< Luka 9 >

1 Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda.
Il convoqua les douze et leur donna le pouvoir de vaincre tous les démons et de guérir les maladies.
2 Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala.
Il les envoya prêcher le Royaume de Dieu et guérir les malades.
3 Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera.
Il leur dit: « Ne prenez rien pour votre voyage: ni bâton, ni portefeuille, ni pain, ni argent. N'ayez pas deux tuniques chacun.
4 Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo.
Dans quelque maison que vous entriez, restez-y, et sortez de là.
5 Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.”
Tous ceux qui ne vous recevront pas, en sortant de cette ville, secouez même la poussière de vos pieds, en témoignage contre eux. »
6 Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.
Ils partirent et parcoururent les villages, prêchant la Bonne Nouvelle et guérissant partout.
7 Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa,
Hérode, le tétrarque, apprit tout ce qu'il avait fait, et il fut très troublé, parce que les uns disaient que Jean était ressuscité des morts,
8 ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.
les autres qu'Élie était apparu, et d'autres encore qu'un des anciens prophètes était ressuscité.
9 Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.
Hérode dit: « J'ai décapité Jean, mais qui est celui-ci, dont j'entends dire tant de choses? » Il chercha à le voir.
10 Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida.
Les apôtres, à leur retour, lui racontèrent ce qu'ils avaient fait. Il les prit et se retira à l'écart, dans un endroit désert, dans une ville appelée Bethsaïda.
11 Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.
Mais la foule, s'en apercevant, le suivit. Il les accueillit, leur parla du Royaume de Dieu, et il guérit ceux qui avaient besoin d'être guéris.
12 Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”
Le jour commençait à baisser; les douze vinrent lui dire: « Renvoie la foule, afin qu'elle aille dans les villages et les fermes d'alentour, qu'elle se loge et se procure de la nourriture, car nous sommes ici dans un lieu désert. »
13 Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.” Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.”
Mais il leur dit: « Vous leur donnez à manger. » Ils dirent: « Nous n'avons pas plus de cinq pains et deux poissons, à moins que nous n'allions acheter de la nourriture pour tous ces gens. »
14 (Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000). Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.”
Car ils étaient environ cinq mille hommes. Il dit à ses disciples: « Faites-les s'asseoir par groupes d'environ cinquante chacun. »
15 Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi.
Ils firent ainsi, et les firent tous s'asseoir.
16 Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu.
Il prit les cinq pains et les deux poissons, et, levant les yeux au ciel, il les bénit, les rompit et les donna aux disciples pour qu'ils les présentent à la foule.
17 Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.
Ils mangèrent et furent tous rassasiés. Ils ramassèrent les douze paniers de morceaux qui restaient.
18 Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
Comme il priait seul, les disciples étaient près de lui, et il leur demanda: « Qui les foules disent-elles que je suis? »
19 Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”
Ils répondirent: « Jean le Baptiseur, mais d'autres disent: Élie, et d'autres encore, qu'un des anciens prophètes est ressuscité. »
20 Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”
Il leur dit: « Mais qui dites-vous que je suis? » Pierre répondit: « Le Christ de Dieu. »
21 Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi.
Mais il les avertit et leur ordonna de ne le dire à personne,
22 Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”
en disant: « Il faut que le Fils de l'homme souffre beaucoup, qu'il soit rejeté par les anciens, les principaux sacrificateurs et les scribes, qu'il soit tué, et qu'il ressuscite le troisième jour. »
23 Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine.
Il dit à tous: « Si quelqu'un veut venir après moi, qu'il renonce à lui-même, qu'il se charge de sa croix, et qu'il me suive.
24 Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa.
Car quiconque veut sauver sa vie la perdra, mais quiconque perdra sa vie à cause de moi la sauvera.
25 Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini?
En effet, que sert à un homme de gagner le monde entier, s'il se perd ou se renie lui-même?
26 Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera.
Car quiconque aura honte de moi et de mes paroles, le Fils de l'homme aura honte de lui, quand il viendra dans sa gloire, et dans la gloire du Père et des saints anges.
27 Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”
Mais je vous dis la vérité: parmi ceux qui se tiennent ici, il en est qui ne goûteront nullement à la mort avant d'avoir vu le Royaume de Dieu. »
28 Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera.
Environ huit jours après ces paroles, il prit avec lui Pierre, Jean et Jacques, et monta sur la montagne pour prier.
29 Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri.
Pendant qu'il priait, l'aspect de son visage se modifia, et ses vêtements devinrent blancs et éblouissants.
30 Anthu awiri, Mose ndi Eliya,
Et voici que deux hommes s'entretenaient avec lui, qui étaient Moïse et Élie,
31 anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu.
lesquels apparurent dans la gloire et parlèrent de son départ, qu'il allait accomplir à Jérusalem.
32 Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye.
Or Pierre et ceux qui étaient avec lui étaient accablés de sommeil; mais, lorsqu'ils furent pleinement réveillés, ils virent sa gloire et les deux hommes qui se tenaient avec lui.
33 Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).
Comme ils se séparaient de lui, Pierre dit à Jésus: « Maître, il est bon pour nous d'être ici. Faisons trois tentes: une pour toi, une pour Moïse et une pour Élie », sans savoir ce qu'il disait.
34 Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta.
Comme il disait cela, une nuée vint les couvrir, et ils eurent peur en entrant dans la nuée.
35 Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.”
Une voix sortit de la nuée, disant: « Celui-ci est mon Fils bien-aimé. Écoutez-le! »
36 Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.
Lorsque la voix se fit entendre, Jésus fut trouvé seul. Ils gardèrent le silence, et ne racontèrent à personne, en ce temps-là, ce qu'ils avaient vu.
37 Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye.
Le lendemain, lorsqu'ils descendirent de la montagne, une grande foule vint à sa rencontre.
38 Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu.
Et voici qu'un homme de la foule s'écrie: « Maître, je te prie de regarder mon fils, car c'est mon unique enfant.
39 Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga.
Voici qu'un esprit le saisit, qu'il crie soudain, qu'il le convulse au point de le faire écumer, et qu'à peine sorti de lui, il le meurtrit gravement.
40 Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”
J'ai supplié tes disciples de le chasser, et ils n'ont pas pu. »
41 Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”
Jésus répondit: « Génération incrédule et perverse, jusqu'à quand serai-je avec vous et vous supporterai-je? Amène ton fils ici. »
42 Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake.
Comme il s'approchait encore, le démon le jeta à terre et le convulsa violemment. Mais Jésus menaça l'esprit impur, guérit le garçon et le rendit à son père.
43 Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu. Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake,
Ils étaient tous étonnés de la majesté de Dieu. Comme tous s'émerveillaient de toutes les choses que Jésus faisait, il dit à ses disciples:
44 “Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”
« Laissez pénétrer ces paroles dans vos oreilles, car le Fils de l'homme sera livré aux mains des hommes. »
45 Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.
Mais ils ne comprirent pas cette parole. Elle leur était cachée, afin qu'ils ne la perçoivent pas, et ils avaient peur de l'interroger sur cette parole.
46 Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo.
Une dispute s'éleva parmi eux pour savoir lequel d'entre eux était le plus grand.
47 Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake.
Jésus, connaissant le raisonnement de leurs cœurs, prit un petit enfant, le plaça à ses côtés,
48 Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”
et leur dit: « Quiconque reçoit ce petit enfant en mon nom me reçoit. Et celui qui me reçoit reçoit celui qui m'a envoyé. Car celui qui est le plus petit parmi vous tous, celui-là sera grand. »
49 Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”
Jean répondit: « Maître, nous avons vu quelqu'un qui chasse les démons en ton nom, et nous le lui avons interdit, parce qu'il ne nous suit pas. »
50 Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”
Jésus lui dit: « Ne l'empêche pas, car celui qui n'est pas contre nous est pour nous. »
51 Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu,
Comme les jours où il devait être enlevé étaient proches, il se disposa à aller à Jérusalem
52 ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira,
et envoya des messagers devant lui. Ils allèrent et entrèrent dans un village des Samaritains, afin de se préparer à le recevoir.
53 koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu.
Ils ne le reçurent pas, parce qu'il voyageait le visage tourné vers Jérusalem.
54 Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?”
Voyant cela, ses disciples, Jacques et Jean, dirent: « Seigneur, veux-tu que nous ordonnions au feu de descendre du ciel et de les détruire, comme l'a fait Élie? »
55 Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula,
Mais il se retourna et les réprimanda: « Vous ne savez pas de quel esprit vous êtes.
56 ndipo iwo anapita ku mudzi wina.
Car le Fils de l'homme n'est pas venu pour détruire la vie des hommes, mais pour les sauver. » Ils se rendirent dans un autre village.
57 Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”
Comme ils continuaient leur chemin, un homme lui dit: « Je veux te suivre partout où tu iras, Seigneur. »
58 Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”
Jésus lui dit: « Les renards ont des trous et les oiseaux du ciel des nids, mais le Fils de l'homme n'a pas où reposer sa tête. »
59 Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.” Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”
Il dit à un autre: « Suis-moi! » Mais il a dit: « Seigneur, permets-moi d'aller d'abord enterrer mon père. »
60 Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”
Mais Jésus lui dit: « Laisse les morts enterrer leurs propres morts, mais toi, va annoncer le Royaume de Dieu. »
61 Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”
Un autre dit aussi: « Je veux te suivre, Seigneur, mais permets-moi d'abord de dire au revoir à ceux qui sont chez moi. »
62 Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”
Mais Jésus lui dit: « Personne, ayant mis la main à la charrue et regardant en arrière, n'est apte au Royaume de Dieu. »

< Luka 9 >