< Malaki 4 >
1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi.
Nebo aj, den ten přichází hořící jako pec, v němž budou všickni pyšní, a všickni pášící bezbožnost jako strniště. I zažhne je ten den, kterýž přijíti má, praví Hospodin zástupů, tak že neostaví jim ani kořene ani ratolesti.
2 Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola.
Vám pak, kteříž se bojíte jména mého, vzejde slunce spravedlnosti, a zdraví bude na paprslcích jeho. Tedy vycházeti budete, a porostete jako telata vykrmená.
3 Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
A pošlapáte bezbožné, tak že budou jako popel pod nohami vašimi v den, kterýž já učiním, praví Hospodin zástupů.
4 Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.
Pamatujtež na zákon Mojžíše služebníka mého, jemuž jsem přikázal na Orébě přednesti všemu Izraeli ustanovení a soudy.
5 “Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
Aj, já pošli vám Eliáše proroka, prvé nežli přijde den Hospodinův veliký a hrozný,
6 Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”
Aby obrátil srdce otců k synům, a srdce synů k otcům jejich, abych přijda, neranil země prokletím.