< Marko 13 >

1 Iye atachoka mʼNyumba ya Mulungu, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Aphunzitsi taonani! Miyala ikuluikulu! Nyumba zikongolerenji!”
uYesu nai wakatula ukugenda kupuma mi itekeelo, ung'wi nua amanysigwa akwe akamukolya, “Ng'walimu, goza i magwe aya ni aku kuilwa ni mazumba!”
2 Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuziona nyumba zikuluzikuluzi? Palibe mwala ndi umodzi pano umene udzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Akamutambuila, Ukihenga i mazumba aya ni makulu? Kutili ga nigwe ni ling'wi nilika sagiila migulya a lingiiza ni shanga aza likugwa pihi.”
3 Yesu atakhala pansi pa phiri la Olivi moyangʼanana ndi Nyumba ya Mulungu, Petro, Yakobo, Yohane ndi Andreya anamufunsa Iye pambali kuti,
Nu ng'wenso nai wakatula wikie migulya a lugulu nula mizeituni kituli ki itekeelo, uPetro, Yakobo, Yohana nu Andrea akamukolya ku kinkunku.
4 “Tatiwuzani, izi zidzachitika liti? Nanga chizindikiro chakuti zatsala pangʼono kukwaniritsidwa chidzakhala chiyani?”
“Kuile, i makani aya akutula nali? Ingi ntuni i kilingasiilyo nika makani aya kupumila?”
5 Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani kuti wina asakunyengeni.
uYsu ai wandilye kuatambuila, “Tuli miakendegeeli kina mntu wihi waleke kumulimilya.
6 Anthu ambiri adzabwera mʼdzina langa, nadzati, ‘Ine ndi Iyeyo,’ ndipo adzanamiza anthu ambiri.
Idu ikapembya ku lina nilane azeligitya 'Unene ng'wenso,' hangi akualimilya idu.
7 Pamene mudzamva zankhondo ndi mbiri zankhondo, musadzadzidzimuke. Zinthu zotere ziyenera kuchitika, koma sikuti chimaliziro chafika kale ayi.
Ni mikija ulugu nu pwepwe nua uligu, leki kitumbi; makani aya atakiwe kupumila, kuiti i mpelo ikili.
8 Mtundu udzawukira mtundu unzake, ndi ufumu kuwukira ufumu unzake. Kudzakhala zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana, ndi njala. Izi ndi chiyambi chabe cha zowawa monga mayi pobereka.
Ihi likunyansuka kikua ni ihi lingiiza, nu utemi nsuta nu utemi. Yikatula ni matetemeko nkika nia kuli ni kuli, hangi nzala. Uwu ingi ng'wandyo nua uwai.
9 “Muyenera kukhala tcheru. Mudzaperekedwa ku mabwalo oweruza ndi kukwapulidwa mwankhanza mʼmasunagoge. Mudzayima pamaso pa abwanamkubwa ndi mafumu monga mboni kwa iwo chifukwa cha Ine.
Tuli miho. Akumutwala kupikiila mu maanza, hagi mukukuwa mu matekeelo. Mukimikigwa ntongeela a ahumi ni atemi ku nsoko ane, anga ukuiili kitalao.
10 Ndipo Uthenga Wabwino uyenera kuyamba walalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.
Kuiti i nkani ninza kusinja hanza itanantigwe ku anyaingu ihi.
11 Nthawi iliyonse pamene mwamangidwa ndi kuyimbidwa mlandu, musadandaule za zimene mudzanena. Zimene mudzapatsidwe pa nthawiyo yankhulani; pakuti sindinu amene mudzayankhula, koma Mzimu Woyera.
Ni ikatula amuamba nu kuinkiilya, leki kitumbi kutula iko nimukaligitya. Mukati itungo nilanso, mukinkiiligwa ntuni nika kuligitya; shanga mikatula nyenye ni mikaligitya, ila Ng'wau Ng'welu.
12 “Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe, ndipo abambo adzapereka mwana wawo. Ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe.
Munyandugu ukumusemela u muluna kubulagwa, u tata nu ng'wana nuakwe. iAna akimika nsuta a atata ao hangi kuasasha kubulagwa.
13 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine, koma amene adzalimbika mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.
Mukutakiilwa ni kila u muntu ku nsoko a lina nilane. Kuiti nuikagimya kupikiila i mpelo, muntu nuanso ukugunika.
14 “Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri.
Ni mikihenga utaki nua ubipigwa wimikile pang'wanso ni shanga utakiwe kimika (nukusoma nua linge), papo niamoli mu Yuda amankiile mu malugulu,
15 Aliyense amene ali pa denga la nyumba yake asatsike kapena kulowa mʼnyumba kukatenga kanthu kalikonse.
nu ng'wenso nukoli migulya i ito nualeke kusima pihi ito, ang'wi kuhola kihi nikikoli kunzi,
16 Aliyense amene ali ku munda asabwerere kukatenga mkanjo wake.
hangi nukoli mu mugunda waleke kusuka kuhola u ng'wenda nuakwe.
17 Kudzakhala koopsa mʼmasiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa!
Kuiti ukia awo i asungu niakete inda nawa niakonsha mu mahiku nanso!
18 Pempherani kuti zimenezi zisadzachitike nthawi yozizira,
Lompi kina ileke kupumila itungo nila ulyuuku.
19 chifukwa masiku amenewo adzakhala owawitsa osafanana ndi ena kuyambira pachiyambi, pamene Mulungu analenga dziko, kufikira lero ndipo sadzafanananso ndi ena.
Kuiti yikatula nu lwago lukulu, naiza lukilikaya kupumila, puma Itunda nai u umbile u unkumbigulu, kupikiila itungili, ishi, ang'wi shanga ikapumila hangi.
20 Ambuye akanapanda kufupikitsa masikuwo, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwiratu, amene anawasankha, Iye anawafupikitsa.
Kupikiila u Mukulu nuikakepya i mahiku. Kutili u muili nuikagunika, kuiti ku nsoko a asagulwa, nuika asagula, wikakepya i namba nia mahiku.
21 Pa nthawi imeneyo, ngati wina adzati kwa inu, ‘Taonani, Khristu ali kuno, kapena, Taonani, uyo ali apoyo!’ musakhulupirire.
Matungo nanso anga ize muntu wihi wika mutambuila, 'Goza, uKristo ukoli apa!' ang'wi 'Goza, ukoli apo!' leki kuhuiili.
22 Pakuti akhristu onama ndi aneneri onama adzaonekera ndipo adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa kuti anyenge osankhidwiratu ngati kutakhala kotheka kutero.
Kuiti iAkristo nia uteele ni anyakidagu nia uteele akupumila hangi akupumya ilingasiilyo nu ukuilwa, iti kina, amukongele, nsigile ga ni asagulwa.
23 Choncho khalani tcheru; ndakuwuzani zonse nthawi isanafike.
Tuli miho! Nakondyaa mutambuila aya ze akili i matungo.
24 “Koma masiku amenewo, masautsowo atatha, “‘dzuwa lidzada, ndipo mwezi sudzawala;
Kuiyi ze yakilaa u lwago nula mahiku nanso, i lyoa likuikilwa kiti, u ng'weli shanga ukupumya u welu nuakwe,
25 nyenyezi zidzagwa kuchokera ku thambo, ndipo mayiko mumlengalenga adzagwedezeka!’
i nzota yukugwa kupuma kilunde, ni ingulu ni ikoli kilunde yukuhingiika.
26 “Nthawi imeneyo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera mʼmitambo ndi mphamvu yayikulu ndi ulemerero.
Papo ni ikamihenga u Ng'wana wang'wa Adamu upembilye mu malunde ku ngulu nkulu ni ikulyo.
27 Ndipo adzatuma angelo ake kukasonkhanitsa osankhidwiratu ake ku mphepo zinayi, kuyambira kumalekezero a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso.
Papo ukulagiilya i amalaika akwe hagi ukuilingiila palung'wi i asagulwa akwe kupuma nkika inne ni yihi, kupuma i mpelo nui ihi kupikiila i mpelo ilunde.
28 “Tsopano phunzirani phunziro ili kuchokera ku mtengo wamkuyu. Pamene msonga za nthambi zake zikhala za nthete ndipo masamba ake ayamba kuphukira, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
Ku mutini imanyisi. Anga itambi nili humile kupumya nu kuika u ukende mu matutu akwe, papo mukulinga kina i kipasu kikoli pakupi.
29 Momwenso pamene muona zinthu izi zikuchitika, dziwani kuti wayandikira, ali pa khomo.
Uu gwa yili, nimikihenga i makani aya anga apumile, lingi kina ukoli pakupi, ni mimpita.
30 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
Tai, kumuili, uwu u ulelwa shanga ukukila kuli ze akili imakani aya kupumila.
31 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Ilunde ni ihi yukukila, kuiti imakani ane shanga akukila lukulu. Kuiti kutula luhiku nulanso ang'wi saa,
32 “Palibe amene akudziwa za tsikulo kapena nthawi, ngakhale angelo akumwamba, kapena Mwana, koma Atate wokha.
kutili nulingile, ga nia malaika nia kilunde, ang'wi Ng'wana, ila Tata.
33 Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike.
Tuli miho, Gozi, ku nsoko shanga mulingile ingi itungo kii akupumila. (Komaniilya; U lukiili ulu, “Mutule miakendegeeli, Gozeeli hangi lompi ku nsoko .....” umutili mu mbugulu nia kali).
34 Zili ngati munthu amene akuchokapo. Amasiyira nyumba yake antchito ake, aliyense ndi ntchito yake; ndi kumuwuza wa pa khomo kuti azikhala maso.
Ingi anga umuntu nulongoe muhinzo; wakaleka ito nilakwe, nu kumuika u mutuung'wa nuakwe kutula muhumi nu ito, kila ung'wi nu mulimo nuakwe. Nu kumulagiilya u musunja kikie miho.
35 “Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha.
Ku lulo tuli miho! Kuiti shanga mulingile ingi nali u mukulu nu ito nuikagomoka ki ito, ihumikile ingi mpindi, utiku nuigingu, itungo nila nsambaligugu ni ikakunkula, ang'wi kidau dau.
36 Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo.
Anga waze kupumpugiilya, waleke kuhanga ulae.
37 Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’”
Iko ni kukiligitya ku kila u muntu; Huguki!”

< Marko 13 >