< Malaki 1 >
1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Detta är den tunge, som Herren talade mot Israel, genom Malachi.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Jag hafver eder kär, säger Herren. Så sägen I: Hvarmed hafver du oss kär? Är icke Esau Jacobs broder? säger Herren. Likväl hafver jag Jacob kär;
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
Och jag hatar Esau, och hafver gjort hans berg öde, och hans arf drakomen till en öken.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Och om Edom säga ville: Vi äre förderfvade, dock vilje vi uppbygga igen det ödelagdt är; då säger Herren Zebaoth alltså: Om de bygga, så skall jag nederbryta; och det skall heta de fördömda landsändar och ett folk der Herren är vred uppå evinnerliga.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Det skola edor ögon se, och I skolen säga: Herren är härlig uti Israels landsändom.
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
En son skall hedra sin fader, och en tjenare sin herra. Är jag nu Fader, hvar är min heder? Är jag Herre, hvar fruktar man mig? säger Herren Zebaoth till eder, Presterna, som mitt Namn förakten. Så sägen I då: Hvarmed förakte vi ditt Namn?
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Dermed att I offren orent bröd uppå mitt altare. Så sägen I: Hvarmed offre vi dig något orent? Dermed, att I sägen: Herrans bord är intet aktandes.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Och när I offren något det blindt är, så måste det icke heta ondt; och när I offren något det halt är eller krankt, så måste det ock intet heta ondt. Bär det dinom Första; hvad gäller, om du skall täckas honom, eller om han vill se uppå din person? säger Herren Zebaoth.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Så bedjer nu Gud, att han ville vara oss nådelig; ty detta är skedt af eder. Menen I, att han skall se till edra person? säger I Herren Zebaoth.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Hvilken är ock ibland eder, den ena dörr tillycker? I tänden ock ingen eld uppå mitt altare omsyss. Jag hafver intet behag i eder, säger Herren Zebaoth; och spisoffer af edra händer är mig icke täckeligit.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Men af solenes uppgång allt intill nedergången skall mitt Namn härligit varda ibland Hedningarna; och i all rum skall mino Namne rökt, och ett rent spisoffer offradt varda; ty mitt Namn skall härligit varda ibland Hedningarna, säger Herren Zebaoth.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
Men I ohelgen det dermed, att I sägen: Herrans bord är oheligt, och dess offer är föraktadt, samt med sinom spis.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Och I sägen: Det är icke utan mödo; och slån det i vädret, säger Herren Zebaoth; och I offren det som röfvadt, halt och krankt är, och offren så spisoffer. Skulle sådant täckas mig ifrån edra hand? säger Herren.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Förbannad vare den bedragaren, den i sinom hjord hafver en Han; och när han gör ett löfte, så offrar han Herranom det som intet doger; ty jag är en stor Konung, säger Herren Zebaoth, och mitt Namn är förskräckeligit ibland Hedningarna.