Il a Béelzébul, » et: « C'est par le prince des démons qu'il chasse les démons. »
23 Pamenepo Yesu anawayitana nawayankhula mʼmafanizo nati: “Kodi Satana angatulutse bwanji Satana?
Il les convoqua et leur dit en paraboles: Comment Satan peut-il chasser Satan?
24 Ngati ufumu ugawanikana mwa iwo okha, ufumu umenewo sungakhalitse.
Si un royaume est divisé contre lui-même, ce royaume ne peut subsister.
25 Ngati nyumba igawanikana mwa iyo yokha, nyumba imeneyo singathe kuyima.
Si une maison est divisée contre elle-même, cette maison ne peut subsister.
26 Ndipo ngati Satana adzitsutsa yekha sangathe kuyima; ulamuliro wake watha.
Si Satan s'est élevé contre lui-même, et s'il est divisé, il ne peut subsister, mais il a une fin.
27 Kunena zoona, palibe munthu angalowe mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kutenga katundu wake pokhapokha atayamba wamumanga munthu wamphamvuyo. Pamenepo akhoza kumubera.
Mais nul ne peut entrer dans la maison de l'homme fort pour piller, s'il ne lie d'abord l'homme fort; alors il pillera sa maison.
28 Ndikukuwuzani zoona kuti machimo onse ndi zamwano zonse za anthu zidzakhululukidwa,
« En vérité, je vous le dis, tous les péchés des descendants de l'homme seront pardonnés, y compris leurs blasphèmes;
29 koma aliyense amene achitira mwano Mzimu Woyera sadzakhululukidwa pakuti wachita tchimo losatha.” (aiōn , aiōnios )
mais celui qui blasphème contre le Saint-Esprit n'a jamais été pardonné, mais il est sujet à une condamnation éternelle. » (aiōn , aiōnios )
30 Ananena izi chifukwa anati, “Ali ndi mzimu woyipa.”
-parce qu'ils disaient: « Il a un esprit impur. »
31 Pamenepo amayi ndi abale ake a Yesu anafika. Atayima kunja, anatuma wina kuti akamuyitane Iye.
Sa mère et ses frères arrivèrent, et, se tenant dehors, ils l'envoyèrent chercher.
32 Gulu la anthu linakhala momuzungulira Iye, ndipo anamuwuza kuti, “Amayi ndi abale anu ali panja akukufunani.”
Une foule était assise autour de lui, et on lui dit: « Voici ta mère, tes frères et tes sœurs qui te cherchent dehors. »
33 Iye anafunsa kuti, “Amayi ndi abale anga ndi ndani?”
Il leur répondit: « Qui sont ma mère et mes frères? »
34 Pamenepo anayangʼana anthu amene anakhala momuzungurira ndipo anati, “Awa ndi amayi anga ndi abale anga!
Regardant ceux qui étaient assis autour de lui, il dit: « Voici ma mère et mes frères!
35 Aliyense amene achita chifuniro cha Mulungu ndi mʼbale wanga ndi mlongo wanga ndi amayi anga.”
Car quiconque fait la volonté de Dieu est mon frère, ma sœur et ma mère. »