< Marko 14 >

1 Tsopano panali patatsala masiku awiri okha kuti tsiku la Paska ndi Phwando la Buledi wopanda yisiti lifike, ndipo akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ankafunafuna mpata woti amugwire Yesu ndi kumupha.
За два ж дні була Пасха й Опрі́сноки. А первосвященики й книжники стали шукати, я́к би пі́дступом взяти Його та забити.
2 Iwo anati, “Koma osati nthawi yaphwando, chifukwa anthu angachite chiwawa.”
Вони говорили: „Та не в свято, щоб бува́ колотне́ча в наро́ді не сталась“.
3 Pamene Iye anali mʼBetaniya, atakhala pa tebulo akudya mʼnyumba ya munthu wodziwika kuti Simoni wakhate, anabwera mayi ndi botolo la mafuta onunkhira amtengo wapamwamba opangidwa ndi nadi. Anaphwanya botololo nakhuthula mafutawo pa mutu wa Yesu.
Коли ж Ісус був у Віфанії, у домі Си́мона, на проказу слабого, і сидів при столі, підійшла одна жінка, аляба́строву пляшечку маючи щирого на́рдового дуже ці́нного мира. І розбила вона аляба́строву пляшечку, і вилила миро на голову Йому!
4 Ena mwa iwo amene analipo, anakwiya nati kwa wina ndi mnzake, “Chifukwa chiyani akuwononga mafuta onunkhirawa?
А дехто обу́рювались між собою й каза́ли: „На́що таке марнотра́тство на миро?
5 Akanatheka kugulitsidwa ndi ndalama zambiri zoposa malipiro a pa chaka ndipo ndalamazo ndi kupatsa osauka.” Ndipo anamudzudzula iye mwaukali.
Бо можна було б це миро продати більше, як за три сотні динаріїв, і вбогим роздати“. І нарікали на неї.
6 Yesu anati, “Musiyeni, chifukwa chiyani mukumuvutitsa? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
Ісус же сказав: „Залиші́ть її! Чого при́крість їй робите? Вона добрий учинок зробила Мені.
7 Anthu osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, ndipo mukhoza kuwathandiza nthawi iliyonse mungafune. Koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
Бо вбогих ви маєте за́вжди з собою, і коли схочете, можете їм робити добро, — Мене ж не постійно ви маєте.
8 Wachita zimene akanatha. Wathira mafuta onunkhira pa thupi langa nthawi isanakwane kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
Що могла, те зробила вона: заздалегі́дь намасти́ла Моє тіло на по́хорон.
9 Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwino udzalalikidwa pa dziko lonse, zimene wachitazi zidzanenedwa pomukumbukira iye.”
Поправді кажу́ вам: де тільки ця Єва́нгелія проповідувана буде в ці́лому світі, — на пам'ятку їй буде сказане й те, що́ зробила вона!“
10 Kenaka Yudasi Isikarioti, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anapita kwa akulu a ansembe kuti akamupereke Yesu.
Юда ж Іскаріо́тський, один із Дванадцятьо́х, подався до первосвящеників, щоб їм Його видати.
11 Iwo anakondwa pakumva zimenezi ndipo analonjeza kumupatsa iye ndalama. Ndipo ankadikira mpata wabwino woti amupereke.
А вони, як почули, зраділи, і обіцяли йому срібнякі́в за те дати. І він став вишукувати, я́к би слушного ча́су їм видати Його.
12 Pa tsiku loyamba la Phwando la Buledi wopanda yisiti, nthawi imene mwa mwambo inali ya kupha mwana wankhosa wa Paska, ophunzira a Yesu anafunsa Iye kuti, “Mufuna tipite kuti kumene tikakonzekere kuti mukadyere Paska?”
А першого дня Опрі́сноків, коли пасху приношено в жертву, сказали Йому Його учні: „Куди хочеш, щоб пішли й приготува́ли ми Тобі пасху спожити?“
13 Pamenepo anatumiza awiri mwa ophunzira ake, nawawuza kuti, “Pitani mu mzinda, ndipo mukakumana ndi mwamuna wonyamula mtsuko wa madzi. Kamutsatireni iye.
І посилає Він двох із Своїх учнів, і каже до них: „Підіть до міста, і стріне вас чоловік, що не́стиме в гле́кові воду, — то йдіть за ним.
14 Kawuzeni mwini nyumba imene iye akalowemo kuti, ‘Aphunzitsi akufunsa: kodi chili kuti chipinda changa cha alendo, kumene ndidyere Paska ndi ophunzira anga?’
І там, куди він уві́йде, скажіть до госпо́даря дому: „Учитель питає: „Де кімна́та Моя, в якій Я споживу́ зо Своїми у́чнями пасху?“
15 Iye adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala kale ndi zonse ndi chokonzedwa kale. Katikonzereni ife Paska kumeneko.”
І він вам покаже велику го́рницю, ви́стелену та готову: там приготуйте для нас“.
16 Ophunzirawo anachoka, napita mu mzindawo ndipo anakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Choncho anakakonza Paska.
І учні пішли, і до міста прийшли, і знайшли, як Він їм сказав, — і зачали́ вони пасху готува́ти.
17 Ndipo kutada Yesu anafika ndi khumi ndi awiriwo.
А коли настав вечір, Він приходить із Дванадцятьма́.
18 Pamene ankadya pa tebulo Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka, mmodzi amene akudya ndi Ine.”
І як сиділи вони при столі й споживали, промовив Ісус: „Поправді кажу вам, що один з-поміж вас, „який споживає зо Мною“, видасть Мене́“.
19 Iwo anamva chisoni, ndipo mmodzi ndi mmodzi anati kwa Iye, “Kodi ndine?”
Вони зачали́ сумувати, і один по одно́му питати Його: „Чи не я?“
20 Iye anayankha kuti, “Ndi mmodzi mwa khumi ndi awirinu, amene akusunsa buledi mʼmbale pamodzi ndi Ine.
А Він їм сказав: „Один із Дванадцятьо́х, що в миску мача́є зо Мною.
21 Mwana wa Munthu adzapita monga momwe zinalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene adzapereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
Людський Син справді йде, як про Нього написано; та горе тому́ чоловікові, що видасть він Лю́дського Сина! Було б краще тому чоловікові, коли б він не родився!“
22 Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, ili ndi thupi langa.”
Як вони ж споживали, Ісус узяв хліб, і поблагословив, поламав, і дав їм, і сказав: „Прийміть, споживайте, це — тіло Моє!“
23 Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo ndipo onse anamweramo.
І взяв Він чашу, і, вчинивши подяку, подав їм, — і пили́ з неї всі.
24 Iye anawawuza kuti, “Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri.
І промовив до них: „Це — кров Моя Ново́го Заповіту, що за багатьох проливається.
25 Zoonadi, ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mphesa mpaka tsikulo pamene ndidzamwa chatsopano mu ufumu wa Mulungu.”
Поправді кажу́ вам, що віднині не пи́тиму Я від плоду виноградного до того дня, як нови́м буду пити його в Царстві Божім!“
26 Atayimba nyimbo, anapita ku phiri la Olivi.
А коли відспівали вони, на го́ру Оливну пішли.
27 Yesu anati, “Nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha Mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
Промовляє тоді їм Ісус: „Усі ви споку́ситесь ночі цієї, як написано: „Уражу́ Па́стиря, — і розпоро́шаться вівці!“
28 Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
По воскресінні ж Своїм Я вас ви́переджу в Галілеї“.
29 Petro anati, “Ngakhale onse adzakuthaweni, ine sindidzatero.”
І відізвався до Нього Петро: „Хоч спокусяться й усі, — та не я!“
30 Yesu anayankha kuti, “Zoona ndikukuwuza kuti lero lino, usiku uno, tambala asanalire kawiri, iweyo udzandikana katatu.”
Ісус же йому відказав: „Поправді кажу́ тобі, що сьогодні, цієї ось ночі, перше ніж заспіває півень дві́чі, — відречешся ти три́чі від Мене!“
31 Koma Petro ananenetsa kuti, “Ngakhale kutakhala kufa nanu, ine sindidzakukanani.” Ndipo ena onse ananena chimodzimodzi.
А він ще сильніш запевняв: „Коли б мені й умерти з Тобою, — я не відречу́ся Тебе!“Так же само сказали й усі.
32 Ndipo anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Khalani pano pamene Ine ndi kupemphera.”
І приходять вони до місцевости, на ім'я́ Гефсима́нія, і каже Він у́чням Своїм: „Посидьте ви тут, поки Я помолюся“.
33 Iye anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane, ndipo anayamba kumva chisoni kwambiri ndi kuvutika mu mtima.
І, взявши з Собою Петра, і Якова та Івана, Він зачав сумувати й тужи́ти.
34 Iye anawawuza kuti, “Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo musagone.”
І сказав Він до них: „Обго́рнена сумом смерте́льним душа Моя! Залиші́ться тут і пильнуйте!“
35 Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi ndi kupemphera kuti ngati ndi kotheka oralo limupitirire.
І Він відійшов трохи далі, припав до землі, та й благав, щоб, як можна, минула Його ця година.
36 Iye anati, “Abba, Atate, zinthu zonse ndi zotheka ndi Inu. Chotsereni chikhochi. Komabe chitani zimene Inu mukufuna, osati zimene Ine ndikufuna.”
І благав Він: „Авва -Отче, — Тобі все можливе: пронеси мимо Мене цю чашу! А проте, — не чого хочу Я, але чого Ти“.
37 Kenaka anabwerera kwa ophunzira ake ndipo anawapeza akugona, Iye anati kwa Petro, “Simoni, kodi uli mtulo? Kodi simukanatha kukhala maso kwa ora limodzi?
І вернувся, і знайшов їх, що спали, та й каже Петрові: „Симоне, спиш ти? Однієї години не зміг попильнува́ти?
38 Khalani tcheru ndi kupemphera kuti musalowe mʼmayesero. Mzimu ukufuna, koma thupi ndi lofowoka.”
Пильнуйте й моліться, щоб не впасти в спокусу, — бадьо́рий бо дух, але не́мічне тіло!“
39 Kenakanso anachoka ndi kukapemphera chimodzimodzi.
І зно́ву пішов і молився, те саме промовивши слово.
40 Iye atabwerera, anawapezanso akugona, chifukwa mʼmaso mwawo munadzaza tulo. Iwo sanadziwe choti anene kwa Iye.
А вернувшись, ізнову знайшов їх, що спали, бо зважні́ли їм очі були́. І не знали вони, що́ Йому відказати.
41 Atabweranso kachitatu, anawafunsa kuti, “Kodi mukugonabe ndi kupumula? Pakwana! Nthawi yafika. Taonani, Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa.
І вернувсь Він утретє, та й каже до них: „Ви ще далі спите́ й спочиваєте? Скі́нчено, — надійшла та година: у руки грішникам ось видається Син Лю́дський!
42 Nyamukani! Tiyeni tizipita! Uyu wondipereka Ine wafika!”
Уставайте, ходім, — ось набли́зивсь Мій зрадник“.
43 Iye akuyankhulabe, Yudasi, mmodzi mwa khumi ndi awiriwo, anatulukira. Anali ndi gulu la anthu litanyamula malupanga ndi zibonga, otumidwa ndi akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo, ndi akuluakulu.
І зараз, як Він ще говорив, прийшов Юда, один із Дванадцятьо́х, а з ним люди з мечами та ки́ями від первосвящеників, і книжників, і старших.
44 Tsopano womupereka anapangana chizindikiro ndi iwo kuti: “Amene ndikapsompsone ndi iyeyo; mukamugwire ndi kumutenga ali womangidwa.”
А зрадник Його дав був знака їм, кажучи: „Кого я поцілую, то Він, — беріть Його, і обере́жно ведіть“.
45 Atapita kwa Yesu nthawi yomweyo, Yudasi anati, “Aphunzitsi,” ndipo anapsompsona.
І, прийшовши, підійшов він негайно та й каже: „Учителю!“І поцілував Його.
46 Anthu anamugwira Yesu ndi kumumanga.
Вони ж руки свої накла́ли на Нього, — і схопи́ли Його.
47 Kenaka mmodzi wa iwo amene anayima pafupipo anatulutsa lupanga lake nakhapa wantchito wa wamkulu wa ansembe, nʼkudula khutu lake.
А один із тих, що стояли навко́ло, меча ви́хопив та й рубону́в раба́ первосвященика, — і відтяв йому вухо.
48 Yesu anati, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira, kuti mubwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira?
А Ісус їм промовив у відповідь: „Немов на розбійника вийшли з мечами та ки́ями, щоб узяти Мене.
49 Tsiku ndi tsiku ndinali ndi inu, kuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, koma inu simunandigwire. Koma malemba ayenera kukwaniritsidwa.”
Я щодня був із вами у храмі, навчаючи, — і Мене не взяли́ ви. Але, щоб збулися Писа́ння“.
50 Pamenepo ophunzira ake onse anathawa namusiya yekha.
Тоді всі полиши́ли Його й повтікали.
51 Mnyamata wamngʼono amene anangofundira nsalu yokha, wopanda chovala ankamutsatira Yesu. Atamugwira,
Один же юна́к, по наго́му заго́рнений у покрива́ло, ішов услід за Ним. І хапа́ють його.
52 anathawa wamaliseche kusiya nsalu yake mʼmbuyo.
Але він, покрива́ло поки́нувши, утік наги́й.
53 Anamutengera Yesu kwa mkulu wa ansembe, ndipo akulu a ansembe, akuluakulu ndi aphunzitsi amalamulo anasonkhana pamodzi.
А Ісуса вони повели́ до первосвященика. І зійшлися всі первосвященики й старші та книжники.
54 Petro anamutsatira ali patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Kumeneko anakhala pansi ndi alonda namawotha moto.
Петро ж зда́лека йшов услід за Ним до сере́дини дво́ру первосвященика; і сидів він із службою, і грівсь при огні.
55 Akulu a ansembe ndi onse olamulira a Ayuda ankafunafuna umboni womutsutsa Yesu kuti amuphe, koma sanapeze wina uliwonse.
А первосвященики та ввесь синедріо́н шукали посві́дчення на Ісуса, щоб Йому заподіяти смерть, — і не знахо́дили.
56 Ambiri anamunenera Iye maumboni abodza, koma maumboni awo sanagwirizane.
Бо багато-хто свідчив фальши́во на Нього, але́ не було́ згідних сві́дчень.
57 Kenaka ena anayimirira namunenera umboni wonama womutsutsa Iye kunena kuti,
Тоді деякі встали, і кривосві́дчили супроти Нього й казали:
58 “Tamumva akunena kuti, ‘Ndidzawononga Nyumba ya Mulungu iyi yopangidwa ndi anthu ndipo mʼmasiku atatu ndidzamanga ina, osati yopangidwa ndi munthu.’”
„Ми чули, як Він говорив: Я зруйную цей храм рукотво́рний, — і за три дні збудую інший, нерукотво́рний“.
59 Ngakhale iwonso umboni wawo sunagwirizane.
Але й так не було́ їхнє свідчення згідне.
60 Kenaka mkulu wa ansembe anayimirira pakati pawo namufunsa Yesu kuti, “Kodi suyankha? Kodi umboni uwu ndi wotani umene anthu akukuchitira?”
Тоді встав насере́дині первосвященик, та й Ісуса спитав і сказав: „Ти нічо́го не відповідаєш, що свідчать вони проти Тебе?“
61 Koma Yesu anakhala chete ndipo sanayankhe. Mkulu wa ansembe anabwereza kumufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Khristu Mwana wa Wodalitsikayo?”
Він же мовчав, і нічого не відповідав. Первосвященик ізно́ву спитав Його, до Нього говорячи: „Чи Христос Ти, Син Благослове́нного?“
62 Yesu anati, “Ndine, ndipo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera mʼmitambo ya kumwamba.”
А Ісус відказав: „Я! І побачите ви Сина Лю́дського, що сидітиме по прави́ці сили Божої, і на хмарах небесних прихо́дитиме!“
63 Mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zaunsembe zake. Iye anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani tikufuna mboni zinanso?
Роздер тоді первосвященик одежу свою та й сказав: „На що́ нам ще свідки потрібні?
64 Mwamva mwanowo. Muganiza chiyani?” Onse anavomereza kuti ndi woyenera imfa.
Ви чули цю богозневагу. Як вам здається?“Вони ж усі присудили, що Він умерти повинен.
65 Kenaka ena anayamba kumulavulira malovu; anamumanga mʼmaso, namumenya ndi zibakera ndipo anati, “Nenera!” Ndipo asilikali anamutenga namumenya.
Тоді деякі стали плювати на Нього, і закривати обличчя Йому, і бити Його та казати Йому: „Пророкуй!“Служба теж Його била по що́ках.
66 Petro ali chakumunsi kwa bwalo la milandu, mmodzi wa atsikana a ntchito a mkulu wa ansembe anabwera.
А коли Петро був на подві́р'ї надо́лі, приходить одна із служниць первосвященика,
67 Ataona Petro akuwotha moto, anamuyangʼanitsitsa. Iye anati, “Iwenso unali pamodzi ndi Mnazareti, Yesu.”
і як Петра вона вгледіла, що грівся, подивилась на нього та й каже: „І ти був із Ісусом Назаряни́ном!“
68 Koma iye anakana nati, “Sindikudziwa kapena kumvetsetsa zimene ukuyankhula.” Ndipo anachoka napita ku chipata.
Він же відрікся, говорячи: „Не відаю, і не розумію, що́ кажеш“. І вийшов назо́вні, на нереддвір'я. І заспівав тоді півень.
69 Pamene mtsikana wantchitoyo anamuona iye, anatinso kwa iwo amene anayimirira pomwepo, “Munthu uyu ndi mmodzi mwa iwo.”
Служниця ж, коли його вгледіла, стала знов говорити прия́вним: „Цей із них!“
70 Anakananso kachiwiri. Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pafupi anati kwa Petro, “Zoonadi ndiwe mmodzi wa iwo, pakuti ndiwe mu Galileya.”
І він зно́ву відрікся. Незаба́ром же знов говорили прия́вні Петрові: „Поправді, ти з них, — бо ти галіле́янин. Та й мо́ва твоя́ така са́ма“.
71 Iye anayamba kudzitemberera, nalumbira kuti, “Sindimudziwa munthu ameneyu.”
А він став клясти́сь та божитись: „Не знаю Цього Чоловіка, про Якого говорите ви!“
72 Nthawi yomweyo tambala analira kachiwiri. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Yesu ananena anamuwuza kuti, “Tambala asanalire kawiri, iwe udzandikana katatu.” Ndipo iye anasweka mtima nayamba kulira.
І заспівав півень хвилі тієї подруге. І згадав Петро слово, що Ісус був промовив йому: „Перше ніж заспіває півень дві́чі, — відречешся ти тричі від Мене“. І кинувся він, та й плакати став.

< Marko 14 >