< Marko 11 >
1 Atayandikira ku Yerusalemu, anafika ku Betifage ndi Betaniya ku phiri la Olivi. Yesu anatuma awiri a ophunzira ake
Og da de nærme sig Jerusalem til Bethfage og Betania ved Oliebjerget, udsender han to af sine Disciple og siger til dem:
2 nati kwa iwo, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukamakalowa, mukapeza mwana wabulu atamangiriridwa pamenepo, amene wina aliyense sanakwerepo. Kamumasuleni ndi kubwera naye kuno.
"Går hen til den Landsby, som ligger lige for eder, og straks, når I komme ind i den, skulle I finde et Føl bundet, på hvilket der endnu aldrig har siddet noget Menneske; løser det og fører det hid!
3 Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Mukuchita zimenezi chifukwa chiyani?’ Kamuwuzeni kuti, ‘Ambuye akumufuna ndipo akamutumiza kuno msanga.’”
Og dersom nogen siger til eder: Hvorfor gøre I dette? da siger: Herren har Brug for det, og han sender det straks herhen igen."
4 Anapita ndipo anakapeza mwana wabulu ali kunja mu msewu waukulu atamumangirira pa chipata. Pamene anamumasula,
Og de gik hen og fandt Føllet bundet ved Døren udenfor ved Gyden, og de løse det.
5 anthu ena amene anayima pomwepo anafunsa kuti, “Mukuchita chiyani, kumasula mwana wabuluyo?”
Og nogle af dem, som stode der, sagde til dem: "Hvad gøre I, at I løse Føllet?"
6 Iwo anayankha monga mmene Yesu anawawuzira, ndipo anthu aja anawalola kuti apite.
Men de sagde til dem, ligesom Jesus havde sagt, og de tilstedte dem det.
7 Atafika naye mwana wabulu kwa Yesu, nayika mikanjo yawo pa buluyo, Iye anakwerapo.
Og de føre Føllet til Jesus og lægge deres Klæder på det, og han satte sig på det.
8 Anthu ambiri anayala mikanjo yawo pa msewu, pamene ena anayala nthambi zomwe anadula mʼminda.
Og mange bredte deres Klæder på Vejen, andre Kviste, som de afskare på Markerne.
9 Amene anatsogola ndi iwo amene ankatsatira ankafuwula kuti, “Hosana! “Odala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye!”
Og de, som gik foran, og de, som fulgte efter, råbte: "Hosanna! velsignet være den, som kommer, i Herrens Navn!
10 “Odala ndi ufumu umene ukubwera wa abambo athu Davide!” “Hosana Mmwambamwamba!”
Velsignet være vor Fader Davids Rige, som kommer, Hosanna i det højeste!"
11 Yesu analowa mu Yerusalemu napita ku Nyumba ya Mulungu. Anayangʼana zonse, koma popeza kuti nthawi inali itapita, anatuluka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
Og han gik ind i Jerusalem, i Helligdommen, og da han havde beset alt, gik han, da det allerede var Aftenstid, ud til Bethania med de tolv.
12 Mmawa mwake pamene amachoka ku Betaniya, Yesu anamva njala.
Og den følgende Dag; da de gik ud fra Bethania, blev han hungrig.
13 Ataonera patali mtengo wamkuyu uli ndi masamba, anapita kuti akaone ngati unali ndi chipatso chilichonse. Atafika, sanapezemo kanthu koma masamba, chifukwa sinali nthawi ya nkhuyu.
Og da han så et Figentræ langt borte, som havde Blade, gik han derhen, om han måske kunde finde noget derpå, og da han kom til det, fandt han intet uden Blade; thi det var ikke Figentid.
14 Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi. (aiōn )
Og han tog til Orde og sagde til det: "Aldrig i Evighed skal nogen mere spise Frugt af dig!" Og hans Disciple hørte det. (aiōn )
15 Atafika ku Yerusalemu, Yesu analowa mʼbwalo lakunja la Nyumba ya Mulungu ndipo anayamba kupirikitsa anthu amene amagula ndi kugulitsa mʼmenemo. Anagubuduza matebulo a osintha ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda,
Og de komme til Jerusalem; og han gik ind i Helligdommen og begyndte at uddrive dem, som solgte og købte i Helligdommen, og han væltede Vekselerernes Borde og Duekræmmernes Stole.
16 ndipo Iye sanalole aliyense kugulitsa malonda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu.
Og han tilstedte ikke, at nogen bar nogen Ting igennem Helligdommen.
17 Ndipo pamene ankawaphunzitsa, Iye anati, “Kodi sikunalembedwe kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero kwa anthu a mitundu yonse?’ Koma inu mwayisandutsa ‘phanga la achifwamba.’”
Og han lærte og sagde til dem: "Er der ikke skrevet, at mit Hus skal kaldes et Bedehus for alle Folkeslagene? Men I have gjort det til en Røverkule."
18 Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamva izi ndipo anayamba kufuna njira yoti amuphere Iye, pakuti amamuopa, chifukwa gulu lonse la anthu linazizwa ndi chiphunzitso chake.
Og Ypperstepræsterne og de skriftkloge hørte det, og de søgte, hvorledes de kunde slå ham ihjel; thi de frygtede for ham, eftersom hele Skaren blev slagen af, Forundring over hans Lære.
19 Pofika madzulo, iwo anatuluka mu mzindamo.
Og da det blev Aften, gik han uden for Staden.
20 Mmamawa, pamene ankayenda, anaona mtengo wamkuyu uja utafota kuyambira ku mizu.
Og da de om Morgenen gik forbi, så de, at Figentræet var visnet fra Roden af.
21 Petro anakumbukira nati kwa Yesu, “Aphunzitsi, taonani! Mtengo wamkuyu munawutemberera uja wafota!”
Og Peter kom det i Hu og siger til ham; "Rabbi! se, Figentræet, som du forbandede, er visnet."
22 Yesu anayankha kuti, “Khalani ndi chikhulupiriro mwa Mulungu.
Og Jesus svarede og siger til dem: "Haver Tro til Gud!
23 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati wina aliyense angalamule phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye mʼnyanja,’ ndipo wosakayika mu mtima mwake koma kukhulupirira kuti chimene akunena chidzachitika, chidzachitikadi kwa iyeyo.
Sandelig, siger jeg eder, den, som siger til dette Bjerg: Løft dig op og; kast dig i Havet, og ikke tvivler i sit Hjerte, men tror, at det sker, som han siger, ham skal det ske.
24 Nʼchifukwa chake ndikukuwuzani kuti chilichonse chimene mupempha mʼpemphero, khulupirirani kuti mwalandira, ndipo chidzakhala chanu.
Derfor siger jeg eder: Alt, hvad I bede om og begære, tror, at I have fået det, så skal det ske eder.
25 Pamene muyimirira kupemphera, ngati muli ndi chifukwa ndi wina, mukhululukireni, kuti Atate anu akumwamba akukhululukireni machimo anu.”
Og når I stå og bede, da forlader, dersom I have noget imod nogen, for at også eders Fader, som er i Himlene, må forlade eder eders Overtrædelser.
26 (Koma ngati simukhululukirana, ngakhale Atate anu akumwamba sadzakhululukira machimo anu).
Men dersom I ikke forlade, skal eders Fader, som er i Himlene, ej heller forlade eders Overtrædelser"
27 Iwo anafikanso ku Yerusalemu, ndipo pamene Yesu amayenda mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
Og de komme atter til Jerusalem; og medens han gik omkring i Helligdommen, komme Ypperstepræsterne og de skriftkloge og de Ældste hen til ham.
28 Iwo anafunsa kuti, “Mukuchita izi ndi ulamuliro wanji? Ndipo anakupatsani ulamuliro umenewu ndi ndani?”
Og de sagde til ham: "Af hvad Magt gør du disse Ting? eller hvem har givet dig denne Magt til at gøre disse Ting?"
29 Yesu anayankha kuti, “Ndikufunsani funso limodzi. Mundiyankhe, ndipo ndikuwuzani ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira izi.
Men Jesus sagde til dem: "Jeg vil spørge eder om een Ting, og svarer mig derpå, så vil jeg sige eder, af hvad Magt jeg gør disse Ting.
30 Ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena kwa anthu? Ndiwuzeni.”
Johannes's Dåb, var den fra Himmelen eller fra Mennesker? Svarer mig!"
31 Iwo anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Wochokera kumwamba,’ atifunsa kuti, ‘Nanga nʼchifukwa chiyani simunamukhulupirire?’
Og de tænkte ved sig selv og sagde: "Sige vi: Fra Himmelen, da vil han sige, hvorfor troede I ham da ikke?
32 Koma ife tikati, ‘Wochokera kwa anthu.’” (Amaopa anthu, pakuti aliyense amakhulupirira kuti Yohane analidi mneneri).
Men sige vi: Fra Mennesker" så frygtede de for Folket; thi alle holdt for, at Johannes virkelig var en Profet.
33 Ndipo anamuyankha Yesu kuti, “Sitikudziwa.” Yesu anati, “Nanenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji ndichitira zimenezi.”
Og de svare og sige til Jesus: "Vi vide det ikke." Og Jesus siger til dem: "Så siger jeg eder ikke heller, af hvad Magt jeg gør disse Ting."