< Malaki 2 >
1 “Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
Maintenant c'est à vous, sacrificateurs, que s'adresse ce commandement.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
Si vous n'écoutez pas, et si vous ne prenez pas à cœur de donner gloire à mon nom, a dit l'Éternel des armées, j'enverrai sur vous la malédiction, et je maudirai vos bénédictions. Oui, je les maudirai, parce que vous ne le prenez point à cœur.
3 “Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
Voici, je détruirai vos semences, et je répandrai sur vos visages de la fiente, la fiente de vos victimes de fêtes; et on vous emportera avec elle.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
Et vous saurez que je vous ai envoyé ce commandement, afin qu'il soit mon alliance avec Lévi, dit l'Éternel des armées.
5 Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
Mon alliance avec lui était la vie et la paix, et je les lui donnai pour qu'il eût de la crainte; et il me craignit, et il trembla devant mon nom.
6 Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
La loi de vérité était dans sa bouche, et il ne s'est point trouvé de perversité sur ses lèvres. Il a marché avec moi dans la paix et dans la droiture, et il en a détourné plusieurs de l'iniquité.
7 “Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
Car les lèvres du sacrificateur doivent garder la science, et de sa bouche on recherche la loi; car il est le messager de l'Éternel des armées.
8 Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Mais vous, vous vous êtes écartés de cette voie; vous en avez fait broncher plusieurs par votre enseignement; vous avez violé l'alliance de Lévi, dit l'Éternel des armées.
9 “Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
Et moi aussi, je vous ai rendus méprisables et abjects à tout le peuple, parce que vous ne gardez pas mes voies, et que vous avez égard à l'apparence des personnes en appliquant la loi.
10 Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
N'avons-nous pas tous un même père? Un même Dieu ne nous a-t-il pas créés? Pourquoi donc sommes-nous perfides l'un envers l'autre, en profanant l'alliance de nos pères?
11 Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
Juda agit perfidement, et une abomination est commise en Israël et à Jérusalem; car Juda profane ce qui est consacré à l'Éternel, ce qu'il aime, et il épouse la fille d'un dieu étranger.
12 Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
L'Éternel retranchera des tentes de Jacob l'homme qui fait cela, celui qui veille, et celui qui répond, et celui qui présente l'offrande à l'Éternel des armées.
13 China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
Et voici une seconde chose que vous faites: vous couvrez de larmes l'autel de l'Éternel, de pleurs et de gémissements, de sorte qu'il ne regarde plus à l'offrande, et ne prend plus plaisir à ce qui vient de vos mains.
14 Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
Et vous dites: “Pourquoi? “Parce que l'Éternel a été témoin entre toi et la femme de ta jeunesse, à laquelle tu es infidèle, bien qu'elle soit ta compagne et la femme de ton alliance.
15 Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
Personne n'a fait cela, ayant un reste d'esprit. Et pourquoi le seul (Abraham) l'a-t-il fait? Il cherchait une postérité de Dieu. Prenez donc garde à votre esprit, et qu'il n'y ait pas d'infidélité envers la femme de ta jeunesse.
16 Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
Car je hais la répudiation, dit l'Éternel, le Dieu d'Israël, et celui qui couvre de violence son vêtement, dit l'Éternel des armées. Prenez donc garde à votre esprit, et ne soyez pas infidèles.
17 Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”
Vous fatiguez l'Éternel par vos paroles, et vous dites: “En quoi le fatiguons-nous? “C'est en disant: Quiconque fait le mal est bon aux yeux de l'Éternel, et c'est en eux qu'il prend plaisir; ou bien: Où est le Dieu de la justice?