< Marko 13 >

1 Iye atachoka mʼNyumba ya Mulungu, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Aphunzitsi taonani! Miyala ikuluikulu! Nyumba zikongolerenji!”
Yesu bho igenda kuh'omela ku lihekalu mmonga ghwa bhanafunzi bha muene akan'kota, “Mwalimu, langayi maganga agha gha kusyangasya ni majengo!”
2 Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuziona nyumba zikuluzikuluzi? Palibe mwala ndi umodzi pano umene udzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Akan'jobhela, ghwilola majengo agha mabhaha? Lijhelepi hata liganga limonga lyalibetakubakila panani pa lenge ambalyo libetakubinisibhwa pasi”.
3 Yesu atakhala pansi pa phiri la Olivi moyangʼanana ndi Nyumba ya Mulungu, Petro, Yakobo, Yohane ndi Andreya anamufunsa Iye pambali kuti,
Na muene bho atamili panani pa kidonda kya Mizeituni kunyuma ku lihekalu, Petro, Yakobo, Yohana ni Andrea bhakan'kota kwa siri,
4 “Tatiwuzani, izi zidzachitika liti? Nanga chizindikiro chakuti zatsala pangʼono kukwaniritsidwa chidzakhala chiyani?”
Tujobhilayi, mambo agha ghibeta kujha ndali? Na kiki dalili gha mambo agha kuh'omela?”
5 Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani kuti wina asakunyengeni.
Yesu akajhanda kubhajobhela, “Mujhiajhi makini kwamba asihidi munu kubhapotosya.
6 Anthu ambiri adzabwera mʼdzina langa, nadzati, ‘Ine ndi Iyeyo,’ ndipo adzanamiza anthu ambiri.
Bhingi bhibeta kuhida kwa lihina lya nene bhibeta kujobha, 'Nene ndiye', na bhibetakubhapotosya bhingi.
7 Pamene mudzamva zankhondo ndi mbiri zankhondo, musadzadzidzimuke. Zinthu zotere ziyenera kuchitika, koma sikuti chimaliziro chafika kale ayi.
Pa mwibeta kup'eleka vita ni tetesi sya vita, musitili; mambo agha ghilondeka kuh'omela lakini mwisho bado.
8 Mtundu udzawukira mtundu unzake, ndi ufumu kuwukira ufumu unzake. Kudzakhala zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana, ndi njala. Izi ndi chiyambi chabe cha zowawa monga mayi pobereka.
Taifa libeta kujhinuka kinyume ni litaifa l'enge, ni bhufalme kinyume ni bhufalme. Pibeta kujha ni matetemeku sehemu mbalimbali ni njala. Obho ndo mwanzo ghwa bhutungu.
9 “Muyenera kukhala tcheru. Mudzaperekedwa ku mabwalo oweruza ndi kukwapulidwa mwankhanza mʼmasunagoge. Mudzayima pamaso pa abwanamkubwa ndi mafumu monga mboni kwa iwo chifukwa cha Ine.
Mujhelayi mihu. Bhibetakubhapeleka mpaka mabarazani, na mwibetakupingibhwa mu masinagogi. Mwibetakujhemikibhwa mbele jha bhatawala ni bhafalme kwa ndabha jha nene, kama bhushuhuda bhwa bhene.
10 Ndipo Uthenga Wabwino uyenera kuyamba walalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.
Lakini injili lazima hoti ihubiribhwayi kwa mataifa ghoha.
11 Nthawi iliyonse pamene mwamangidwa ndi kuyimbidwa mlandu, musadandaule za zimene mudzanena. Zimene mudzapatsidwe pa nthawiyo yankhulani; pakuti sindinu amene mudzayankhula, koma Mzimu Woyera.
Pabhibeta kubhakamula ni kubhakabidhi, musitili kuhusu khela kya mwibeta kujobha. Ndani jha muda obhu, mwibetakupelibhwa kiki kya kujobha; Mwibeta lepi kujha muenga mwilongila, bali Roho mtakatifu.
12 “Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe, ndipo abambo adzapereka mwana wawo. Ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe.
Ndugu ibetakun'shtaki ndugu kukomibhwa, Dadi ni mwana munu. Bhana bhibeta kujhama kinyume ni Dadi jhabhi ni kusababisya kukomibhwa.
13 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine, koma amene adzalimbika mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.
Mwibetakudadibhwa ni khila munu kwa ndabha jha lihina lya nene. Lakini jha ibetakuvumilila mpaka kumuisu, munu ojhu ibeta kuokoka.
14 “Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri.
Pamwibetakubhona lichukizo lya bhuharibifu lijhemili pala palilondeka lepi kujhema (jhaisoma na amanyayi), ndipo bhabhajhele mugati mwa Yuda bhajumbililayi kukidonda,
15 Aliyense amene ali pa denga la nyumba yake asatsike kapena kulowa mʼnyumba kukatenga kanthu kalikonse.
nu muene jha ajhele kunani pa nyumba asiseleli pasi pa nyumba, au kutola kyokyoha kyekijhele kwibhala,
16 Aliyense amene ali ku munda asabwerere kukatenga mkanjo wake.
na jhaajhele kun'gonda asikerebhuki kulota liguanda lya muene.
17 Kudzakhala koopsa mʼmasiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa!
Lakini ole bhabhi bhadala bha bhajhele ni luleme ni bhabhijhong'esya mu magono aghu!
18 Pempherani kuti zimenezi zisadzachitike nthawi yozizira,
Mus'omelayi kujha jhisih'omeli wakati bhwa mepu.
19 chifukwa masiku amenewo adzakhala owawitsa osafanana ndi ena kuyambira pachiyambi, pamene Mulungu analenga dziko, kufikira lero ndipo sadzafanananso ndi ena.
Kwani pibeta kujha ni malombosi mabhaha, ambagho ghabhwayilepi kuh'omela, kuhomela K'yara abhubhombili bhulimwengu, mpaka henu, ijhelepi, wala jhibetalepi kuh'omela kabhele.
20 Ambuye akanapanda kufupikitsa masikuwo, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwiratu, amene anawasankha, Iye anawafupikitsa.
Mpaka Bwana paibetakup'ongosya magono, ghujhelepi mb'ele ghwa ghwibeta kuokoka, lakini kwa ndabha jha bhateule, jhaibeta kubhahagula, ibetakup'ongosya namba sya magono.
21 Pa nthawi imeneyo, ngati wina adzati kwa inu, ‘Taonani, Khristu ali kuno, kapena, Taonani, uyo ali apoyo!’ musakhulupirire.
Wakati obhu kama munu jhejhioha ibetakubhajobhela, langai, Kristu ajhele apa!' au 'Langai, ajhe pala!' musiamini.
22 Pakuti akhristu onama ndi aneneri onama adzaonekera ndipo adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa kuti anyenge osankhidwiratu ngati kutakhala kotheka kutero.
Kwani bhakristu bha bhudesi ni manabii bha bhudesi bhibeta kuh'omela ni kulasya ishara ni maajabu ili kwamba, bhabhakofiajhi, yamkini hata bhateule.
23 Choncho khalani tcheru; ndakuwuzani zonse nthawi isanafike.
Mujhiaji mihu! Nimelikubhajobhela agha ghoha kabla jha bhwakati.
24 “Koma masiku amenewo, masautsowo atatha, “‘dzuwa lidzada, ndipo mwezi sudzawala;
Lakini baada jha mal'ombosi gha magono aghu, lijobha libeta kus'opibhwa ngisi, muesi ghwibeta lepi kupisya mwanga ghwake,
25 nyenyezi zidzagwa kuchokera ku thambo, ndipo mayiko mumlengalenga adzagwedezeka!’
Matondo ghibeta kubina kuh'omela kunani ni nghofu syasijhele kumbinguni sibetakutikisika.
26 “Nthawi imeneyo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera mʼmitambo ndi mphamvu yayikulu ndi ulemerero.
Ndipo pabhibeta kumbona mwana ghwa Adamu ihida mumabhengu kwa nghofu mbaha ni bhutukufu.
27 Ndipo adzatuma angelo ake kukasonkhanitsa osankhidwiratu ake ku mphepo zinayi, kuyambira kumalekezero a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso.
Ndipo paibeta kutuma malaika bha muene na ibeta kubhabhonganya pamonga bhateule bha muene kuh'omela pande mbaha nne sya dunia, kuh'omela mwisho ghwa dunia mpaka mwisho ghwa mbingu.
28 “Tsopano phunzirani phunziro ili kuchokera ku mtengo wamkuyu. Pamene msonga za nthambi zake zikhala za nthete ndipo masamba ake ayamba kuphukira, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
Kwa mtini mwikimanyisijhi. Kama tawi kyalibhwesya kupisya ni kubheka haraka mat'ondo ghake, ndipo mwibeta kumanya kujha kilolelu kijhe karibu.
29 Momwenso pamene muona zinthu izi zikuchitika, dziwani kuti wayandikira, ali pa khomo.
Ndo kyajhijhele pamwibetakubhona mambo agha ghih'omela, mumanyayi kujha ajhele karibu, ni malango.
30 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
Bhokweli, nikabhajobhela, kizazi ekhe kibetap'etalepi patali kabla mambo agha ghah'omili lepi.
31 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Mbingu ni nchi sibeta kup'eta, lakini malobhi ghangu ghibeta lepi kup'eta kamwe.
32 “Palibe amene akudziwa za tsikulo kapena nthawi, ngakhale angelo akumwamba, kapena Mwana, koma Atate wokha.
Lakini kuhusu ligono elu au saa ajhelepi jha ibeta kumanya, hata malaika bha kumbinguni, wala mwana, ila Dadi.
33 Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike.
Mujhelayi mihu Langayi, kwa ndabha mumanyilepi ni muda bholoki ghibeta kuh'omela. (zingatilayi: N'sitari obho, “Mujhelayi bhaangalifu, mulangayi na mus'okayi kwa ndabha...” bhujhelepi mu nakala sya muandi).
34 Zili ngati munthu amene akuchokapo. Amasiyira nyumba yake antchito ake, aliyense ndi ntchito yake; ndi kumuwuza wa pa khomo kuti azikhala maso.
Ni kama munu jhailota ku safuari: alekili nyumba jha muene, ni kumbeka n'tumwa ghwa muene kujha ntawala ghwa nyumba, khila mmonga ni mbombo jha muene. Ni kumwamuru mlinzi kutama mihu.
35 “Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha.
Henu mujhelayi mihu! kwani mumanyilepi bwana ghwa nyumba pa ibeta kubhujhe kunyumba, jhibhwesekana kimihi kilukya manane, wakati likongobha palibeta kubheka, au lukhela.
36 Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo.
Kama ahidili ghafla, asikukoleli ugonili.
37 Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’”
Khela kyanikakijobha kwa bhebhe, nikakijobha kwa kila munu: Mukeshayi”!

< Marko 13 >