< Marko 2 >

1 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
Og nogen dager derefter gikk han atter inn i Kapernaum, og det spurtes at han var hjemme.
2 Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
Og mange samlet sig, så de ikke lenger fikk rum, ikke engang ved døren, og han talte ordet til dem.
3 Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
Og de kom til ham med en verkbrudden, som blev båret av fire mann;
4 Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
og da de ikke kunde komme frem til ham for folketrengselen, tok de taket av der hvor han var, og brøt hull og firte ned sengen som den verkbrudne lå på.
5 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
Og da Jesus så deres tro, sa han til den verkbrudne: Sønn! dine synder er dig forlatt.
6 Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
Men nogen skriftlærde satt der og tenkte i sine hjerter:
7 “Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
Hvorfor taler denne mann så? Han spotter Gud; hvem kan forlate synder uten en, det er Gud?
8 Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
Og Jesus kjente straks i sin ånd at de tenkte så ved sig selv, og han sa til dem: Hvorfor tenker I slikt i eders hjerter?
9 Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
Hvad er lettest, enten å si til den verkbrudne: Dine synder er dig forlatt, eller å si: Stå op og ta din seng og gå?
10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
Men forat I skal vite at Menneskesønnen har makt på jorden til å forlate synder - så sier han til den verkbrudne:
11 “Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
Jeg sier dig: Stå op og ta din seng og gå hjem til ditt hus!
12 Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
Og han stod op og tok straks sin seng og gikk ut for alles øine, så alle blev ute av sig selv av forundring og priste Gud og sa: Slikt har vi aldri sett.
13 Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
Og han gikk atter ut til sjøen, og alt folket kom til ham, og han lærte dem.
14 Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
Og da han gikk videre, så han Levi, Alfeus' sønn, sitte på tollboden, og han sa til ham: Følg mig! Og han stod op og fulgte ham.
15 Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
Og det skjedde at han satt til bords i hans hus; og mange toldere og syndere satt til bords med Jesus og hans disipler; for det var mange av dem, og de fulgte ham.
16 Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
Og da de skriftlærde og fariseerne så at han åt sammen med toldere og syndere, sa de til hans disipler: Han eter og drikker med toldere og syndere!
17 Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
Og da Jesus hørte det, sa han til dem: De friske trenger ikke til læge, men de som har ondt; jeg er ikke kommet for å kalle rettferdige, men for å kalle syndere.
18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
Og Johannes' og fariseernes disipler holdt faste, og de kom og sa til ham: Hvorfor faster Johannes' disipler og fariseernes disipler, men dine disipler faster ikke?
19 Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
Og Jesus sa til dem: Kan vel brudesvennene faste så lenge brudgommen er hos dem? Så lenge de har brudgommen hos sig, kan de ikke faste.
20 Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
Men de dager skal komme da brudgommen blir tatt fra dem, og da skal de faste, på den dag.
21 “Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
Ingen syr en lapp av ukrympet tøi på et gammelt klædebon, ellers river den nye lapp et stykke med sig av det gamle, og riften blir verre.
22 Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
Og ingen fyller ny vin i gamle skinnsekker; ellers vil vinen sprenge sekkene og vinen spilles og sekkene ødelegges; men ny vin i nye skinnsekker!
23 Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
Og det skjedde at han gikk igjennem en aker på sabbaten, og hans disipler begynte å plukke aks mens de gikk der.
24 Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
Og fariseerne sa til ham: Se, hvorfor gjør de på sabbaten det som ikke er tillatt?
25 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
Og han sa til dem: Har I aldri lest hvad David gjorde da han var i nød og sultet, han selv og de som var med ham,
26 Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
hvorledes han gikk inn i Guds hus, da Abjatar var yppersteprest, og åt skuebrødene, som ingen har lov til å ete uten prestene, og gav også dem som var med ham?
27 Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
Og han sa til dem: Sabbaten blev til for menneskets skyld, og ikke mennesket for sabbatens skyld.
28 Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”
Så er da Menneskesønnen herre også over sabbaten.

< Marko 2 >