< Malaki 1 >
1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Malheur accablant de la parole du Seigneur, adressée à Israël, par l’entremise de Malachie.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
Je vous ai aimés, dit le Seigneur, et vous avez dit: En quoi nous avez-vous aimés? Est-ce qu’Esaü n’était pas frère de Jacob? dit le Seigneur, et j’ai aimé Jacob;
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
Mais j’ai haï Esaü; et j’ai fait de ses montagnes une solitude, et j’ai abandonné son héritage aux dragons du désert.
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Que si l’Idumée dit: Nous avons été détruits, mais revenant nous bâtirons ce qui a été détruit: voici ce que dit le Seigneur des armées: Ceux-ci bâtiront, et moi je détruirai; et ils seront appelés bornes d’impiété et peuple contre qui le Seigneur s’est irrité jusqu’à jamais.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Et vos yeux verront, et vous direz: Que le Seigneur soit magnifié par delà les limites d’Israël.
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
Un fils honore son père et un serviteur son maître; si donc moi, je suis votre père, où est mon honneur? et si moi, je suis votre Seigneur, où est la crainte de moi? dit le Seigneur des armées, à vous, ô prêtres, qui méprisez mon nom, et qui dites: En quoi avons-nous méprisé votre nom?
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Vous offrez sur mon autel un pain souillé, et vous dites: En quoi vous avons-nous souillé? En ce que vous dites: La table du Seigneur est méprisée.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Si vous offrez un animal aveugle pour être immolé, n’est-ce pas un mal? et si vous en offrez un boiteux ou malade, n’est-ce pas un mal? offre-le à ton gouverneur pour voir s’il lui plaira, ou s’il accueillera ta face, dit le Seigneur des armées.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Et maintenant implorez la face du Seigneur, afin qu’il ait pitié de vous (car c’est par votre main que cela a été fait), pour voir si de quelque manière il accueillera vos faces, dit le Seigneur des armées.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
Qui est celui parmi vous qui ferme les portes de mon temple, et qui allume le feu sur mon autel gratuitement? mon affection n’est pas en vous, dit le Seigneur des armées, et je ne recevrai pas de présent de votre main.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Car, depuis le lever du soleil jusqu’à son coucher, grand est mon nom parmi les nations; et en tout lieu l’on sacrifie, et une oblation pure est offerte à mon nom, parce que grand est mon nom parmi les nations, dit le Seigneur des armées.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
Et vous l’avez souillé en ce que vous dites: La table du Seigneur est souillée; et ce qu’on pose dessus est méprisable, aussi bien que le feu qui le dévore.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Et vous avez dit: Voilà de notre travail, et vous avez soufflé dessus, dit le Seigneur des armées; et vous avez amené un animal boiteux et malade, fruit de vos rapines, et vous l’offrez en présent; est-ce que je le recevrai de votre main? dit le Seigneur.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
Maudit le fourbe qui a dans son troupeau un mâle, et qui faisant un vœu, immole un animal débile au Seigneur; parce que je suis le grand roi, dit le Seigneur des armées, et mon nom est terrible parmi les nations.