< Luka 8 >

1 Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
Hanchu, môrkhat suole chu, Jisua'n Galilee ram khopuingei le khuongei nâma Pathien Rêngram Thurchi Sa misîrin a chaia. Ruoisi sômleinik ngeiin an jûia.
2 komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
Nupang senkhat ramkhori sûr renga an natnangeia a dam, Mary Magdalene, a sûng renga ramkhori sari a rujûlpai pe,
3 Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
Herod office'a sin milien Chuza lômnu Joanna ngei, Susanna ngei, le midang nupang tamtak ngeiin an jûi saa. Hi mingei hin an sumin Jisua le a ruoisingei an san ngei ngâi ani.
4 Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
Khopui ankhat renga adanga mipuingei Jisua kôm an hong intûpkhôma, Jisua'n chongmintêkin a ril ngeia.
5 “Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
Mi inkhat a bu rît rangin a loilâia a sea. Sachi a rethea, senkhat lampui kôla achula, vangeiin an sâk ripa.
6 Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
Senkhat lungpherpha pil chunga achula, a hong mônga, pil an zit loi sikin a rôp nôk ripa.
7 Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
Senkhat chu riling kâra achula, ahong thuora, rilingin adîp thata.
8 Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
Senkhat chu pil sana achula, a hong insôna, abâk raza chitin an hong inra zoi. Hanchu hi chongngei hih a rila, Jisua'n, Kuor nin dônin chu rangâi roi, a tipe ngeia.
9 Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
A ruoisingeiin hi chongmintêk omtie, Jisua an rekela.
10 Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
Jisua'n, “Pathien Rêngram chong inthup riettheina nin kôma ipêk ani. Ania midangngei rangin chu, an ena an mu loina rang le an rangâia an rietminthâr loina rangin, chongmintêk vaiin misîr pe rang ani” tiin a thuon ngeia.
11 “Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
“Chongmintêk omtie chu hi anghin ani; Sachi chu Pathien chong ani.
12 Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
Sachi lampui kôla chul chu, chong chu an rieta, ania, an iem loina rang le minringa an om loina rangin Soitanin an chong riet hah an mulungrîl renga a lâk pe ngâia.
13 Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
Lung chung pila chul chu, an chong riet râisân takin an poma, nikhomrese, an nia han rujung inthuk nei loiin, an chunga minsinna a hongtung tena chu an inlet nôk ngâia.
14 Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
Riling kâra chul chu, chong an rieta, aniatachu, hi ringnun hoiinhâina le inchongna ngei hin lungkâng a pêka, adîpa, amara reng min phâk ngâi mak.
15 Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
Pil sana chul chu, chong an riet hah mulungrîla asadimin an dara, an jôma, an inra mâka dier ngei hah anni” a tia.
16 “Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
Tutên châti mochokin bêl nuoia dar ngâi mak ngei, jâlmun nuoia khom dar ngâi mak ngei. A lût murdi'n an mu theina rangin a darna muna kêng an dar ngâi.
17 Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
Ânthup murdi khom tâng minsuok nîng a ta, ihîpa om murdi khom avâra la minlangsuok nîng atih.
18 Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
“Singthei roi, inmo nin rangâi, asikchu, a dônngei chu bôkpe sa nîng a ta, a dônloi chu a dôn vieta ai mindon te ha khom la lâk pe rip an tih,” a tia.
19 Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
Hanchu, a nû le a lâibungngei Jisua kôma an honga, ania mipui sikin a kôma tung thei mak ngeia.
20 Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
Mi inkhatin, “Na nû le na lâibungngeiin nang mu nuomin pêntieng an inding” a tipea.
21 Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
Hanchu, Jisua'n an kôma, “Ka nû le ka lâibungngei chu Pathien chong rangâia a jômngei hih anni” a tia.
22 Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
Sûnkhat chu Jisua le a ruoisingei rukuonga an chuonga, “Dîl râl tieng son lenkân rei u” a tia, hanchu an inphêta.
23 Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
Hanchu an se lâiin, Jisua chu a ina. Inningloiin phâivuopui a hong thoa, an rukuong tuiin a sip vavânga, rolo innîkin an oma.
24 Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
Hanchu, ruoisingei Jisua kôma an sea, an kaithoia, “Minchupu, Minchupu! Kin thi suo rang kêng ani zoi” an tia. Hanchu, Jisua ânthoia, Phâivuopui le tuidârinsok hah chong a pêka, an dâiruom zoia.
25 Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
Hanchu, a ruoisingei kôma, “Khonmo, nan taksônna a om?” a tipe ngeia. Kamâmin an chia, Khoi anga miriem mo hi? Phâivuopui le tuidârinsokngei khom chong a pêka a chong an ijôm hi, anin tia.
26 Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
Hanchu Jisua le a ruoisingei hah Galilee dîl râl, Gerasa, ram an tunga.
27 Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
Jisua'n tuipânga a lôn lehan, khopui renga mi inkhat, ramkhori sûr ân tongpuia. Ha mi hah zora sôttak renga, dierboiin, ina khom om ngâi loiin thâna lei om ngâi ania.
28 Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
Jisua a mûn chu ânieka, a ke bula ânboka, ânring takin, Jisua Pathien Ânchungtak Nâipasal, imo ni lo rang ni ti? Dûk ni mintong no roh, tiin a ngêna.
29 Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
Jisua'n ratha innim hah chong a pêk sika ma angtaka ai ti ani. Vêl tamtak an sûra, lung ina an khum ngâia, a kut le a ke zingjirûiin an khita chu a potsata, ramkhori han ramchâr tieng han a rujûl ngâi ani.
30 Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
Jisua'n, “Imo ni riming?” tiin a rekela, “Ki riming chu, Mob” tiin a thuona, a sûnga ramkhori tamtak an lût sikin.
31 Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos g12)
Hanchu, ramkhoringei han, khurmongboia tîr loina rangin Jisua an ngêna. (Abyssos g12)
32 Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
Hanchu, ha muol panga han vok pâl sâk rokin an oma, ramkhoringeiin ha vokngei sûnga lût rangin Jisua an ngêna, a phalpe ngeia.
33 Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
Mipa sûng renga an jôka, vokngei sûnga an lût zoia. Rôlsôr dîl rakhama an tâna, tuia an tâka an thi let zoi.
34 Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
Hanchu, vok avâipungei han neinun omtie an rietin chu, an sea khopuia le loia mingei an va ril ngeia.
35 Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
Hanchu, neinun omtie en rangin mingei an suoka, Jisua kôm an hongin chu, ramkhori sûrpu hah, puon silin, ruthuok kipin Jisua ke bula insungin an mua, an rêngin an chia.
36 Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
Hanchu, amu nâmin a dam tie mingei kôma an rila,
37 Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
Ha Gerasa rama mingei han an chi sikin Jisua hah an kôm renga rot rangin an ngêna, hanchu Jisua rukuonga a chuonga a mâk ngei zoi.
38 Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
Ramkhori a sûng renga a jôka a dampu han, Jisua kôm nang jûi ki tih, a tia.
39 “Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
Hanniresea, Jisua'n, “Ni ina senla, nu chunga Pathien sintho tie va misîr roh” a tipea. Hanchu, a sea, khopui sûng pumpuia a chunga Jisua sintho tie hah a misîr zoi.
40 Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
Hanchu, Jisua dîl râl tieng a hongtung nôkin chu, mipuingei ama lei ngak sikin an lei modôma.
41 Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
Ha khuoa synagog ruoipu Jairus a honga, Jisua ke bula ânboka, a ina se rangin a ngêna.
42 chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
A nâikhât nâinupang, kum sômleinik mi, a thi vavâng sikin. Hanchu, Jisua a sên chu mipuingeiin an ûmhura.
43 Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
Nupang inkhat kum sômleinik piel, hulloi inrik a oma, ai dôn murdi doctora a thâm let zoia, tute lakin mindam thei mak ngeia.
44 Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
Mipuingei kâra Jisua nûktieng a honga, a puonmor a tôna, harenghan a dam kelena.
45 Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
Jisua'n, “Tumo ni tôn?” a tia. Kei chu ni mu-ung an ti chita. Hanchu Peter'n a kôma, “Minchupu, hi dôra mipuiin nang an uop hite” a tipea.
46 Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
Ania, Jisua'n “tuminin chu min tôn, Keima renga sinthotheina ajôk” a tia.
47 Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
Nupangnu ani ti rietsuok ani zoi, ti ânriet tena chu, innîk pumin mipuingei makunga, Jisua ke bula inbokin, a tôna harenghan a dam kelen roi hah misîr zoi.
48 Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
Hanchu, Jisua'n a kôma, “Ka nâinupang, na taksônnân nang a mindam zoi, rathanngam takin se ta roh” a tipea.
49 Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
Jisua'n ha a ti lâitakin, ruoipu in renga thangthei a honga, Jairus kôma, “Na nâinupang a thi zoi, Minchupu jêl khâi no roh” a tia.
50 Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
Jisua'n a rieta, Jairus kôma, “Chino roh, iem ngit roh, dam a tih,” a tipea.
51 Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
In ava tungin chu Peter, John, Jacob, nâite nû le pa pêna chu tute dang a kôma lût phal maka.
52 Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
Hataka om murdi nâite chûlin an chapa, Jisua'n, “Chap no roi, athi ni mak, a in kêng” a tia.
53 Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
Hanchu, nâite hah a thi ani iti an riet sikin an munuisana.
54 Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
Hanchu, Jisua'n a kut a sûra, “Ka nâite, hong inthoi roh” a tia.
55 Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
Hanchu, a ringna a juong kîra, harenghan a hon thoia, Jisua'n “sâk rang imokhat pêk roi” a tia.
56 Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.
A nû le a pa'n kamâm om an ti tataka; nikhomrese, Jisua'n chu a sintho hah tute ril loi rangin chong a pêka zoi.

< Luka 8 >