< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Rəbbee Cun cuvab İzraililqa, Malakiya peyğambarıle ğana hixhar ha'a.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Rəbbee «Zas şu vukkiykıninbıva» eyhe. Şossemee «Şi nəxübne vukkiykınva?» qiyghanas əxə. Rəbbeeyid inva eyhe: – Nya'a, Esav Yaaq'ubna çoc dişdiy vor? Zımee, Yaaq'ub ıkkanaalin şu, cuke g'abıynbı, g'əvxü,
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
Esaviy mang'uke g'abıynbımee, Zı əq'əna qav'u. Zı manbı vooxhen suvabı q'əra qa'as hassır, manbışde doyulin cigabı çaq'alaaşis huvu.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Edom vooxhene, Esavıke g'abıynbışisse eyhes əxə: – Şakın ıxheeyid, şi meed man hatq'ur-hiyxürin cigabı qa'asınbıcad. Saccu Xəəne G'oşunbışde Rəbbee inva vod eyhe: – Hasre, manbışe ale'ecencad, Zımee meed hı'ğəkkar ha'asın. Gırgıne gahbışil manbışde ölkayk'le g'ulyopt'ulna ölkava eyhes, coyub Rəbbina qəl avquyn millet xhinne qıvaats'as.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Şok'le man vuşdecad uleppışika g'acumee, şucad eyhes: «İzrailiked şaqana, Rəbbin do axtıda vod!»
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhen: – Ay Yizın do qizar hidya'an kaahinar! Duxee dekkıs, g'uleeyib cune iyesiys hı'rmat giviyxhe. Zı Dekxheene, nyavxha şu Zas giviyxhena hı'rmat? Zı İyesiyxhee meeb nyavxha şu Zas giviyxhena hı'rmat? Şosse «Nəxüdne şi Yiğın do qizar hidi'ıva?» qiyghanas əxə.
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
– Şu Yizde q'urbanbı allya'ane cigalqa kara idyalesın Zasın otxhuniy adı giyxhe. Mançikad, «Şi Vas dekkanan nəxüdne ha'ava?» qiyghan. Şu Rəbbin q'urbanbı allya'an ciga qizar hidi'ı, məxüd Mang'us dekkanan ha'a.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Şu bı'rq'ı'n həyvanar q'urbanna alli'iy yugunne vod? K'aana, vuk'arna həyvan q'urbanna ablyav'uy nya'a yugunne vod? Məxbına sa həyvan yiğne ölkayne xərıng'us hevle, ilekke mang'us ğu ikkiykanaseeva, mang'vee yiğna haa'asee? Məxüd Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhe!
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Həşde Allahıs düə hee'e, Mang'vee şos rəhı'm hee'ecen. Şu məxdın q'urbanbı allya'amee, Mana şoqa yugra eyxheye? Məxüd Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhe!
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Vuşde sang'vee, Yizde q'urbanbı allya'ane cigee, q'ərane cigeeqa ts'a gyoxhxhan ha'asse, Yizde xaan akkabıcad qı'iynxhiy yugda eyxheyiy! Yizın yik' şoka gyotxhan deş, şu allya'an q'urbanbıd alyaat'as deş! Məxüd Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhe!
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Verığ ılqəəne cigeençe, k'yooçene cigeeqamee, Yizın do milletbışde yı'q'nee axtıda vod! Gırgınəəng'ə Yizde doyule ətirbı gyoxhxhan ha'a, məttın paybı adayle! Man Yizın do milletbışde yı'q'nee, axtıda ıxhayke ha'a! Məxüd Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhe!
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
Şumee, «Rəbbine q'urbanbı allya'ane cigaylin otxhuniy muq'addasın deş vod, man qizar hide'eeyid eyxheva» uvhu, mançina muq'addasiyvalla avaak'an haa'a.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Ooğançe «İnimeena əq'übavad!» uvhu, şu mançilqa yı'q' sak'al ha'a! Məxüd Xəybışde Xərıng'vee Rəbbee eyhe! Şu Zas q'urbanna ablyaa'asva q'ööq'üna, k'aana, vuk'arna həyvan abeene, Zı mana şoke alyabat'aye? Məxüd Rəbbee eyhe!
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Syuruneençe g'apsırne yugne g'argıne cigee, Xudaavandays q'ı'bı'lyna həyvan abıyne horalays bed-düə vuxhena! Zı inekke xərna Paççahva, gırgıne milletbışe Yizın do axtı qa'a! Məxüd Xəəne G'oşunbışde Rəbbee eyhe!

< Malaki 1 >