< Malaki 3 >
1 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
Se, jeg sender min Engel, og han skal bane Vej for mit Åsyn; og til sit Tempel kommer i et Nu den Herre, I søger, og Pagtens Engel, som I længes efter; se, han kommer, siger Hærskarers HERRE.
2 Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
Men hvo kan udholde den Dag, han kommer, og hvo kan stå, når han kommer til Syne? Han er jo som Metalsmelterens Ild og Tvætternes Lud.
3 Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
Han sidder og smelter og renser Sølv; han renser Levis Sønner, lutrer dem som Guld og Sølv, så de kan frembære Offergave for HERREN i Retfærdighed,
4 ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
at Judas og Jerusalems Offergave må være HERREN liflig som i fordums Dage, i henrundne År.
5 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
Jeg nærmer mig eder til Dom og vidner i Hast mod Troldmændene, Ægteskabsbryderne, Menederne og dem, som undertrykker Daglejere, Enker og faderløse, gør fremmede Uret og ikke frygter mig, siger Hærskarers HERRE.
6 “Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
Thi jeg, HERREN, er ikke blevet en anden, men I har ikke ophørt at være Jakobsønner".
7 Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
Siden eders Fædres Dage er I afveget fra mine Bud og har ikke holdt dem. Vend om til mig, så vil jeg vende om til eder, siger Hærskarers HERRE. Og I spørger: "Hvorledes skal vi vende os?"
8 “Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
Skal et Menneske bedrage Gud? I bedrager mig jo! Og I spørger:"Hvorved har vi bedraget dig?" Med Tienden og Offerydelsen!
9 Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
I trues med Forbandelse og bedrager dog mig, ja alt Folket gør det!
10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
Bring hele Tienden tiI Forrådshuset, så der kan være Mad i mit Hus; sæt mig på Prøve dermed, siger Hærskarers HERRE, om jeg da ikke åbner eder Himmelens Sluser og udøser Velsignelse over eder i Overmål.
11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Jeg vil for eders Skyld skræmme Æderne, så at de ikke ødelægger eder Landets Afgrøde, og Vinstokken på Marken skal ikke slå eder fejl, siger Hærskarers HERRE.
12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Og alle Folkene skal love eder, fordi l har et yndigt Land, siger Hærskarers HERRE.
13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
I taler stærke Ord imod mig, siger HERREN. Og I spørger: "Hvad taler vi imod dig?"
14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
I siger: "Det er ørkesløst at tjene Gud; hvad vinder vi ved at opfylde hans Krav og gå sørgeklædte for Hærskarers HERREs Åsyn?
15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
Nej, vi må love de frække! De øver Gudløshed og kommer til Vejrs; de frister Gud og slipper godt derfra."
16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
Da talte de, som frygter HERREN, med hverandre. Og HERREN lyttede og hørte efter, og en Bog blev skrevet for hans Åsyn, for at de kunde ihukommes, som frygter HERREN og slår Lid til hans Navn.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
Den Dag jeg griber ind, skal de tilhøre mig som mit Eje, siger Hærskarers HERRE, og jeg vil handle nænsomt med dem, som en Fader handler nænsomt med sin Søn, der tjener ham.
18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”
Da skal l atter kende Forskel på retfærdig og gudløs, på den, som tjener Gud, og den, som ikke tjener ham.