< Marko 12 >

1 Kenaka Iye anayamba kuyankhula nawo mʼmafanizo: “Munthu wina analima munda wamphesa. Anamanga mpanda mozungulira, nakumba dzenje lofinyiramo mphesa ndipo anamanga nsanja. Anawubwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita ku dziko lina.
Začal pak vyprávět následující příběh: „Jeden člověk založil vinici. Obehnal ji plotem, postavil lis na víno a vystavěl hlídkovou věž. Potom vinici pronajal pachtýřům a sám odcestoval.
2 Pa nthawi yokolola anatumiza wantchito kwa alimiwo kuti akatenge kuchokera kwa iwo zina mwa zipatso za munda wamphesa.
Když přišla doba vinobraní, pověřil jednoho ze svých sluhů, aby od pachtýřů vybral podíl z úrody, který mu náležel.
3 Koma iwo anamugwira, namumenya ndi kumupirikitsa wopanda kanthu.
Ale pachtýři sluhu ztloukli a vyhodili s prázdnou.
4 Kenaka anatumizanso wantchito wina kwa iwo. Iwo anamumenya munthuyo pamutu ndipo anamuzunza mochititsa manyazi.
Majitel tam poslal jiného. Po něm začali házet kamení, těžce ho zranili na hlavě a vyhnali.
5 Anatumizanso wina, ndipo iwo anamupha. Anatumizanso ena ambiri; ena a iwo anawamenya, ena anawapha.
Poslal tam tedy dalšího a toho zabili. Tak majitel vinice postupně vyslal ještě několik svých lidí. Ke všem se chovali surově, některé ztloukli, jiné ubili.
6 “Munthu uja anatsala ndi mwana mmodzi, wamwamuna amene amamukonda. Pomaliza anamutumiza mwanayo nati, ‘Adzamuchitira ulemu mwana wanga.’
Nakonec tam vypravil svého jediného milovaného syna. Domníval se, že před ním přece jen budou mít respekt.
7 “Koma alimi aja anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndi mlowamʼmalo. Tiyeni timuphe, ndipo cholowacho chidzakhala chathu.’
Ale nájemci si řekli: ‚To je jediný dědic. Zabijme ho a vinice bude naše.‘
8 Ndipo anamutenga ndi kumupha, ndipo anamuponya kunja kwa munda wamphesa.
A tak se stalo. Syna zavraždili a tělo vyhodili z vinice ven.
9 “Kodi nanga mwini munda wamphesa adzachita chiyani? Iye adzabwera ndi kupha alimiwo nadzapereka munda wamphesawo kwa ena.
Co si myslíte, že udělá ten majitel, až přijde? Spravedlivě je odsoudí k smrti a vinici pronajme jiným.
10 Kodi simunawerenge lemba lakuti: “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wakhala mwala wa pa ngodya.
Vzpomeňte si, že v Bibli je psáno: ‚Kámen, kterým stavitelé opovrhli, se nakonec stal kamenem nejdůležitějším – svorníkem klenby.
11 Ambuye achita zimenezi, ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu?’”
Pán Bůh to tak učinil a my stojíme v údivu.‘“
12 Ndipo akulu a ansembe, aphunzitsi a malamulo ndi akuluakulu anafunafuna njira yoti amugwirire Iye chifukwa amadziwa kuti anayankhula fanizoli mowatsutsa iwo. Koma amaopa gulu la anthu; ndipo anamusiya napita.
Židovští vůdci pochopili, že ten příběh platil jim, že oni jsou těmi proradnými pachtýři. Rádi by byli Ježíše zatkli, ale báli se davu. Prozatím od toho museli upustit.
13 Pambuyo pake anatuma ena a Afarisi ndi Aherode kwa Yesu kuti adzamukole mawu ake.
Poslali však za ním několik farizejů a členů Herodovy strany, aby ho vyprovokovali k nějakému žalovatelnému výroku.
14 Iwo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ife tikudziwa kuti Inu ndi munthu amene mumanena zoona. Inu simutengeka ndi anthu, chifukwa simusamala kuti ndi ndani; koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu molingana ndi choonadi. Kodi ndi koyenera kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?
„Mistře, “oslovili ho úlisně, „víme, že pravda je ti nade všechno; ať se to komu líbí či nelíbí, učíš pravdě tak, jak ji znáš od Boha. Řekni nám: máme platit Římu daně, nebo nemáme?“
15 Kodi ife tipereke msonkho kapena ayi?” Koma Yesu anadziwa chinyengo chawo. Iye anafunsa kuti, “Bwanji mukufuna kundipeza chifukwa? Bweretsani ndalama kuti ndiyione.”
Ježíš však nastraženou past prohlédl. „Co to na mě zkoušíte, podejte mi peníz!“
16 Iwo anamubweretsera ndalama, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi nkhope iyi ndi ya ndani? Nanga malembawa ndi a ndani?” Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.”
Když mu ho podali, zeptal se: „Čí obraz a jméno je na té minci?“„Římského císaře, “řekli.
17 Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.” Ndipo anazizwa naye.
„Dávejte tedy císaři, co je císařovo, a co je Boží, dávejte Bohu.“Tak jim to zase nevyšlo.
18 Kenaka Asaduki, amene amati kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Iye ndi funso.
Potom přišli se záludnou otázkou příslušníci skupiny saducejů, kteří nevěřili ve vzkříšení z mrtvých.
19 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
Řekli: „Mistře, v Mojžíšově zákoně je psáno: Zemře-li ženatý muž a nezanechá po sobě žádného dědice, jeho svobodný bratr je povinen oženit se s vdovou a zplodit bratrovi potomka.
20 Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyamba anakwatira namwalira wosabereka ana.
Povíme ti příběh: Bylo sedm bratrů. Nejstarší se oženil, brzo však zemřel a nenechal po sobě žádných dětí.
21 Wachiwiri anakwatira mkazi wamasiyeyo, koma iye anamwalira wosabereka mwana. Zinali chimodzimodzi ndi wachitatu.
Druhý se oženil s vdovou, ale brzy zemřel bezdětný. Tak to stále pokračovalo, až zemřel i poslední. Nikdo z nich nezanechal dědice.
22 Kunena zoona, palibe ndi mmodzi yemwe wa asanu ndi awiriwo anasiya ana. Pomaliza, mkaziyo anamwaliranso.
Nakonec zemřela i ta žena.
23 Pa kuuka kwa akufa, adzakhala mkazi wa yani pakuti anakwatiwa ndi onse asanu ndi awiri?”
Naše otázka zní: Čí bude ta žena po vzkříšení? Vždyť ji mělo za manželku všech sedm.“
24 Yesu anawafunsa kuti, “Kodi si pamenepa nanga pomwe mumalakwira chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu za Mulungu?
Ježíš odpověděl: „Vaše chyba je v tom, že neznáte Bibli a nevěříte v Boží moc. Manželství je záležitostí pozemského života.
25 Pamene akufa auka, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
Až lidé vstanou z mrtvých, nebudou už mezi nimi tělesné svazky. Přetrvají jen svazky ducha.
26 Tsopano kunena zakuti akufa amauka, kodi simunawerenge mʼbuku la Mose, pa nkhani yachitsamba choyaka moto, mmene Mulungu anati kwa iye, ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?’
A o vzkříšení samotném vůbec nepochybujte. Cožpak jste nečetli o Mojžíšovi a hořícím keři? Jak se tam Bůh tehdy představil? ‚Já jsem Bůh Abrahámův, Bůh Izákův, Bůh Jákobův.‘Když o lidech zesnulých před mnoha staletími říká: ‚já JSEM jejich Bůh, ‘pak je jasné, že pro něj nikdy nepřestali existovat. Vidíte, jak jste vedle.“
27 Iye si Mulungu wa anthu akufa, koma wa amoyo. Inu mwalakwitsa kwambiri!”
28 Mmodzi wa aphunzitsi amalamulo anabwera namva iwo akukambirana motsutsana. Poona kuti Yesu anawapatsa yankho labwino, anamufunsa Iye kuti, “Mwa malamulo onse, kodi lopambana koposa ndi liti?”
Tyto rozhovory sledoval jeden z učitelů zákona. Zdálo se mu, že Ježíš odpovídá znamenitě. A tak mu předložil svůj problém: „Které přikázání je nejdůležitější?“
29 Yesu anayankha kuti, “Lamulo loposa onse ndi ili: ‘Tamvani inu Aisraeli! Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi!
Ježíš nezaváhal: „První přikázání zní takto: Slyš Izraeli, Pak Bůh je jediný Pán.
30 Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse ndi mphamvu zako zonse.’
Miluj ho z celého srdce, celou bytostí a ze všech sil.
31 Lachiwiri ndi ili: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ Palibe lamulo lina loposa amenewa.”
A to druhé: Miluj druhého člověka tak, jako miluješ sebe. Nejsou důležitější přikázání než tato.“
32 Munthuyo anayankha kuti, “Mwanena bwino Aphunzitsi. Mwalondola ponena kuti Mulungu ndi mmodzi ndipo palibe wina wofanana naye koma Iye yekha.
„Mistře, tys dobře vystihl to podstatné, “musel uznat tazatel. „Bůh je jen jeden a kromě něho není jiného.
33 Kumukonda Iye; ndi mtima wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini, ndi zopambana kuposa zopereka ndi nsembe zopsereza.”
Milovat ho z celého srdce, celým rozumem a vší silou své vůle a druhé lidi milovat jako sebe – to je víc než všechny oběti zvířat na oltáři.“
34 Yesu ataona kuti wayankha mwanzeru, anati kwa iye, “Iwe suli kutali ndi ufumu wa Mulungu.” Ndipo kuyambira pamenepo panalibe ndi mmodzi yemwe anayesa kumufunsanso.
„Ty nejsi daleko od Božího království, “ocenil jeho postoj Ježíš. Pak už se ho nikdo neodvážil na nic zeptat.
35 Yesu akuphunzitsa mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amanena kuti, ‘Khristu ndi Mwana wa Davide?’
Později, když Ježíš učil v chrámu, položil otázku: „Z čeho náboženští učitelé usuzují, že Kristus musí být potomkem krále Davida?
36 Pajatu Davide mwini wake, poyankhula mwa Mzimu Woyera, ananena kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani pa dzanja langa lamanja kufikira nditayika adani anu pansi pa mapazi anu.’
Vždyť sám David napsal, inspirován Duchem svatým: ‚Bůh řekl mému Pánu: Seď po mé pravici, dokud ti tvé nepřátele nepoložím k nohám.‘
37 Davide mwini wake amutchula Iye, ‘Ambuye.’ Nanga angakhale bwanji mwana wake?” Gulu lalikulu la anthu linamvetsera ndi chisangalalo.
Když ho David nazývá svým Pánem, jak by tedy mohl být Davidovým synem?“Ježíš měl vždycky mnoho pozorných posluchačů.
38 Pamene ankaphunzitsa, Yesu anati, “Samalani ndi aphunzitsi a malamulo. Amakonda kuyendayenda atavala mikanjo ikuluikulu ndi kumalonjeredwa mʼmisika.
Jednou je varoval: „Dejte si pozor na učitele, kteří se na veřejnosti procházejí v krásných šatech a čekají, že je lidé budou uctivě zdravit a klanět se jim.
39 Ndipo amakhala pa mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malo aulemu pa maphwando.
Rádi si zajišťují přední sedadla v modlitebnách a čestná místa na hostinách.
40 Amawononga chuma cha akazi amasiye ndiponso amapemphera mapemphero aatali odzionetsera. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”
Vyjídají vdovské domy tím, že si dávají platit za modlitby, které úmyslně protahují. Protože učí jiné a takhle se chovají, Bůh je potrestá tím přísněji.“
41 Yesu anakhala pansi moyangʼanana ndi pamene amaperekera zopereka ndipo amaona anthu akupereka ndalama zawo mʼthumba la Nyumba ya Mulungu. Anthu ambiri olemera anaponya ndalama zambiri.
Jednou si Ježíš sedl proti chrámové pokladně a pozoroval lidi. Mnozí bohatí tam vkládali značné částky peněz.
42 Koma mkazi wamasiye, wosauka anabwera ndi kuyikamo tindalama tiwiri ta kopala, tongokwanira theka la ndalama.
Přišla také jedna chudá vdova a do pokladny vhodila dvě drobné mince.
43 Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mayi wosauka wamasiyeyu waponya zambiri mʼthumbali kuposa ena onsewa.
Ježíš si zavolal své učedníky a řekl jim: „Poslyšte, ta chudá vdova vlastně dala víc než boháči.
44 Iwo apereka molingana ndi chuma chawo; koma iye, mwaumphawi wake, wapereka zonse anali nazo ngakhale zoti akanagulira chakudya.”
Ti dávali jen přebytky, bez kterých se snadno obejdou, ale ta žena dala všechno, co měla na živobytí.“

< Marko 12 >