< Marko 2 >
1 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
Po nekaj dneh je ponovno vstopil v Kafarnáum, in razglasilo se je, da je v hiši.
2 Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
In nemudoma so bili zbrani mnogi, toliko, da tam ni bilo več prostora, da jih sprejme, ne, niti pred vrati ne; in oznanjal jim je besedo.
3 Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
In prišli so k njemu in prinesli nekoga, bolnega zaradi paralize, ki je bil prenašan od štirih.
4 Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
Ko pa zaradi gneče niso mogli priti bliže k njemu, so odkrili streho, kjer je bil. In ko so jo predrli, so spustili posteljo, na kateri je ležal bolni zaradi paralize.
5 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
Ko je Jezus videl njihovo vero, je rekel bolnemu zaradi paralize: »Sin, tvoji grehi so ti odpuščeni.«
6 Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
Toda bili so nekateri izmed pisarjev, ki so tam sedeli ter v svojih srcih razmišljali:
7 “Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
»Zakaj ta človek govori takšna bogokletja? Kdo lahko odpušča grehe razen Boga samega?«
8 Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
In takoj, ko je Jezus v svojem duhu zaznal, da so v sebi tako modrovali, jim je rekel: »Zakaj v svojih srcih razmišljate te besede?
9 Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
Ali je bolnemu zaradi paralize lažje reči: ›Tvoji grehi so ti odpuščeni‹ ali reči: ›Vstani in vzemi svojo posteljo ter hôdi?‹
10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
Toda da boste lahko vedeli, da ima Sin človekov na zemlji oblast odpuščati grehe, (reče bolnemu zaradi paralize)
11 “Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
pravim ti: ›Vstani in vzemi svojo posteljo ter pojdi svojo pot v svojo hišo.‹«
12 Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
In ta je takoj vstal, vzel posteljo ter pred njimi vsemi odšel, tako da so bili vsi osupli in slavili Boga, rekoč: »Nikoli tega nismo videli na tak način.«
13 Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
In ponovno je odšel naprej ob morski obali, in vsa množica je krenila k njemu in jih je učil.
14 Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
In ko je hodil mimo, je zagledal Levija, Alfejevega sina, ki je sedel pri kraju plačevanja davkov ter mu rekel: »Sledi mi.« In ta je vstal ter mu sledil.
15 Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
In pripetilo se je, ko je Jezus v njegovi hiši sedel pri obedu, da je tudi mnogo davkarjev in grešnikov sedelo skupaj z Jezusom in njegovimi učenci, kajti bilo jih je mnogo in so mu sledili.
16 Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
In ko so ga pisarji in farizeji videli jesti z davkarji in grešniki, so njegovim učencem rekli: »Kako to, da jé in pije z davkarji in grešniki?«
17 Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
Ko je Jezus to slišal, jim reče: »Tisti, ki so zdravi, nimajo nobene potrebe po zdravniku, temveč tisti, ki so bolni; nisem prišel klicat pravičnih, temveč grešnike h kesanju.«
18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
Janezovi učenci in učenci farizejev so se postili; in prišli so ter mu rekli: »Zakaj se Janezovi učenci in učenci farizejev postijo, tvoji učenci pa se ne postijo?«
19 Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
Jezus jim je rekel: »Ali se lahko otroci svatovske sobe postijo, dokler je z njimi ženin? Kolikor dolgo imajo s seboj ženina, se ne morejo postiti.
20 Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
Toda prišli bodo dnevi, ko bo ženin vzet proč od njih in tedaj, v tistih dneh, se bodo postili.
21 “Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
Tudi nihče ne prišije koščka novega oblačila na staro obleko; sicer bo nov košček, ki jo je zapolnil, odvzel iz stare in nastane hujša raztrganina.
22 Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
In novega vina nihče ne vliva v stare mehove, sicer novo vino mehove razžene, vino pa se izlije in mehovi bodo poškodovani; temveč mora biti novo vino vlito v nove mehove.«
23 Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
In pripetilo se je, da je na šabatni dan šel skozi žitna polja; in njegovi učenci so med hojo začeli smukati žitno klasje.
24 Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
Farizeji so mu rekli: »Glej, zakaj delajo na šabatni dan to, kar ni zakonito?«
25 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
Rekel jim je: »Ali niste nikoli brali, kaj je storil David, ko je imel potrebo in je bil lačen on in tisti, ki so bili z njim?
26 Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
Kako je v dneh vélikega duhovnika Abjatárja odšel v Božjo hišo in jedel hlebe navzočnosti, kar ni zakonito jesti [nikomur] razen duhovnikom in je dal tudi tem, ki so bili z njim?«
27 Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
In rekel jim je: »Šabat je bila narejena zaradi človeka, ne pa človek zaradi šabate,
28 Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”
zato je Sin človekov Gospod tudi [čez] šabat.«