< Marko 2 >
1 Patapita masiku pangʼono, Yesu atalowanso mu Kaperenawo, zinamveka kuti wabwera ali mʼnyumba.
After some days He entered Capernaum again, and it soon became known that He was at home;
2 Choncho anthu ambiri anasonkhana kotero kuti panalibenso malo, ngakhale ndi pa khomo pomwe, ndipo Iye anawalalikira mawu.
and such numbers of people came together that there was no longer room for them even round the door. He was speaking His Message to them,
3 Amuna anayi anabwera, atanyamula munthu wofa ziwalo.
when there came a party of people bringing a paralytic--four men carrying him.
4 Popeza sakanatha kufika naye kwa Yesu chifukwa cha gulu la anthu, anasasula denga chapamwamba pamene panali Yesu, ndipo atabowoleza, anatsitsa mphasa yomwe munthu wofa ziwaloyo anagonapo.
Finding themselves unable, however, to bring him to Jesus because of the crowd, they untiled the roof just over His head, and after clearing an opening they lowered the mat on which the paralytic was lying.
5 Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati kwa wofa ziwaloyo, “Mwana, machimo ako akhululukidwa.”
Seeing their faith, Jesus said to the paralytic, "My son, your sins are pardoned."
6 Ndipo ena mwa aphunzitsi amalamulo anakhala pansi pomwepo, namaganiza mʼmitima mwawo kuti,
Now there were some of the Scribes sitting there, and reasoning in their hearts.
7 “Nʼchifukwa chiyani munthuyu ayankhula chotere? Iye akuchitira mwano Mulungu! Ndani angakhululukire munthu machimo kupatula Mulungu yekha?”
"Why does this man use such words?" they said; "he is blaspheming. Who can pardon sins but One--that is, God?"
8 Nthawi yomweyo Yesu anadziwa mu mzimu wake kuti izi ndi zimene ankaganiza mʼmitima yawo, ndipo anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukuganiza zinthu izi?
At once perceiving by His spirit that they were reasoning within themselves, Jesus asked them, "Why do you thus argue in your minds?
9 Chapafupi nʼchiyani; kunena kwa wofa ziwaloyu kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kuti, ‘Imirira, tenga mphasa yako ndipo yenda?’
Which is easier?--to say to this paralytic, 'Your sins are pardoned,' or to say, 'Rise, take up your mat, and walk?'
10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo.” Anati kwa wofa ziwaloyo,
But that you may know that the Son of Man has authority on earth to pardon sins" --He turned to the paralytic, and said,
11 “Ndikuwuza iwe, imirira, tenga mphasa yako ndipo pita kwanu.”
"To you I say, 'Rise, take up your mat and go home.'"
12 Anayimirira, nanyamula mphasa yake natuluka onse akumuona. Izi zinadabwitsa aliyense ndipo anayamika Mulungu nati, “Sitinaonepo zinthu ngati izi!”
The man rose, and immediately under the eyes of all took up his mat and went out, so that they were all filled with astonishment, gave the glory to God, and said, "We never saw anything like this."
13 Yesu anatulukanso napita kumbali ya nyanja. Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye, ndipo anayamba kuliphunzitsa.
Again He went out to the shore of the Lake, and the whole multitude kept coming to Him, and He taught them.
14 Pamene ankayendabe, anaona Levi mwana wa Alufeyo atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anamuwuza kuti, “Tsate Ine.” Ndipo Levi anayimirira namutsata Iye.
And as He passed by, He saw Levi the son of Alphaeus sitting at the Toll Office, and said to him, "Follow me." So he rose and followed Him.
15 Yesu atakalandira chakudya ku nyumba kwa Levi, amisonkho ambiri ndi “ochimwa” ankadya naye pamodzi ndi ophunzira ake, pakuti anali ambiri amene anamutsatira.
When He was sitting at table in Levi's house, a large number of tax-gatherers and notorious sinners were at table with Jesus and His disciples; for there were many such who habitually followed Him.
16 Pamene aphunzitsi amalamulo a Afarisi anamuona akudya ndi “ochimwa” ndi amisonkho, anafunsa ophunzira ake kuti, “Chifukwa chiyani amadya ndi olandira msonkho ndi ochimwa?”
But when the Scribes of the Pharisee sect saw Him eating with the sinners and the tax-gatherers, they said to His disciples, "He is eating and drinking with the tax-gatherers and sinners!"
17 Yesu atamva zimenezi, anawawuza kuti, “Anthu amene ali bwino safuna singʼanga koma odwala. Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa.”
Jesus heard the words, and He said, "It is not the healthy who require a doctor, but the sick: I did not come to appeal to the righteous, but to sinners."
18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi a Afarisi amasala kudya. Anthu ena anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Zitheka bwanji kuti ophunzira a Yohane ndi ophunzira a Afarisi amasala kudya, koma anu satero?”
(Now John's disciples and those of the Pharisees were keeping a fast.) And they came and asked Him, "How is it that John's disciples and those of the Pharisees are fasting, and yours are not?"
19 Yesu anayankha nati, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya bwanji pamene iye ali nawo pamodzi? Iwo sangatero, pamene iye ali nawo pamodzi.
"Can a wedding party fast while the bridegroom is among them?" replied Jesus. "So long as they have the bridegroom with them, fasting is impossible.
20 Koma nthawi idzafika pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo, ndipo pa tsiku limenelo adzasala kudya.
But a time will come when the Bridegroom will be taken away from them; then they will fast.
21 “Palibe amene amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale. Ngati atatero, chigamba chatsopanocho chidzazomola chovala chakalecho, kukulitsa chibowocho.
No one mends an old garment with a piece of unshrunk cloth. Otherwise, the patch put on would tear away from it--the new from the old--and a worse hole would be made.
22 Ndipo palibe amene amathira vinyo watsopano mʼmatumba akale a vinyo. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba a vinyo ndipo vinyoyo pamodzi ndi matumbawo zidzawonongeka. Ayi, satero, amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso.”
And no one pours new wine into old wineskins. Otherwise the wine would burst the skins, and both wine and skins would be lost. New wine needs fresh skins!"
23 Tsiku lina la Sabata, Yesu amadutsa pakati pa minda ya tirigu, ndipo ophunzira ake amayenda naye limodzi, nayamba kubudula ngala za tiriguyo.
One Sabbath He was walking through the wheatfields when His disciples began to pluck the ears of wheat as they went.
24 Afarisi anati kwa Iye, “Taonani, chifukwa chiyani akuchita chosaloledwa ndi lamulo pa Sabata?”
So the Pharisees said to Him, "Look! why are they doing what on the Sabbath is unlawful?"
25 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita pamene iye ndi anzake anali osowa ndi anamva njala?
"Have you never read," Jesus replied, "what David did when the necessity arose and he and his men were hungry:
26 Pa nthawi ya Abiatara mkulu wa ansembe, iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndi kudya buledi wopatulika amene amaloledwa kuti adye ndi ansembe okha. Ndipo anapereka wina kwa anzake.”
how he entered the house of God in the High-priesthood of Abiathar, and ate the Presented Loaves--which none but the priests are allowed to eat--and gave some to his men also?"
27 Pamenepo anawawuza kuti, “Sabata linapangidwira munthu, osati munthu kupangidwira Sabata.
And Jesus said to them: "The Sabbath was made for man, not man for the Sabbath;
28 Choncho Mwana wa Munthu ali Ambuye ngakhale wa Sabata.”
so that the Son of Man is Lord even of the Sabbath."