< Marko 10 >

1 Ndipo Yesu anachoka pamalowo ndi kupita kudera la Yudeya ndi kutsidya la mtsinje wa Yorodani. Magulu a anthu anabweranso kwa Iye, ndipo monga mwachizolowezi chake anawaphunzitsa.
Soon on His feet once more, He enters the district of Judaea and crosses the Jordan: again the people flock to Him, and ere long, as was usual with Him, He was teaching them once more.
2 Afarisi ena anabwera kudzamuyesa pomufunsa kuti, “Kodi malamulo amalola kuti mwamuna asiye mkazi wake?”
Presently a party of Pharisees come to Him with the question--seeking to entrap Him, "May a man divorce his wife?"
3 Iye anayankha kuti, “Kodi Mose anakulamulani chiyani?”
"What rule did Moses lay down for you?" He answered.
4 Iwo anati, “Mose amaloleza mwamuna kulemba kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa mkazi.”
"Moses," they said, "permitted a man to draw up a written notice of divorce, and to send his wife away."
5 Yesu anayankha kuti, “Mose anakulemberani lamulo ili chifukwa chakuwuma kwa mitima yanu.
"It was in consideration of your stubborn hearts," said Jesus, "that Moses enacted this law for you;
6 Koma pachiyambi cha chilengedwe, Mulungu ‘analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.’
but from the beginning of the creation the rule was, 'Male and female did God make them.
7 ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake,
For this reason a man shall leave his father and his mother, and shall cling to his wife,
8 ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ Potero sali awirinso, koma mmodzi.
and the two shall be one'; so that they are two no longer, but 'one.'
9 Chifukwa chake chimene Mulungu wachilumikiza pamodzi, munthu wina asachilekanitse.”
What, therefore, God has joined together let not man separate."
10 Pamene analinso mʼnyumba, ophunzira anamufunsa Yesu za izi.
Indoors the disciples began questioning Jesus again on the same subject.
11 Iye anayankha kuti, “Aliyense amene aleka mkazi wake ndi kukakwatira wina achita chigololo kulakwira mkaziyo.
He replied, "Whoever divorces his wife and marries another woman, commits adultery against the first wife;
12 Ndipo akasiya mwamuna wake ndi kukakwatiwa ndi wina, achita chigololo.”
and if a woman puts away her husband and marries another man, she commits adultery."
13 Anthu anabweretsa ana kwa Yesu kuti awadalitse, koma ophunzira anawadzudzula.
One day people were bringing young children to Jesus for Him to touch them, but the disciples interfered.
14 Pamene Yesu anaona zimenezi anayipidwa. Anati kwa iwo, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse, pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa onga awa.
Jesus, however, on seeing this, was moved to indignation, and said to them, "Let the little children come to me: do not hinder them; for to those who are childlike the Kingdom of God belongs.
15 Ndikukuwuzani choonadi, aliyense amene sadzalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana sadzalowamo.”
In solemn truth I tell you that no one who does not receive the Kingdom of God like a little child will by any possibility enter it."
16 Ndipo ananyamula ana mʼmanja ake, ndi kuyika manja ake pa iwo nawadalitsa.
Then He took them in His arms and blessed them lovingly, one by one, laying His hands upon them.
17 Yesu atanyamuka, munthu wina anamuthamangira nagwa mogwada pamaso pake. Iye anafunsa kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
As He went out to resume His journey, there came a man running up to Him, who knelt at His feet and asked, "Good Rabbi, what am I to do in order to inherit the Life of the Ages?" (aiōnios g166)
18 Yesu anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukunditchula wabwino? Palibe wabwino koma Mulungu yekha.
"Why do you call me good?" asked Jesus in reply; "there is no one truly good except One--that is, God.
19 Iwe umadziwa malamulo: ‘Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni wonama, usachite chinyengo, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
You know the Commandments--'Do not murder;' 'Do not commit adultery;' 'Do not steal;' 'Do not lie in giving evidence;' 'Do not defraud;' 'Honour thy father and thy mother.'"
20 Iye anati, “Aphunzitsi zonsezi ndinazisunga kuyambira ndili mnyamata.”
"Rabbi," he replied, "all these Commandments I have carefully obeyed from my youth."
21 Yesu anamuyangʼana ndi kumukonda nati, “Ukusowa chinthu chimodzi. Pita, kagulitse zonse zimene uli nazo ndipo kapereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ndipo ukabwere ndi kunditsata Ine.”
Then Jesus looked at him and loved him, and said, "One thing is lacking in you: go, sell all you possess and give the proceeds to the poor, and you shall have riches in Heaven; and come and be a follower of mine."
22 Pa chifukwa ichi nkhope yake inagwa. Anachoka ali wachisoni, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
At these words his brow darkened, and he went away sad; for he was possessed of great wealth.
23 Yesu anayangʼanayangʼana ndipo anati kwa ophunzira ake, “Nʼkovutadi kuti achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!”
Then looking round on His disciples Jesus said, "With how hard a struggle will the possessors of riches enter the Kingdom of God!"
24 Ophunzira anadabwa ndi mawu ake. Koma Yesu anatinso, “Ananu, nʼkovutadi kulowa mu ufumu wakumwamba!
The disciples were amazed at His words. Jesus, however, said again, "Children, how hard a struggle is it for those who trust in riches to enter the Kingdom of God!
25 Ndi kwapafupi kwa ngamira kuti idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kuti alowe mu ufumu wa Mulungu.”
It is easier for a camel to go through the eye of a needle than for a rich man to enter the Kingdom of God."
26 Ophunzira anadabwa kwambiri, ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
They were astonished beyond measure, and said to one another, "Who then can be saved?"
27 Yesu anawayangʼana ndipo anati, “Kwa munthu zimenezi nʼzosatheka, koma osati ndi Mulungu; zinthu zonse zimatheka ndi Mulungu.”
Jesus looking on them said, "With men it is impossible, but not with God; for everything is possible with God."
28 Petro anati kwa Iye, “Ife tasiya zonse ndi kukutsatani!”
"Remember," said Peter to Him, "that we forsook everything and have become your followers."
29 Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti palibe aliyense amene wasiya nyumba kapena abale kapena alongo kapena amayi kapena abambo kapena ana kapena minda chifukwa cha Ine ndi Uthenga Wabwino
"In solemn truth I tell you," replied Jesus, "that there is no one who has forsaken house or brothers or sisters, or mother or father, or children or lands, for my sake and for the sake of the Good News,
30 adzalephera kulandira 100 (nyumba, abale, alongo, amayi, ana ndi minda, pamodzi ndi mazunzo) mʼbado uno ndi moyo wosatha nthawi ya mʼtsogolo. (aiōn g165, aiōnios g166)
but will receive a hundred times as much now in this present life--houses, brothers, sisters, mothers, children, lands--and persecution with them--and in the coming age the Life of the Ages. (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Koma ambiri amene ndi woyambirira adzakhala omalizira, ndipo omalizira adzakhala oyambirira.”
But many who are now first will be last, and the last, first."
32 Ali pa ulendo wawo wopita ku Yerusalemu, Yesu ali patsogolo, ophunzira ake anadabwa, ndipo amene amamutsatira amachita mantha. Anatenganso ophunzira ake khumi ndi awiri pa mbali ndipo anawawuza zimene zikamuchitikire Iye.
They were still on the road going up to Jerusalem, and Jesus was walking ahead of them; they were full of wonder, and some, though they followed, did so with fear. Then, once more calling to Him the Twelve, He began to tell them what was about to happen to Him.
33 Iye anati, “Ife tikupita ku Yerusalemu ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Adzamuweruza kuti aphedwe ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina,
"See," He said, "we are going up to Jerusalem, where the Son of Man will be betrayed to the High Priests and the Scribes. They will condemn Him to death, and will hand Him over to the Gentiles;
34 amene adzamuchita chipongwe ndi kumuthira malovu, kumukwapula ndi kumupha. Patatha masiku atatu adzauka.”
they will insult Him in cruel sport, spit on Him, scourge Him, and put Him to death; but on the third day He will rise to life again."
35 Ndipo Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anabwera kwa Iye ndipo anati, “Aphunzitsi, tikufuna kuti mutichitire ife chilichonse chimene tipemphe.”
Then James and John, the sons of Zabdi, came up to Him and said, "Rabbi, we wish you would grant us whatever request we make of you."
36 Iye anafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndikuchitireni chiyani?”
"What would you have me do for you?" He asked.
37 Iwo anayankha kuti, “Timafuna kuti mmodzi wa ife adzakhale kumanja ndi wina kumanzere mu ulemerero wanu.”
"Allow us," they replied, "to sit one at your right hand and the other at your left hand, in your glory."
38 Yesu anati, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungamwere chikho chimene ndidzamwera kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwe nawo?”
"You know not," said He, "what you are asking. Are you able to drink out of the cup from which I am to drink, or to be baptized with the baptism with which I am to be baptized?"
39 Iwo anayankha kuti, “Tikhoza.” Yesu anawawuza kuti, “Mudzamweradi chikho chimene Ine ndidzamwera, ndi kubatizidwa ndi ubatizo umene Ine ndidzabatizidwe nawo,
"We are able," they replied. "Out of the cup," said Jesus, "from which I am to drink you shall drink, and with the baptism with which I am to be baptized you shall be baptized;
40 koma kukhala kumanja kapena kumanzere si Ine wopereka. Malo awa ndi a amene anasankhidwiratu.”
but as to sitting at my right hand or at my left, that is not mine to give: it will be for those for whom it is reserved."
41 Ophunzira khumiwo otsalawo atamva izi anapsera mtima Yakobo ndi Yohane.
The other ten, hearing of it, were at first highly indignant with James and John.
42 Yesu anawayitana pamodzi nati, “Inu mukudziwa kuti iwo amene amadziyesa ngati atsogoleri a anthu amitundu ina amadyera anthu awo masuku pamutu. Akuluakulu awonso amaonetsadi mphamvu zawo pa iwo.
Jesus, however, called them to Him and said to them, "You are aware how those who are deemed rulers among the Gentiles lord it over them, and their great men make them feel their authority;
43 Sizili choncho ndi inu. Mʼmalo mwake, amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu ayenera kukhala wotumikira,
but it is not to be so among you. No, whoever desires to be great among you must be your servant;
44 ndipo aliyense amene akufuna kukhala wamkulu akhale kapolo wa onse.
and whoever desires to be first among you must be the bondservant of all.
45 Pakuti ngakhale Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kuti ukhale dipo la anthu ambiri.”
For the Son of Man also did not come to be waited upon, but to wait on others, and to give His life as the redemption-price for a multitude of people."
46 Ndipo anafika ku Yeriko. Pamene Yesu ndi ophunzira ake, pamodzi ndi gulu lalikulu la anthu, ankatuluka mu mzinda, munthu wosaona, Bartumeyu (mwana wa Tumeyu), amakhala mʼmbali mwa msewu ali kupempha.
They came to Jericho; and as He was leaving that town--Himself and His disciples and a great crowd--Bartimaeus (the son of Timaeus), a blind beggar, was sitting by the way-side.
47 Pamene anamva kuti anali Yesu wa ku Nazareti, anayamba kufuwula kuti, “Yesu, Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Hearing that it was Jesus the Nazarene, he began to cry out, "Son of David, Jesus, have pity on me."
48 Ambiri anamukalipira ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulitsabe kuti, “Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
Many angrily told him to leave off shouting; but he only cried out all the louder, "Son of David, have pity on me."
49 Yesu anayima nati, “Muyitaneni.” Ndipo anamuyitana kuti, “Kondwera! Imirira! Akukuyitana.”
Then Jesus stood still. "Call him," He said. So they called the blind man. "Cheer up," they said; "rise, he is calling you."
50 Anaponya mkanjo wake kumbali, analumpha nabwera kwa Yesu.
The man flung away his outer garment, sprang to his feet, and came to Jesus.
51 Yesu anamufunsa kuti, “Ukufuna ndikuchitire chiyani?” Wosaonayo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndikufuna ndione.”
"What shall I do for you?" said Jesus. "Rabboni," replied the blind man, "let me recover my sight."
52 Yesu anati, “Pita, chikhulupiriro chako chakuchiritsa!” Nthawi yomweyo anapenya, nʼkumatsatira Yesu pa ulendowo.
"Go," said Jesus, "your faith has cured you." Instantly he regained his sight, and followed Him along the road.

< Marko 10 >