< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Une révélation, la parole de Yahvé à Israël par Malachie.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
« Je t'ai aimé », dit Yahvé. Pourtant, vous dites: « Comment nous avez-vous aimés? » « Esaü n'était-il pas le frère de Jacob? dit Yahvé, « J'ai aimé Jacob,
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
mais j'ai haï Esaü, j'ai fait de ses montagnes un désert, et j'ai donné son héritage aux chacals du désert. »
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
Alors qu'Édom dit: « Nous sommes abattus, mais nous reviendrons et nous rebâtirons les ruines », Yahvé des armées dit: « Ils bâtiront, mais je les renverserai; et on les appellera « le pays des méchants », le peuple contre lequel Yahvé manifeste sa colère à jamais. »
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Vos yeux verront et vous direz: « Yahvé est grand, même au-delà de la frontière d'Israël. »
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
« Un fils honore son père, et un serviteur son maître. Si je suis un père, où est mon honneur? Et si je suis un maître, où est le respect qui m'est dû? » dit Yahvé des armées à vous, prêtres, qui méprisez mon nom. Vous dites: « Comment avons-nous méprisé ton nom? »
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Vous offrez sur mon autel des pains souillés. Vous dites: Comment t'avons-nous pollué? En cela, vous dites: La table de Yahvé est méprisable.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Quand vous offrez un aveugle en sacrifice, n'est-ce pas un mal? Et quand vous offrez en sacrifice des boiteux et des malades, n'est-ce pas un mal? Présentez-le maintenant à votre gouverneur! Sera-t-il satisfait de vous? Ou bien acceptera-t-il votre personne? » dit Yahvé des Armées.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
« Implorez maintenant la faveur de Dieu, afin qu'il nous fasse grâce. Avec cela, acceptera-t-il l'un de vous? » dit Yahvé des Armées.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
« Oh, s'il y en avait un parmi vous qui fermât les portes, pour que vous n'allumiez pas en vain du feu sur mon autel! Je ne prends aucun plaisir en vous, dit Yahvé des armées, et je n'accepterai pas d'offrande de votre part.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Car, depuis le lever du soleil jusqu'à son coucher, mon nom est grand parmi les nations, et en tout lieu on offre à mon nom de l'encens et une offrande pure, car mon nom est grand parmi les nations, dit l'Éternel des armées.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
« Mais vous le profanez en disant: 'La table de l'Éternel est souillée, et son fruit, sa nourriture même, est méprisable'.
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Vous dites aussi: 'Voici, quelle fatigue c'est!'. Et vous l'avez reniflé, dit Yahvé des Armées, et vous avez apporté ce qui a été pris par violence, le boiteux et le malade; c'est ainsi que vous apportez l'offrande. Dois-je accepter cela de ta main? dit Yahvé.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
« Mais est maudit le trompeur qui a dans son troupeau un mâle, et qui fait des vœux et sacrifie à l'Éternel une chose défectueuse; car je suis un grand Roi, dit Yahvé des armées, et mon nom est redoutable parmi les nations. »

< Malaki 1 >