< Marko 1 >

1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
īśvaraputrasya yīśukhrīṣṭasya susaṁvādārambhaḥ|
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
bhaviṣyadvādināṁ granthēṣu lipiritthamāstē, paśya svakīyadūtantu tavāgrē prēṣayāmyaham| gatvā tvadīyapanthānaṁ sa hi pariṣkariṣyati|
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
"paramēśasya panthānaṁ pariṣkuruta sarvvataḥ| tasya rājapathañcaiva samānaṁ kurutādhunā|" ityētat prāntarē vākyaṁ vadataḥ kasyacidravaḥ||
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
saēva yōhan prāntarē majjitavān tathā pāpamārjananimittaṁ manōvyāvarttakamajjanasya kathāñca pracāritavān|
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
tatō yihūdādēśayirūśālamnagaranivāsinaḥ sarvvē lōkā bahi rbhūtvā tasya samīpamāgatya svāni svāni pāpānyaṅgīkr̥tya yarddananadyāṁ tēna majjitā babhūvuḥ|
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
asya yōhanaḥ paridhēyāni kramēlakalōmajāni, tasya kaṭibandhanaṁ carmmajātam, tasya bhakṣyāṇi ca śūkakīṭā vanyamadhūni cāsan|
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
sa pracārayan kathayāñcakrē, ahaṁ namrībhūya yasya pādukābandhanaṁ mōcayitumapi na yōgyōsmi, tādr̥śō mattō gurutara ēkaḥ puruṣō matpaścādāgacchati|
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
ahaṁ yuṣmān jalē majjitavān kintu sa pavitra ātmāni saṁmajjayiṣyati|
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
aparañca tasminnēva kālē gālīlpradēśasya nāsaradgrāmād yīśurāgatya yōhanā yarddananadyāṁ majjitō'bhūt|
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
sa jalādutthitamātrō mēghadvāraṁ muktaṁ kapōtavat svasyōpari avarōhantamātmānañca dr̥ṣṭavān|
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
tvaṁ mama priyaḥ putrastvayyēva mamamahāsantōṣa iyamākāśīyā vāṇī babhūva|
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
tasmin kālē ātmā taṁ prāntaramadhyaṁ nināya|
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
atha sa catvāriṁśaddināni tasmin sthānē vanyapaśubhiḥ saha tiṣṭhan śaitānā parīkṣitaḥ; paścāt svargīyadūtāstaṁ siṣēvirē|
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
anantaraṁ yōhani bandhanālayē baddhē sati yīśu rgālīlpradēśamāgatya īśvararājyasya susaṁvādaṁ pracārayan kathayāmāsa,
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
kālaḥ sampūrṇa īśvararājyañca samīpamāgataṁ; atōhētō ryūyaṁ manāṁsi vyāvarttayadhvaṁ susaṁvādē ca viśvāsita|
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
tadanantaraṁ sa gālīlīyasamudrasya tīrē gacchan śimōn tasya bhrātā andriyanāmā ca imau dvau janau matsyadhāriṇau sāgaramadhyē jālaṁ prakṣipantau dr̥ṣṭvā tāvavadat,
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
yuvāṁ mama paścādāgacchataṁ, yuvāmahaṁ manuṣyadhāriṇau kariṣyāmi|
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
tatastau tatkṣaṇamēva jālāni parityajya tasya paścāt jagmatuḥ|
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
tataḥ paraṁ tatsthānāt kiñcid dūraṁ gatvā sa sivadīputrayākūb tadbhrātr̥yōhan ca imau naukāyāṁ jālānāṁ jīrṇamuddhārayantau dr̥ṣṭvā tāvāhūyat|
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
tatastau naukāyāṁ vētanabhugbhiḥ sahitaṁ svapitaraṁ vihāya tatpaścādīyatuḥ|
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
tataḥ paraṁ kapharnāhūmnāmakaṁ nagaramupasthāya sa viśrāmadivasē bhajanagrahaṁ praviśya samupadidēśa|
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
tasyōpadēśāllōkā āścaryyaṁ mēnirē yataḥ sōdhyāpakāiva nōpadiśan prabhāvavāniva prōpadidēśa|
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
aparañca tasmin bhajanagr̥hē apavitrabhūtēna grasta ēkō mānuṣa āsīt| sa cītśabdaṁ kr̥tvā kathayāñcakē
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
bhō nāsaratīya yīśō tvamasmān tyaja, tvayā sahāsmākaṁ kaḥ sambandhaḥ? tvaṁ kimasmān nāśayituṁ samāgataḥ? tvamīśvarasya pavitralōka ityahaṁ jānāmi|
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
tadā yīśustaṁ tarjayitvā jagāda tūṣṇīṁ bhava itō bahirbhava ca|
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
tataḥ sō'pavitrabhūtastaṁ sampīḍya atyucaiścītkr̥tya nirjagāma|
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
tēnaiva sarvvē camatkr̥tya parasparaṁ kathayāñcakrirē, ahō kimidaṁ? kīdr̥śō'yaṁ navya upadēśaḥ? anēna prabhāvēnāpavitrabhūtēṣvājñāpitēṣu tē tadājñānuvarttinō bhavanti|
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
tadā tasya yaśō gālīlaścaturdiksthasarvvadēśān vyāpnōt|
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
aparañca tē bhajanagr̥hād bahi rbhūtvā yākūbyōhanbhyāṁ saha śimōna āndriyasya ca nivēśanaṁ praviviśuḥ|
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
tadā pitarasya śvaśrūrjvarapīḍitā śayyāyāmāsta iti tē taṁ jhaṭiti vijñāpayāñcakruḥ|
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
tataḥ sa āgatya tasyā hastaṁ dhr̥tvā tāmudasthāpayat; tadaiva tāṁ jvarō'tyākṣīt tataḥ paraṁ sā tān siṣēvē|
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
athāstaṁ gatē ravau sandhyākālē sati lōkāstatsamīpaṁ sarvvān rōgiṇō bhūtadhr̥tāṁśca samāninyuḥ|
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
sarvvē nāgarikā lōkā dvāri saṁmilitāśca|
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
tataḥ sa nānāvidharōgiṇō bahūn manujānarōgiṇaścakāra tathā bahūn bhūtān tyājayāñcakāra tān bhūtān kimapi vākyaṁ vaktuṁ niṣiṣēdha ca yatōhētōstē tamajānan|
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
aparañca sō'tipratyūṣē vastutastu rātriśēṣē samutthāya bahirbhūya nirjanaṁ sthānaṁ gatvā tatra prārthayāñcakrē|
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
anantaraṁ śimōn tatsaṅginaśca tasya paścād gatavantaḥ|
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
taduddēśaṁ prāpya tamavadan sarvvē lōkāstvāṁ mr̥gayantē|
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
tadā sō'kathayat āgacchata vayaṁ samīpasthāni nagarāṇi yāmaḥ, yatō'haṁ tatra kathāṁ pracārayituṁ bahirāgamam|
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
atha sa tēṣāṁ gālīlpradēśasya sarvvēṣu bhajanagr̥hēṣu kathāḥ pracārayāñcakrē bhūtānatyājayañca|
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
anantaramēkaḥ kuṣṭhī samāgatya tatsammukhē jānupātaṁ vinayañca kr̥tvā kathitavān yadi bhavān icchati tarhi māṁ pariṣkarttuṁ śaknōti|
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
tataḥ kr̥pālu ryīśuḥ karau prasāryya taṁ spaṣṭvā kathayāmāsa
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
mamēcchā vidyatē tvaṁ pariṣkr̥tō bhava| ētatkathāyāḥ kathanamātrāt sa kuṣṭhī rōgānmuktaḥ pariṣkr̥tō'bhavat|
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
tadā sa taṁ visr̥jan gāḍhamādiśya jagāda
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
sāvadhānō bhava kathāmimāṁ kamapi mā vada; svātmānaṁ yājakaṁ darśaya, lōkēbhyaḥ svapariṣkr̥tēḥ pramāṇadānāya mūsānirṇītaṁ yaddānaṁ tadutsr̥jasva ca|
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
kintu sa gatvā tat karmma itthaṁ vistāryya pracārayituṁ prārēbhē tēnaiva yīśuḥ punaḥ saprakāśaṁ nagaraṁ pravēṣṭuṁ nāśaknōt tatōhētōrbahiḥ kānanasthānē tasyau; tathāpi caturddigbhyō lōkāstasya samīpamāyayuḥ|

< Marko 1 >