< Marko 12 >
1 Kenaka Iye anayamba kuyankhula nawo mʼmafanizo: “Munthu wina analima munda wamphesa. Anamanga mpanda mozungulira, nakumba dzenje lofinyiramo mphesa ndipo anamanga nsanja. Anawubwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita ku dziko lina.
Og han begyndte at tale til dem i Lignelser: "En Mand plantede en Vingård og satte et Gærde derom og gravede en Perse og byggede et Tårn, og han lejede den ud til Vingårdsmænd og drog udenlands.
2 Pa nthawi yokolola anatumiza wantchito kwa alimiwo kuti akatenge kuchokera kwa iwo zina mwa zipatso za munda wamphesa.
Og da Tiden kom, sendte han en Tjener til Vingårdsmændene, for at han af Vingårdsmændene kunde få af Vingårdens Frugter.
3 Koma iwo anamugwira, namumenya ndi kumupirikitsa wopanda kanthu.
Og de grebe ham og sloge ham og sendte ham tomhændet bort.
4 Kenaka anatumizanso wantchito wina kwa iwo. Iwo anamumenya munthuyo pamutu ndipo anamuzunza mochititsa manyazi.
Og han sendte atter en anden Tjener til dem; og ham sloge de i Hovedet og vanærede.
5 Anatumizanso wina, ndipo iwo anamupha. Anatumizanso ena ambiri; ena a iwo anawamenya, ena anawapha.
Og han sendte en anden; og ham sloge de ihjel; og mange andre; nogle sloge de, og andre dræbte de.
6 “Munthu uja anatsala ndi mwana mmodzi, wamwamuna amene amamukonda. Pomaliza anamutumiza mwanayo nati, ‘Adzamuchitira ulemu mwana wanga.’
Endnu een havde han, en elsket Søn; ham sendte han til sidst til dem, idet han sagde: "De ville undse sig for min Søn."
7 “Koma alimi aja anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndi mlowamʼmalo. Tiyeni timuphe, ndipo cholowacho chidzakhala chathu.’
Men hine Vingårdsmænd sagde til hverandre: "Der er Arvingen; kommer lader os slå ham ihjel, så bliver Arven vor."
8 Ndipo anamutenga ndi kumupha, ndipo anamuponya kunja kwa munda wamphesa.
Og de grebe ham og sloge ham ihjel og kastede ham ud af Vingården.
9 “Kodi nanga mwini munda wamphesa adzachita chiyani? Iye adzabwera ndi kupha alimiwo nadzapereka munda wamphesawo kwa ena.
Hvad vil da Vingårdens Herre gøre? Han vil komme og ødelægge Vingårdsmændene og give Vingården til andre.
10 Kodi simunawerenge lemba lakuti: “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wakhala mwala wa pa ngodya.
Have I ikke også læst dette Skriftord: Den Sten, som Bygningsmændene forkastede, den er bleven til en Hovedhjørnesten?
11 Ambuye achita zimenezi, ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu?’”
Fra Herren er dette kommet, og det er underligt for vore Øjne."
12 Ndipo akulu a ansembe, aphunzitsi a malamulo ndi akuluakulu anafunafuna njira yoti amugwirire Iye chifukwa amadziwa kuti anayankhula fanizoli mowatsutsa iwo. Koma amaopa gulu la anthu; ndipo anamusiya napita.
Og de søgte at gribe ham, men de frygtede for Mængden; thi de forstode, at han sagde denne Lignelse imod dem; og de forlode ham og gik bort.
13 Pambuyo pake anatuma ena a Afarisi ndi Aherode kwa Yesu kuti adzamukole mawu ake.
Og de sendte nogle til ham af Farisæerne og af Herodianerne, for at de skulde fange ham i Ord.
14 Iwo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ife tikudziwa kuti Inu ndi munthu amene mumanena zoona. Inu simutengeka ndi anthu, chifukwa simusamala kuti ndi ndani; koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu molingana ndi choonadi. Kodi ndi koyenera kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?
Og de kom og sagde til ham: "Mester! vi vide, at du er sanddru og ikke bryder dig om nogen; thi du ser ikke på Menneskers Person, men lærer Guds Vej i Sandhed. Er det tilladt at give Kejseren Skat eller ej? Skulle vi give eller ikke give?"
15 Kodi ife tipereke msonkho kapena ayi?” Koma Yesu anadziwa chinyengo chawo. Iye anafunsa kuti, “Bwanji mukufuna kundipeza chifukwa? Bweretsani ndalama kuti ndiyione.”
Men da han så deres Hykleri, sagde han til dem: "Hvorfor friste I mig? Bringer mig en Denar", for at jeg kan se den."
16 Iwo anamubweretsera ndalama, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi nkhope iyi ndi ya ndani? Nanga malembawa ndi a ndani?” Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”
Men de bragte den. Og han siger til dem: "Hvis Billede og Overskrift er dette?" Men de sagde til ham: "Kejserens."
17 Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.” Ndipo anazizwa naye.
Og Jesus sagde til dem: "Giver Kejseren, hvad Kejserens er, og Gud, hvad Guds er." Og de undrede sig over ham.
18 Kenaka Asaduki, amene amati kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Iye ndi funso.
Og der kommer Saddukæere til ham, hvilke jo sige, at der ingen Opstandelse er, og de spurgte ham og sagde:
19 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
"Mester! Moses har foreskrevet os, at når nogens Broder dør og og efterlader, en Hustru og ikke efterlader noget Barn, da skal hans Broder tage hans Hustru og oprejse sin Broder Afkom.
20 Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyamba anakwatira namwalira wosabereka ana.
Der var syv Brødre; og den første tog en Hustru, og da han døde, efterlod han ikke Afkom.
21 Wachiwiri anakwatira mkazi wamasiyeyo, koma iye anamwalira wosabereka mwana. Zinali chimodzimodzi ndi wachitatu.
Og den anden tog hende og døde uden at efterlade Afkom, og den tredje ligeså.
22 Kunena zoona, palibe ndi mmodzi yemwe wa asanu ndi awiriwo anasiya ana. Pomaliza, mkaziyo anamwaliranso.
Og alle syv, de efterlode ikke Afkom. Sidst af dem alle døde og så Hustruen.
23 Pa kuuka kwa akufa, adzakhala mkazi wa yani pakuti anakwatiwa ndi onse asanu ndi awiri?”
I Opstandelsen, når de opstå, hvem af dem skal så have hende til Hustru? Thi de have alle syv haft hende til Hustru."
24 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi si pamenepa nanga pomwe mumalakwira chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu za Mulungu?
Jesus sagde til dem: "Er det ikke derfor, I fare vild, fordi I ikke kende Skrifterne, ej heller Guds Kraft?
25 Pamene akufa auka, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
Thi når de opstå fra de døde, da tage de hverken til Ægte eller bortgiftes, men de ere som Engle i Himlene.
26 Tsopano kunena zakuti akufa amauka, kodi simunawerenge mʼbuku la Mose, pa nkhani yachitsamba choyaka moto, mmene Mulungu anati kwa iye, ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?’
Men hvad de døde angår, at de oprejses, have I da ikke læst i Mose Bog i Stedet om Tornebusken, hvorledes Gud talede til ham og sagde: Jeg er Abrahams Gud og Isaks Gud og Jakobs Gud?
27 Iye si Mulungu wa anthu akufa, koma wa amoyo. Inu mwalakwitsa kwambiri!”
Han er ikke dødes, men levendes Gud; I fare meget vild."
28 Mmodzi wa aphunzitsi amalamulo anabwera namva iwo akukambirana motsutsana. Poona kuti Yesu anawapatsa yankho labwino, anamufunsa Iye kuti, “Mwa malamulo onse, kodi lopambana koposa ndi liti?”
Og en af de skriftkloge, som havde hørt deres Ordskifte og set, at han svarede dem godt, kom til ham og spurgte ham: "Hvilket Bud er det første af alle?"
29 Yesu anayankha kuti, “Lamulo loposa onse ndi ili: ‘Tamvani inu Aisraeli! Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi!
Jesus svarede: "Det første er: Hør Israel! Herren, vor Gud, Herren er een;
30 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse ndi mphamvu zako zonse.’
og du skal elske Herren, din Gud af hele dit Hjerte og af hele din Sjæl og af hele dit Sind og af hele din Styrke.
31 Lachiwiri ndi ili: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ Palibe lamulo lina loposa amenewa.”
Et andet er dette: Du skal elske din Næste som dig selv. Større end disse er intet andet Bud."
32 Munthuyo anayankha kuti, “Mwanena bwino Aphunzitsi. Mwalondola ponena kuti Mulungu ndi mmodzi ndipo palibe wina wofanana naye koma Iye yekha.
Og den skriftkloge sagde til ham: "Rigtigt, Mester, og med Sandhed har du sagt, at han er een, og der er ingen anden foruden ham.
33 Kumukonda Iye; ndi mtima wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini, ndi zopambana kuposa zopereka ndi nsembe zopsereza.”
Og at elske ham af hele sit Hjerte og af hele sin Forstand og af hele sin Styrke og at elske sin Næste som sig selv, det er mere end alle Brændofrene og Slagtofrene."
34 Yesu ataona kuti wayankha mwanzeru, anati kwa iye, “Iwe suli kutali ndi ufumu wa Mulungu.” Ndipo kuyambira pamenepo panalibe ndi mmodzi yemwe anayesa kumufunsanso.
Og da Jesus så, at han svarede forstandigt, sagde han til ham: "Du er ikke langt fra Guds Rige." Og ingen vovede mere at rette Spørgsmål til ham.
35 Yesu akuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amanena kuti, ‘Khristu ndi Mwana wa Davide?’
Og da Jesus lærte i Helligdommen, tog han til Orde og sagde: "Hvorledes sige de skriftkloge, at Kristus er Davids Søn?
36 Pajatu Davide mwini wake, poyankhula mwa Mzimu Woyera, ananena kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani pa dzanja langa lamanja kufikira nditayika adani anu pansi pa mapazi anu.’
David selv sagde ved den Helligånd: Herren sagde til min Herre: Sæt dig ved min, højre Hånd, indtil jeg får lagt dine Fjender som en Skammel for dine Fødder.
37 Davide mwini wake amutchula Iye, ‘Ambuye.’ Nanga angakhale bwanji mwana wake?” Gulu lalikulu la anthu linamvetsera ndi chisangalalo.
David selv kalder ham Herre; hvorledes er han da hans Søn?" Og den store Skare hørte ham gerne.
38 Pamene ankaphunzitsa, Yesu anati, “Samalani ndi aphunzitsi a malamulo. Amakonda kuyendayenda atavala mikanjo ikuluikulu ndi kumalonjeredwa mʼmisika.
Og han sagde i sin Undervisning: "Tager eder i Vare for de skriftkloge, som gerne ville gå i lange Klæder og lade sig hilse på Torvene
39 Ndipo amakhala pa mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malo aulemu pa maphwando.
og gerne ville have de fornemste Pladser i Synagogerne og sidde øverst til Bords ved Måltiderne;
40 Amawononga chuma cha akazi amasiye ndiponso amapemphera mapemphero aatali odzionetsera. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
de, som opæde Enkers Huse og på Skrømt bede længe, disse skulle få des hårdere Dom."
41 Yesu anakhala pansi moyangʼanana ndi pamene amaperekera zopereka ndipo amaona anthu akupereka ndalama zawo mʼthumba la Nyumba ya Mulungu. Anthu ambiri olemera anaponya ndalama zambiri.
Og han satte sig lige over for Tempelblokken og så, hvorledes Mængden lagde Penge i Blokken, og mange rige lagde meget deri.
42 Koma mkazi wamasiye, wosauka anabwera ndi kuyikamo tindalama tiwiri ta kopala, tongokwanira theka la ndalama.
Og der kom en fattig Enke og lagde to Skærve i, hvilket er en Hvid".
43 Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mayi wosauka wamasiyeyu waponya zambiri mʼthumbali kuposa ena onsewa.
Og han kaldte sine Disciple til sig og sagde til dem: "Sandelig, siger jeg eder, denne fattige Enke har lagt mere deri end alle de som lagde i Tempelblokken.
44 Iwo apereka molingana ndi chuma chawo; koma iye, mwaumphawi wake, wapereka zonse anali nazo ngakhale zoti akanagulira chakudya.”
Thi de lagde alle af deres Overflod; men hun lagde af sin Fattigdom alt det, hun havde, sin hele Ejendom."