< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
K A WANANA o ka olelo a Iehova i ka Iseraela ma o Malaki la.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Ua aloha aku au ia oukou, wahi a Iehova; Aka, ke ninau mai nei oukou, Ma ke aha la kau i aloha mai ai ia makou? Aole anei o Esau ka hoahanau o Iakoba? wahi a Iehova; Aka, i aloha aku au ia Iakoba,
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
A hoowahawaha hoi au ia Esau, A hooneoneo aku la au i kona mau mauna, A hoolilo iho la i kona aina i mau wahi noho o ka waonahele.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
No ka mea, ke olelo nei ko Edoma, Ua auhulihia kakou, Aka, e kukulu hou auanei kakou i na wahi neoneo: Penei ka Iehova o na kaua i olelo mai ai, E kukulu lakou, a e wawahi hoi au: E kapaia lakou, Na aina o ka aia, A o na kanaka a Iehova e inaina mau loa ai.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
A e ike auanei ko oukou mau maka, a e olelo aku oukou, E hoonuiia auanei o Iehova mai ka palena aku o Iseraela.
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
Ua hoomaikai ke keiki i kona makuakane, A o ke kauwa i kona haku: Ina hoi he makua wau, auhea la kuu hoomaikaiia? Ina hoi he haku wau, auhea la hoi kuu weliweliia? Wahi a Iehova o na kaua ia oukou, e na kahuna hoowahawaha i kuu inoa. Ke ninau mai nei oukou, Ma ke aha ka makou i hoowahawaha ai i kou inoa?
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Ke mohai mai nei oukou i ka berena haumia maluna o ko'u kuahu; Ke ninau mai nei oukou, Ma ke aha la ka makou i hoohaumia aku ai ia oe? Ma ka mea a oukou e olelo nei, He mea wahawaha ka papaaina o Iehova.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ina paha e kaumaha oukou i ka mea makapo i mea mohai, aole anei ia he hewa? Ina hoi e mohai oukou i ka mea oopa a me ka mea mai, aole anei he hewa ia? Ke i aku nei au, e haawi aku ia mea na kou alii, E oluolu mai anei ia ia oe? E maliu mai anei kela ia oe? wahi a Iehova o na kaua.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Nolaila hoi, ke nonoi aku nei oukou i ke Akua, e aloha mai oia ia kakou: No oukou aku ia mea; e maliu mai anei kela ia oukou? Wahi a Iehova o na kaua.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Owai la ka mea o oukou e pani wale i na puka? Aole oukou e kuni make hewa maluna o kuu kuahu. Aole au i oluolu ia oukou, wahi a Iehova o na kaua; Aole hoi e maliu au i ka mohai na ko oukou lima mai.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
No ka mea, mai ka hikina o ka la a hiki i ke komohana, E nui auanei kuu inoa iwaena o na lahuikanaka; A ma na wahi a pau loa e kuniia'i ka mea ala no kuu inoa, A me ka mohai maemae: No ka mea, e nui auanei kuu inoa iwaena o na lahuikanaka, Wahi a Iehova o na kaua.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
Aka, ua hoino oukou ia i ka oukou olelo ana, Ua haumia ka papaaina o Iehova, A o ka hua maluna, oia o kana ai, he mea hoowahawaha ia.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Ke olelo nei oukou, Ka! kai ka luhi! A na oukou ia i hoopailuaia'i, wahi a Iehova o na kaua; No ka mea, ke mohai iho nei oukou i ka mea i haehaeia, A me ka oopa, a me ka maimai, A pela oukou i lawe mai ai i ka mohai. E oluolu anei au i keia mea na ko oukou lima mai? wahi a Iehova.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Aka, auwe ka mea hoopunipuni, Ka mea nana ka hipakane maloko o kana ohana, Aka, ua hoolaa, a ua mohai iho i ka mea haumia: No ka mea, he alii nui hoi wau, wahi a Iehova o na kaua, A he mea weliweli ko'u inoa iwaena o na lahuikanaka.

< Malaki 1 >