< Marko 15 >
1 Mmamawa, akulu a ansembe pamodzi ndi akuluakulu, aphunzitsi amalamulo ndi olamulira onse anamanga fundo. Anamumanga Yesu, namutenga ndi kukamupereka kwa Pilato.
and immediately (upon/to/against the/this/who *k*) early counsel/council to do/make: do the/this/who high-priest with/after the/this/who elder: Elder and scribe and all the/this/who council to bind the/this/who Jesus to carry off and to deliver (the/this/who *k*) Pilate
2 Pilato anafunsa kuti, “Kodi Iwe ndi Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
and to question it/s/he the/this/who Pilate you to be the/this/who king the/this/who Jew the/this/who then to answer it/s/he (to say *N(k)O*) you to say
3 Akulu a ansembe anamunenera zinthu zambiri.
and to accuse it/s/he the/this/who high-priest much
4 Ndipo Pilato anamufunsanso Iye kuti, “Kodi Iwe suyankhapo kanthu? Tamva zinthu zambiri akukunenerazi.”
the/this/who then Pilate again (to question *N(k)O*) it/s/he to say no to answer none look! how much/many? you (to accuse *N(K)O*)
5 Koma Yesu sanayankhebe, ndipo Pilato anadabwa.
the/this/who then Jesus no still none to answer so to marvel the/this/who Pilate
6 Pa nthawi ya Phwando, panali chizolowezi chomasula munthu wamʼndende amene anthu amupempha.
according to then festival to release: release it/s/he one prisoner (which to refuse/excuse *N(k)O*)
7 Munthu wotchedwa Baraba anali mʼndende pamodzi ndi anthu owukira amene anapha anthu pa nthawi ya chipolowe.
to be then the/this/who to say: call Barabbas with/after the/this/who insurrectionist to bind who/which in/on/among the/this/who uprising murder to do/make: do
8 Gulu la anthu linabwera kwa Pilato ndi kumufunsa kuti awachitire zimene amachita nthawi zonse.
and (to ascend *N(K)O*) the/this/who crowd be first to ask as/just as (always *ko*) to do/make: do it/s/he
9 “Kodi mukufuna kuti ndikumasulireni mfumu ya Ayuda?” Pilato anafunsa,
the/this/who then Pilate to answer it/s/he to say to will/desire to release: release you the/this/who king the/this/who Jew
10 podziwa kuti akulu a ansembe anamupereka Yesu kwa iye chifukwa cha nsanje.
to know for that/since: that through/because of envy to deliver it/s/he the/this/who high-priest
11 Koma akulu a ansembe anasonkhezera anthu kuti Pilato amasule Baraba mʼmalo mwa Yesu.
the/this/who then high-priest to incite the/this/who crowd in order that/to more: rather the/this/who Barabbas to release: release it/s/he
12 Pilato anawafunsa kuti, “Kodi nanga ndichite chiyani ndi uyu amene mukumutcha mfumu ya Ayuda?”
the/this/who then Pilate again to answer (to say *N(k)O*) it/s/he which? therefore/then to will/desire to do/make: do which to say: call (the/this/who *no*) king the/this/who Jew
13 Anafuwula kuti, “Mpachikeni!”
the/this/who then again to cry to crucify it/s/he
14 Pilato anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani? Wapalamula mlandu wotani?” Koma anafuwula kwambiri, “Mpachikeni!”
the/this/who then Pilate to say it/s/he which? for to do/make: do evil/harm: evil the/this/who then (excessively *N(k)O*) to cry to crucify it/s/he
15 Pilato pofuna kuwakondweretsa anthuwo, anawamasulira Baraba. Analamula kuti Yesu akwapulidwe mwankhanza, ndipo anamupereka kuti akapachikidwe.
the/this/who then Pilate to plan the/this/who crowd the/this/who sufficient to do/make: do to release: release it/s/he the/this/who Barabbas and to deliver the/this/who Jesus to whip in order that/to to crucify
16 Asilikali anamutenga Yesu ndi kupita naye mʼkati mwa nyumba yaufumu (dera lokhalako asilikali a mfumu) ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali.
the/this/who then soldier to lead away it/s/he in/inner/inwardly the/this/who palace/courtyard which to be praetorium and to call together all the/this/who band
17 Anamuveka Iye mwinjiro wofiira, kenaka analuka chipewa cha minga ndi kuyika pa mutu pake.
and (to dress *N(k)O*) it/s/he purple cloth and to put on it/s/he to weave thorny crown
18 Ndipo anayamba kunena kwa lye kuti, “Ulemu kwa inu Mfumu ya Ayuda!”
and be first to pay respects to it/s/he to rejoice (the/this/who *o*) (king *N(k)O*) the/this/who Jew
19 Ndipo anamugogoda pa mutu mobwerezabwereza ndi ndodo ndi kumulavulira. Anamugwadira ndi kumulambira Iye.
and to strike it/s/he the/this/who head reed/stick/pen and to spit on/at it/s/he and to place the/this/who a knee to worship it/s/he
20 Ndipo anamuchita chipongwe, anamuvula mwinjiro wofiira uja ndi kumuveka zovala zake. Kenaka anamutenga kuti akamupachike.
and when to mock it/s/he to strip it/s/he the/this/who purple cloth and to put on it/s/he the/this/who clothing (it/s/he *N(K)O*) and to lead out it/s/he in order that/to (to crucify *NK(o)*) it/s/he
21 Munthu wina ochokera ku Kurene, Simoni, abambo a Alekisanda ndi Rufasi amadutsa kuchokera ku dziko la kwawo, ndipo anamuwumiriza kuti anyamule mtanda.
and to force to pass one Simon Cyrene to come/go away from field the/this/who father Alexander and Rufus in order that/to to take up the/this/who cross it/s/he
22 Anafika naye Yesu pa malo otchedwa Gologota (kutanthauza kuti, malo a bade)
and to bear/lead it/s/he upon/to/against (the/this/who *no*) Golgotha place which to be (to mean *NK(o)*) Skull place
23 Kenaka anamupatsa Iye vinyo wosakaniza ndi mure, koma Iye sanamwe.
and to give it/s/he (to drink *K*) to mix with myrrh wine (which *N(k)O*) then no to take
24 Ndipo anamupachika Iye. Anachita maere ogawana zovala zake kuti aone chimene aliyense angatenge.
and (to crucify *N(k)O*) it/s/he (and *no*) (to divide *N(k)O*) the/this/who clothing it/s/he to throw: throw lot upon/to/against it/s/he which? which? to take up
25 Linali ora lachitatu mmawa pamene anamupachika Yesu.
to be then hour third and to crucify it/s/he
26 Chikwangwani cholembedwapo mlandu wake chinali choti: mfumu ya ayuda.
and to be the/this/who inscription the/this/who cause/charge it/s/he to write on the/this/who king the/this/who Jew
27 Achifwamba awiri anapachikidwanso pamodzi ndi Iye, wina kumanja kwake ndi wina kumanzere kwake.
and with it/s/he to crucify two robber/rebel one out from right and one out from left/south it/s/he
28 (Ndipo malemba anakwaniritsidwa amene amati, “Iye anayikidwa mʼgulu la anthu oyipa).”
(and to fulfill the/this/who a writing the/this/who to say and with/after lawless to count *K*)
29 Amene amadutsa pafupi anamunenera mawu amwano, akupukusa mitu yawo ndi kuti, “Haa! Iwe amene udzawononga Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso masiku atatu,
and the/this/who to pass by/through to blaspheme it/s/he to move the/this/who head it/s/he and to say aha! the/this/who to destroy/lodge the/this/who temple and to build in/on/among Three day
30 tsika kuchoka pa mtandapo ndipo udzipulumutse wekha!”
to save you (and *k*) (to come/go down *N(k)O*) away from the/this/who cross
31 Chimodzimodzinso akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamunyoza Iye pakati pawo. Iwo anati, “Anapulumutsa ena, koma sangathe kudzipulumutsa yekha!
similarly (then *k*) and the/this/who high-priest to mock to/with one another with/after the/this/who scribe to say another to save themself no be able to save
32 Musiyeni Khristu, Mfumu ya Aisraeli, atsike tsopano kuchoka pa mtanda, kuti ife tione ndi kukhulupirira.” Iwonso amene anapachikidwa naye pamodzi anamulalatira.
the/this/who Christ the/this/who king (the/this/who *k*) Israel to come/go down now away from the/this/who cross in order that/to to perceive: see and to trust (in) (it/s/he *O*) and the/this/who to crucify with (with *no*) it/s/he to revile it/s/he
33 Pa ora lachisanu ndi chimodzi masana mdima unabwera pa dziko lonse mpaka pa ora lachisanu ndi chinayi masana.
(and *no*) to be (then *k*) hour sixth darkness to be upon/to/against all the/this/who earth: country until hour ninth (hour)
34 Pa ora lachisanu ndi chinayi Yesu analira mofuwula kuti, “Eloi, Eloi, lama sabakitani?” Kutanthauza kuti, “Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?”
and the/this/who ninth (hour) (the/this/who *k*) hour to cry out the/this/who Jesus voice/sound: voice great (to say *k*) Eloi Eloi why? sabachthani which to be to mean the/this/who God me the/this/who God me toward which? to leave behind me
35 Ena amene anali pafupi atamva izi anati, “Tamverani, akuyitana Eliya.”
and one the/this/who to stand by to hear to say (look! *N(k)O*) Elijah to call
36 Munthu wina anathamanga, natenga chinkhupule atachiviyika mu vinyo wosasa, anachizika ku mtengo, ndi kumupatsa Yesu kuti amwe. Munthuyo anati, “Musiyeni yekha tsopano. Tiyeni tione ngati Eliya angabwere kudzamutsitsa.”
to run then (one *N(k)O*) and to fill sponge vinegar to put on (and/both *k*) reed/stick/pen to water it/s/he to say to release: leave to perceive: see if to come/go Elijah to take down it/s/he
37 Ndi mawu ofuwula, Yesu anapuma komaliza.
the/this/who then Jesus to release: leave voice/sound: voice great to expire
38 Chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi.
and the/this/who curtain the/this/who temple to split toward two away from from above/again until under
39 Ndipo Kenturiyo, amene anayima patsogolo pa Yesu, atamva kulira kwake ndi kuona mmene anafera anati, “Zoonadi, uyu anali Mwana wa Mulungu.”
to perceive: see then the/this/who centurion the/this/who to stand by out from hostile it/s/he that/since: that thus(-ly) (to cry *KO*) to expire to say truly this/he/she/it the/this/who a human son God to be
40 Amayi ena anali patali kuonerera. Pakati pawo panali Mariya Magadalena, Mariya amayi a Yakobo wamngʼono ndi Yose ndi Salome.
to be then and woman away from from afar to see/experience in/on/among which (to be *ko*) and Mary the/this/who Magdalene and Mary the/this/who (the/this/who *k*) James the/this/who small and Joseph mother and Salome
41 Amayi awa ankamutsatira Iye mu Galileya ndi kumutumikira Iye pa zosowa zake. Amayi enanso ambiri amene anabwera naye ku Yerusalemu analinso pomwepo.
which (and *ko*) when to be in/on/among the/this/who Galilee to follow it/s/he and to serve it/s/he and another much the/this/who to ascend with it/s/he toward Jerusalem
42 Linali Tsiku Lokonzekera (kunena kuti, tsiku lomwe limatsatizana ndi Sabata). Choncho madzulo atayandikira,
and already evening to be since to be Preparation which to be to/with Sabbath
43 Yosefe wa ku Arimateyu, mkulu wolamulira odziwika bwino, amene amadikirira ufumu wa Mulungu, anapita kwa Pilato molimba mtima ndi kukapempha mtembo wa Yesu.
(to come/go *N(k)O*) Joseph the/this/who away from Arimathea proper member of a council which and it/s/he to be to wait for/welcome the/this/who kingdom the/this/who God be bold to enter to/with (the/this/who *no*) Pilate and to ask the/this/who body the/this/who Jesus
44 Pilato anadabwa pakumva kuti anali atamwalira kale. Anayitana Kenturiyo, namufunsa ngati Yesu anali atamwalira kale.
the/this/who then Pilate to marvel if already to die/be dead and to call to/summon the/this/who centurion to question it/s/he if (of old *NK(o)*) to die
45 Atawuzidwa ndi Kenturiyo kuti zinali motero, anapereka mtembowo kwa Yosefe.
and to know away from the/this/who centurion to give the/this/who (corpse *N(k)O*) the/this/who Joseph
46 Choncho Yosefe anagula nsalu yabafuta, natsitsa thupi, ndipo analikulunga mʼnsalu, naliyika mʼmanda amene anawagoba pa mwala. Kenaka anagubuduza mwala umene anatseka nawo mandawo.
and to buy linen (and *k*) to take down it/s/he to enwrap the/this/who linen and (to place *NK(O)*) it/s/he in/on/among (grave *NK(o)*) which to be to hew out from rock and to roll before stone upon/to/against the/this/who door the/this/who grave
47 Mariya Magadalena ndi Mariya amayi a Yose anaona kumene anamuyika Yesu.
the/this/who then Mary the/this/who Magdalene and Mary the/this/who Joseph to see/experience where? (to place *N(k)O*)