< Malaki 2 >

1 “Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
And now, A! ye preestis, this maundement is to you.
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
If ye wolen here, and if ye `wolen not putte on the herte, that ye yyue glorie to my name, seith the Lord of oostis, Y schal sende nedynesse in to you, and Y schal curse to youre blessyngis; and Y schal curse hem, for ye han not putte on the herte.
3 “Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
Lo! Y schal caste to you the arm, and Y schal scatere on youre cheere the drit of youre solempnytees, and it schal take you with it.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
And ye schulen wite, that Y sente to you this maundement, that my couenaunt were with Leuy, seith the Lord of oostis.
5 Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
My couenaunt was with hym of lijf and pees; and Y yaf to hym a drede, and he dredde me, and he dredde of face of my name.
6 Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
The lawe of trewthe was in his mouth, and wickidnesse was not foundun in hise lippis; in pees and in equite he walkide with me, and he turnede awei many men fro wickidnesse.
7 “Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
For the lippis of a prest kepen science, and thei schulen ayen seke the lawe of `the mouth of hym, for he is an aungel of the Lord of oostes.
8 Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
But ye wenten awei fro the weie, and sclaundren ful many men in the lawe; ye maden voide the couenaunt of Leuy, seith the Lord of oostis.
9 “Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
For which thing and Y yaf you worthi to be dispisid, and bowen to alle puplis, as ye kepten not my weies, and token a face in the lawe.
10 Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
Whether not o fadir is of alle you? whether o God made not of nouyt you? Whi therfor ech of you dispisith his brother, and defoulith the couenaunt of youre fadris?
11 Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
Judas trespasside, and abhomynacioun is maad in Israel, and in Jerusalem; for Judas defoulide the halewyng of the Lord, which he louyde, and he hadde the douyter of an alien god.
12 Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
The Lord schal distrie the man that dide this thing, the maister and disciple, fro the tabernacle of Jacob, and him that offrith a yifte to the Lord of oostis.
13 China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
And eftsoone ye diden this thing; ye hiliden with teeris the auter of the Lord, with wepyng and mourenyng; so that Y biholde no more to sacrifice, nether resseyue ony thing plesaunt of youre hond.
14 Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
And ye seiden, For what cause? For the Lord witnesside bitwixe thee and the wijf of thi `puberte, that is, tyme of mariage, which thou dispisidist, and this is thi felowe, and wijf of thi couenaunt.
15 Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
Whether oon made not, and residue of spirit is his? and what sekith oon, no but the seed of God? Therfore kepe ye youre spirit, and nyle thou dispise the wijf of thi yongthe;
16 Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
whanne thou hatist hir, leue thou hir, seith the Lord God of Israel. Forsothe wickidnesse schal kyuere the closyng of hym, seith the Lord of oostis; kepe ye youre spirit, and nyle ye dispise.
17 Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”
Ye maden the Lord for to trauele in youre wordis, and ye seiden, Wherynne maden we hym for to trauele? In that that ye seien, Ech man that doith yuel, is good in the siyt of the Lord, and siche plesen to hym; ether certis where is the God of doom?

< Malaki 2 >