< Malaki 3 >
1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
“See, I am about to send my messenger, and he will prepare the way before me. Then the Lord, whom you seek, will suddenly come to his temple. The messenger of the covenant in whom you delight, see, he will come,” says Yahweh of hosts.
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
But who will be able to endure the day of his coming? Who will be able to stand when he appears? For he will be like a refiner's fire and like laundry soap.
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
He will sit as a refiner and purifier of silver, and he will purify the sons of Levi. He will refine them like gold and silver, and they will bring offerings of righteousness to Yahweh.
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
Then the offering of Judah and Jerusalem will be pleasing to Yahweh, as in the days of old, and as in ancient years.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
“Then I will approach you for judgment. I will quickly become a witness against the sorcerers, the adulterers, the false witnesses, and against those who oppress the hired worker in his wages, those who oppress the widow and the fatherless, against those who turn away the foreigner, and against those who do not honor me,” says Yahweh of hosts.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
“For I, Yahweh, have not changed; therefore you, sons of Jacob, have not come to an end.
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
From the days of your fathers you have turned aside from my ordinances and have not kept them. Return to me, and I will return to you,” says Yahweh of hosts. “But you say, 'How will we return?'
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
Would a person rob God? Yet you are robbing me. But you say, 'How have we robbed you?' In tithes and offerings.
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
You are cursed with a curse, for you are robbing me, the whole nation.
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Bring the full tithe into the storehouse, so that there may be food in my house, and test me now in this,” says Yahweh of hosts, “if I do not open to you the windows of heaven and pour out a blessing on you, until there is no more room for it all.
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
I will speak against those who destroy your crops, so that they do not destroy the harvest of your land. Your vines in the fields will not lose their fruit,” says Yahweh of hosts.
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
“All the nations will call you blessed, for you will be a land of delight,” says Yahweh of hosts.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
“Your words against me have been strong,” says Yahweh. “But you say, 'What have we said among ourselves against you?'
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
You have said, 'It is useless to serve God. What profit is it that we have kept his requirements or walked mournfully before Yahweh of hosts?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
So now we call the arrogant blessed. Evildoers not only prosper, but they even test God and escape.'”
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Then those who feared Yahweh spoke with one another. Yahweh paid attention and listened, and a book of remembrance was written before him about those who feared Yahweh and honored his name.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
“They will be mine,” says Yahweh of hosts, “my own treasured possession, on the day that I act. I will pity them, as a man pities his own son who serves him.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
Then once again you will distinguish between the righteous and the wicked, between one who worships God and one who does not worship him.