< Malaki 3 >

1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
Mira, estoy enviando a mi mensajero, y él preparará el camino delante de mí; y el Señor, a quién buscas, vendrá de repente a su Templo; y él mensajero del pacto, en quien se complacen, mira, él viene, dice el Señor de los ejércitos.
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
¿Pero por quién se puede enfrentar el día de su venida? ¿Y quién puede mantenerse en pie cuando lo vean? porque él es como el fuego del fundidor y el jabón del limpiador.
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
Él tomará asiento, fundirá y limpiará a los hijos de Leví, quemando el mal de ellos como refinando el oro y la plata; para que hagan ofrendas al Señor en justicia.
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
Entonces la ofrenda de Judá y Jerusalén agradará al Señor, como en días pasados, y como en años pasados.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
Y me acercaré a ti para juzgar; pronto seré testigo contra los hechiceros, contra los adúlteros, contra aquellos que juran en falso; contra aquellos que le impiden el pago al criado, y que oprimen a la viuda y al huérfano, que no le dan sus derechos al hombre extranjero y a los que no me temen, dice el Señor de ejércitos.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
Porque yo soy el Señor, no he cambiado; y ustedes, hijos de Jacob, no han sido cortados.
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
Desde los días de tus padres, han rechazado mis reglas y no las has guardado. Vuelve a mí y volveré a ti, dice el Señor de los ejércitos. Pero tú dices: ¿Cómo vamos a volver?
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
¿Se apartará un hombre de Dios de lo que es correcto? Pero has guardado lo que es mío. Pero tú dices: ¿Qué te hemos ocultado? Décimas y ofrendas.
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
Estás maldito con una maldición; porque me has ocultado lo que es mío, incluso toda esta nación.
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Deja que tus diezmos entren en el almacén para que haya comida en mi casa, y ponme a prueba al hacerlo, dice el Señor de los ejércitos, y mira si no hago las ventanas del cielo que se abran y enviaré tal bendición que no hay espacio para ello.
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Y por ustedes reprenderé al devorador para que no destruya los frutos de su tierra; y el fruto de su vid no será arrojada al campo antes de tiempo, dice el Señor de los ejércitos.
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Y serán nombrados bienaventurados por todas las naciones; porque serán una tierra deseable, dice el Señor de los ejércitos.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
Tus palabras han sido fuertes contra mí, dice el Señor. Y todavía dices: ¿Qué hemos dicho en tu contra?
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
Ustedes han dicho: No sirve de nada adorar a Dios: ¿qué beneficio hemos obtenido al cumplir sus órdenes y al vestirnos de luto ante el Señor de los ejércitos?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
Y ahora nos parecen felices los hombres orgullosos; sí, los malhechores están bien; ponen a Dios a prueba y están a salvo.
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Entonces aquellos en quienes estaba el temor del Señor hablaron entre sí; y el Señor dio oído, y fue registrado en un libro para ser tenido en cuenta delante de él, para aquellos que tenían el temor del Señor y para los que piensan en su nombre.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
Y serán míos, dice el Señor, en el día en que los haga mi tesoro especial; y tendré misericordia de ellos como un hombre tiene misericordia de su hijo que le sirve.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
Entonces verán de nuevo cómo el hombre recto es diferente del pecador y el siervo de Dios del que no lo es.

< Malaki 3 >